2 Mbiri 14 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 14:1-15

1Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.

Asa Mfumu ya Yuda

2Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake. 3Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera. 4Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake. 5Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake. 6Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.

7Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.

8Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.

9Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa. 10Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.

11Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”

12Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa, 13ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo. 14Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko. 15Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.

Thai New Contemporary Bible

2พงศาวดาร 14:1-15

1และอาบียาห์ทรงล่วงลับไปอยู่กับบรรพบุรุษและถูกฝังไว้ในเมืองดาวิด แล้วอาสาโอรสของพระองค์ขึ้นครองราชย์แทน ในรัชกาลของพระองค์แผ่นดินสงบสุขอยู่สิบปี

กษัตริย์อาสาแห่งยูดาห์

(1พกษ.15:11-12)

2อาสาทรงทำสิ่งที่ดีงามและถูกต้องในสายพระเนตรของพระยาห์เวห์พระเจ้าของพระองค์ 3ทรงรื้อแท่นบูชาของชนต่างด้าวและสถานบูชาบนที่สูงทั้งหลาย ทรงทุบหินศักดิ์สิทธิ์และโค่นเสาเจ้าแม่อาเชราห์14:3 คือ สัญลักษณ์ของเจ้าแม่อาเชราห์ เช่นเดียวกับที่อื่นๆ ใน 2พงศาวดารทิ้ง 4พระองค์ทรงบัญชาชนยูดาห์ให้แสวงหาพระยาห์เวห์พระเจ้าของบรรพบุรุษของพวกเขา และเชื่อฟังบทบัญญัติและพระบัญชาของพระเจ้า 5พระองค์ทรงรื้อสถานบูชาบนที่สูงทั้งหลายกับแท่นเผาเครื่องหอมออกจากทุกเมืองของยูดาห์ ราชอาณาจักรสงบสุขภายใต้การปกครองของพระองค์ 6พระองค์ได้ทรงสร้างเมืองป้อมปราการต่างๆ ของยูดาห์เพราะแผ่นดินสงบสุข ไม่มีข้าศึกมาสู้รบในช่วงนั้น เพราะองค์พระผู้เป็นเจ้าประทานการพักสงบแก่พระองค์

7อาสาตรัสกับชนยูดาห์ว่า “ให้เราสร้างเมืองเหล่านี้ ก่อกำแพงรอบ มีหอคอย ประตู และดาล ดินแดนยังเป็นของเรา เพราะเราแสวงหาพระยาห์เวห์พระเจ้าของเรา พระองค์จึงทรงให้เรามีความสงบสุขรอบด้าน” พวกเขาก็ลงมือทำและเจริญรุ่งเรือง

8กองทัพของอาสามีกำลังจากยูดาห์ 300,000 คนถือโล่ใหญ่กับหอก และจากเบนยามิน 280,000 คนถือโล่เล็กกับธนู คนเหล่านี้ล้วนเป็นนักรบแกล้วกล้า

9เศราห์ชาวคูชยกทัพใหญ่มหึมา14:9 ภาษาฮีบรูว่าด้วยกองทัพนับแสนหรือด้วยกองทัพนับพันและมีรถม้าศึกสามร้อยคัน รุกมาถึงเมืองมาเรชาห์ 10อาสาออกมาประจันหน้า ตั้งแนวรบที่หุบเขาเศฟาธาห์ใกล้มาเรชาห์

11อาสาทูลพระยาห์เวห์พระเจ้าของพระองค์ว่า “ข้าแต่องค์พระผู้เป็นเจ้า ไม่มีใครอื่นเสมอเหมือนพระองค์ที่จะช่วยผู้ไร้กำลังต่อกรกับผู้มีอำนาจ ข้าแต่พระยาห์เวห์พระเจ้าของข้าพระองค์ทั้งหลาย ขอทรงช่วยเพราะข้าพระองค์ทั้งหลายพึ่งในพระองค์ และข้าพระองค์ทั้งหลายมาต่อสู้กองทัพมหึมานี้ในพระนามของพระองค์ ข้าแต่องค์พระผู้เป็นเจ้า พระองค์ทรงเป็นพระเจ้าของเหล่าข้าพระองค์ ขออย่าให้มนุษย์ชนะพระองค์เลย”

12องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงปราบชาวคูชต่อหน้าอาสากับยูดาห์ ชาวคูชถอยหนีไป 13และอาสากับกองทัพรุกไล่พวกเขาไปไกลถึงเกราร์ ชาวคูชล้มตายมากมายจนไม่อาจฟื้นตัวได้อีก พวกเขาแหลกลาญไปต่อหน้าองค์พระผู้เป็นเจ้ากับกองกำลังของพระองค์ ชนยูดาห์นำของเชลยจำนวนมากกลับมา 14พวกเขาทำลายล้างหมู่บ้านทั้งปวงรอบเกราร์เพราะความกลัวขององค์พระผู้เป็นเจ้าอยู่เหนือพวกนั้น พวกเขาริบข้าวของทั่วหมู่บ้านเหล่านั้น เนื่องจากมีของเชลยมากมายที่นั่น 15พวกเขายังโจมตีค่ายของคนเลี้ยงสัตว์ และกวาดต้อนแกะ แพะ อูฐ กลับมายังกรุงเยรูซาเล็มด้วย