2 Mbiri 14 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 14:1-15

1Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.

Asa Mfumu ya Yuda

2Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake. 3Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera. 4Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake. 5Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake. 6Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.

7Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.

8Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.

9Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa. 10Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.

11Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”

12Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa, 13ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo. 14Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko. 15Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

歷代志下 14:1-15

亞撒王擊敗古實人

1亞比雅與祖先同眠後,葬在大衛城中,他兒子亞撒繼位。亞撒執政期間,國中太平十年。 2亞撒做他的上帝耶和華看為好、視為正的事, 3拆除外族神明的邱壇和神廟,打碎神柱,砍倒亞舍拉神像, 4命令猶大人尋求他們祖先的上帝耶和華,遵行祂的律法和誡命。 5他除掉猶大各城邑的邱壇和香壇,那時國中太平。 6他還在猶大修築堅城,那些年國中太平,沒有戰事,因為耶和華賜他平安。 7他對猶大人說:「我們要修築城邑,在四周建造城牆和望樓,裝置大門和門閂。我們仍擁有這片土地,是因為我們尋求我們的上帝耶和華;我們尋求祂,祂就賜我們四境平安。」於是,他們修築城邑,凡事順利。 8亞撒的軍隊中有三十萬持大盾牌和矛槍的猶大人,二十八萬持小盾牌和弓箭的便雅憫人。他們都是英勇的戰士。

9古實謝拉率領一百萬大軍和三百輛戰車攻打猶大,到了瑪利沙10亞撒出兵迎敵,雙方在瑪利沙洗法谷擺開陣勢。 11亞撒呼求他的上帝耶和華說:「耶和華啊,唯有你才能幫助弱小的勝過強大的。我們的上帝耶和華啊,求你幫助我們,因為我們依靠你,奉你的名迎戰這大軍。耶和華啊,你是我們的上帝,不要讓人勝過你。」

12於是,耶和華使古實人敗在亞撒猶大人面前,古實人潰逃。 13亞撒率領軍隊乘勝追擊,直追到基拉耳古實人在耶和華和祂的軍兵面前大敗,傷亡慘重,一蹶不振。猶大人擄走了許多財物, 14攻陷了基拉耳四周的城邑,因為這些城裡的人都懼怕耶和華。他們洗劫各城,因為城中有大量財物。 15他們毀壞牲畜的圍欄,搶走許多羊和駱駝,然後返回耶路撒冷