2 Mbiri 13 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 13:1-22

Abiya Mfumu ya Yuda

1Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda, 2ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka zitatu. Dzina la amayi ake linali Maaka mwana wa Urieli wa ku Gibeya.

Koma panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu. 3Abiya anapita ku nkhondo ndi asilikali odziwa bwino nkhondo 400,000, ndipo Yeroboamu anandandalitsa ankhondo, asilikali 800,000 odziwa bwino nkhondo, osankhidwa ndi amphamvu, woti amenyane naye.

4Abiya anayima pa phiri la Zemaraimu, mʼdziko lamapiri la Efereimu, ndipo anati, “Yeroboamu ndi Aisraeli onse, tandimverani! 5Kodi inu simukudziwa kuti Yehova, Mulungu wa Israeli, wapereka ufumu wa Israeli kwa Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya ndiponso pangano la mchere? 6Komabe Yeroboamu mwana wa Nebati, mtumiki wa Solomoni mwana wa Davide, anawukira mbuye wake. 7Ndipo anthu ena achabechabe anasonkhana kwa iye ndipo anatsutsana ndi Rehobowamu mwana wa Solomoni pamene anali wamngʼono ndi wosalimba mtima ndi wopanda mphamvu kuti athe kulimbana nawo.

8“Ndipo tsopano inu mwakonzekera kutsutsana ndi ufumu wa Yehova, umene uli mʼmanja mwa zidzukulu za Davide. Inu ndithu mulipo ankhondo ambirimbiri ndipo muli ndi ana angʼombe agolide amene Yeroboamu anapanga kuti akhale milungu yanu. 9Koma kodi inu simunathamangitse ansembe a Yehova, ana a Aaroni ndiponso Alevi ndi kudzisankhira ansembe anuanu monga anthu ena amachitira? Aliyense amene amabwera kuti adzipatule atatenga mwana wangʼombe wamwamuna ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri amakhala wansembe wa zinthu zimene sizili milungu.

10“Koma kunena za ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, ndipo sitinamusiye. Ansembe amene amatumikira Yehova ndi ana a Aaroni ndipo amathandizidwa ndi Alevi. 11Mmawa uliwonse ndi madzulo aliwonse amapereka nsembe zopsereza ndi kufukiza lubani kwa Yehova. Iwo amayika buledi pa tebulo loyeretsedwa monga mwa mwambo ndipo amayatsa nyale pa zoyikapo nyale zagolide madzulo aliwonse. Ife timachita zofuna za Yehova Mulungu wathu. Koma inu mwamusiya. 12Mulungu ali nafe pakuti ndiye mtsogoleri wathu. Ansembe ake atanyamula malipenga, adzayimba mfuwu wankhondo kulimbana nanu. Inu Aisraeli musalimbane ndi Yehova, Mulungu wa makolo anu, pakuti simungathe kupambana.”

13Tsono Yeroboamu anali atatumiza asilikali kumbuyo mowazungulira, kotero kuti iye ali kutsogolo kwa anthu a ku Yuda, anthu owabisalira anali kumbuyo kwawo. 14Asilikali a Yuda anatembenuka ndipo anaona kuti nkhondo imachitikira kutsogolo ndi kumbuyo. Ndipo iwo anafuwulira Yehova. Ansembe anayimba malipenga awo 15ndipo asilikali a Yuda anafuwula mawu ankhondo. Atafuwula mawu ankhondowo, Mulungu anagonjetsa Yeroboamu pamodzi ndi Aisraeli onse pamaso pa Abiya ndi Yuda. 16Aisraeli anathawa Ayuda. Ndipo Mulungu anawapereka mʼmanja mwawo. 17Abiya pamodzi ndi anthu ake anapha anthu ambiri, kotero kuti Aisraeli 500,000 odziwa bwino nkhondo anaphedwa. 18Ankhondo a Israeli anagonjetsedwa pa nthawi imeneyi, ndipo ankhondo a Yuda anapambana chifukwa anadalira Yehova, Mulungu wa makolo awo.

19Abiya anathamangitsa Yeroboamu ndipo anamulanda mizinda ya Beteli, Yesana, ndi Efroni pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. 20Yeroboamu sanapezenso mphamvu nthawi ya Abiya. Ndipo Yehova anamukantha nafa.

21Koma Abiya mphamvu zake zinakula. Iye anakwatira akazi 14 ndipo anali ndi ana aamuna 22 ndi ana aakazi 16.

22Zina ndi zina zokhudza Abiya, zimene anachita ndi zimene anayankhula, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mneneri Ido.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

歷代志下 13:1-22

亞比雅與耶羅波安爭戰

1耶羅波安王執政第十八年,亞比雅登基做猶大王, 2耶路撒冷執政三年。他母親叫米該亞13·2 米該亞」在代下11·20是「押沙龍的女兒瑪迦」。,是基比亞烏列的女兒。亞比雅耶羅波安之間常有爭戰。 3有一次,亞比雅率領四十萬精兵出戰,耶羅波安率領八十萬精兵列陣迎戰。

4亞比雅站在以法蓮山區的西瑪蓮山上說:「耶羅波安和全體以色列人啊,你們聽我說, 5你們不知道以色列的上帝耶和華曾經立下永世之約13·5 永世之約」希伯來文是「鹽約」。,要把以色列國永遠賜給大衛和他的子孫嗎? 6尼八的兒子耶羅波安本是大衛的兒子所羅門的僕人,他卻背叛他的主人, 7召集一群無賴惡棍,與所羅門的兒子羅波安作對。那時,羅波安年輕怯懦,無力抵抗。

8「現在你們仗著人多勢眾,又有耶羅波安製造的金牛犢作為你們的神明,便企圖反抗大衛子孫所治理的耶和華的國度。 9你們趕走了做耶和華祭司的亞倫之後裔和利未人,效法外族人的惡俗為自己設立祭司。任何人牽來一頭公牛犢和七隻公綿羊,就可以自封為假神的祭司。

10「至於我們,耶和華是我們的上帝,我們沒有背棄祂,我們有亞倫的後裔做祭司事奉耶和華,也有利未人各盡其職。 11他們每天早晚向耶和華獻燔祭,燒芬芳的金燈臺香,把供餅擺在潔淨13·11 潔淨」指宗教禮儀上的潔淨。的桌子上,每晚點上的燈。我們遵守我們上帝耶和華的吩咐,你們卻背棄祂。 12上帝與我們同在,祂率領我們。祂的祭司就要吹響向你們進攻的號角。以色列人啊,不要與你們祖先的上帝耶和華作對,因為你們絕不會得勝。」

13耶羅波安卻在猶大人後面設伏兵,企圖前後夾攻他們。 14猶大人轉身,發現自己前後受敵,就呼求耶和華。祭司吹響號角, 15猶大人便吶喊,上帝使耶羅波安以色列人敗在亞比雅猶大人面前。 16以色列人從猶大人面前逃跑,上帝把他們交在猶大人手中。 17亞比雅和他的軍隊大敗以色列人,殲滅了他們五十萬精兵。 18這樣,以色列人被擊敗,猶大人因為倚靠他們祖先的上帝耶和華而大獲全勝。

19亞比雅追趕耶羅波安,攻取了伯特利耶沙拿以法拉音各城以及它們周圍的村莊。 20亞比雅在世之日,耶羅波安再也沒有恢復勢力。後來,耶和華攻擊他,他就死了。 21亞比雅卻日漸強大,他有十四個妻妾、二十二個兒子、十六個女兒。 22亞比雅其餘的事及其言行都記在易多先知的史記上。