2 Mbiri 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 1:1-17

Solomoni Apempha Nzeru

1Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.

2Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja. 3Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja. 4Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu. 5Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko. 6Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.

7Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”

8Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake. 9Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi. 10Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”

11Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo, 12Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”

13Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.

14Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu. 15Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa. 16Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe. 17Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.

New International Reader’s Version

2 Chronicles 1:1-17

Solomon Asks God for Wisdom

1Solomon was the son of David. Solomon made his position secure over his kingdom. The Lord his God was with him. He made Solomon very great.

2Solomon spoke to the whole community of Israel. He spoke to the commanders of thousands of men and commanders of hundreds. He spoke to the judges and all the leaders in Israel. He spoke to the leaders of Israel’s families. 3Solomon and the whole community went to the high place at Gibeon. That’s because God’s tent of meeting was there. The Lord’s servant Moses had made the tent in the desert. 4David had carried up the ark of God from Kiriath Jearim. He had it brought to the place he had prepared for it. He had set up a tent for it in Jerusalem. 5But the bronze altar that Bezalel had made was in Gibeon. Bezalel was the son of Uri. Uri was the son of Hur. The altar was in front of the Lord’s holy tent. So Solomon and the whole community asked the Lord for advice in Gibeon. 6Solomon went up to the bronze altar in front of the Lord at the tent of meeting. Solomon sacrificed 1,000 burnt offerings on the altar.

7That night God appeared to Solomon. He said to him, “Ask for anything you want me to give you.”

8Solomon answered God, “You were very kind to my father David. Now you have made me king in his place. 9Lord God, let the promise you gave to my father David come true. You have made me king. My people are as many as the dust of the earth. They can’t be counted. 10Give me wisdom and knowledge. Then I’ll be able to lead these people. Without your help, who would be able to rule this great nation of yours?”

11God said to Solomon, “I am glad that those are the things you really want. You have not asked for wealth, possessions or honor. You have not even asked to have your enemies killed. You have not asked to live for a long time. Instead, you have asked for wisdom and knowledge. You want to be able to rule my people wisely. I have made you king over them. 12So wisdom and knowledge will be given to you. I will also give you wealth, possessions and honor. You will have more than any king before you ever had. And no king after you will have as much.”

13Then Solomon left the high place at Gibeon. He went from the tent of meeting there to Jerusalem. And he ruled over Israel.

14Solomon had 1,400 chariots and 12,000 horses. He kept some of them in the chariot cities. He kept others with him in Jerusalem. 15The king made silver and gold as common in Jerusalem as stones. He made cedar wood as common there as sycamore-fig trees in the western hills. 16Solomon got horses from Egypt and Kue. The king’s buyers purchased them from Kue at the current price. 17They could get a chariot from Egypt for 15 pounds of silver. They could get a horse for less than four pounds of silver. They sold horses and chariots to all the Hittite and Aramean kings.