2 Mafumu 8 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 8:1-29

Mayi wa ku Sunemu Atenganso Munda wake

1Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.” 2Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.

3Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake. 4Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.” 5Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake.

Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.” 6Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo.

Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”

Hazaeli Apha Beni-Hadadi

7Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,” 8inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’ ”

9Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’ ”

10Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.” 11Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.

12Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?”

Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”

13Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?”

Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”

14Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.” 15Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.

Yehoramu Mfumu ya ku Yuda

16Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda. 17Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu. 18Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova. 19Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.

20Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu. 21Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo. 22Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.

23Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? 24Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Ahaziya Mfumu ya ku Yuda

25Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira. 26Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli. 27Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.

28Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu. 29Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu.

Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.

New Russian Translation

4 Царств 8:1-29

Возвращение земли шунамитянки

1Елисей сказал женщине, сына которой он воскресил:

– Уходи с семьей и поселись, где сможешь, потому что Господь навел на страну голод, который будет длиться семь лет.

2Женщина собралась и сделала, как сказал Божий человек. Вместе с семьей она ушла и семь лет жила в земле филистимлян.

3Через семь лет она вернулась из земли филистимлян и пошла к царю просить о своем доме и земле. 4А царь в то время беседовал с Гиезием, слугой Божьего человека, и сказал:

– Расскажи мне о великих делах, которые совершил Елисей.

5Как раз, когда Гиезий рассказывал царю о том, как Елисей воскресил мертвого, женщина, чьего сына Елисей воскресил, пришла просить царя о своем доме и земле. Гиезий сказал:

– Вот это и есть та женщина, господин мой царь, а это ее сын, которого воскресил Елисей.

6Царь расспросил женщину, и она рассказала ему. Тогда он назначил чиновника рассмотреть ее дело, сказав ему:

– Верни ей все, что у нее было, а также все доходы от ее земли, что были получены с того дня, как она покинула страну, до этого дня.

Предсказание Елисея об убийстве Венадада

7Елисей пришел в Дамаск, когда Венадад, царь Арама, был болен. Когда царю доложили: «Сюда пришел Божий человек», 8– он сказал Хазаилу:

– Возьми с собой подарок и иди встречать Божьего человека. Спроси через него Господа, сказав: «Выздоровею ли я от этой болезни?»

9Хазаил пошел встречать Елисея, взяв с собой в дар лучших товаров Дамаска на сорок верблюжьих поклаж. Он пришел, встал перед ним и сказал:

– Твой сын Венадад, царь Арама, послал меня спросить: «Выздоровею ли я от этой болезни?»

10Елисей сказал:

– Иди и скажи ему: «Ты обязательно выздоровеешь», но Господь открыл мне, что на самом деле он умрет.

11Елисей смотрел на него не отрываясь, пока Хазаил не смутился. Тогда Божий человек заплакал.

12– Почему мой господин плачет? – спросил Хазаил.

– Потому что я знаю, какое зло ты причинишь израильтянам, – ответил он. – Ты сожжешь их крепости, юношей их убьешь мечом, разобьешь их младенцев о землю и порубишь их беременных женщин.

13Хазаил сказал:

– Как твой слуга, который лишь пес, сможет совершить такое большое дело?

– Господь открыл мне, что ты станешь царем Арама, – ответил Елисей8:13 Здесь Елисей произносит пророчество, которое ранее было открыто Богом Илии (см. 3 Цар. 19:15-17)..

14Тогда Хазаил ушел от Елисея и вернулся к своему господину.

Венадад спросил:

– Что сказал тебе Елисей?

Хазаил ответил:

– Он сказал мне, что ты непременно выздоровеешь.

15Но на другой день он взял одеяло, намочил его водой, накрыл им лицо царя, и тот умер. А Хазаил стал царем вместо него.

Иорам – царь Иудеи

(2 Пар. 21:5-10, 20)

16На пятом году правления израильского царя Иорама, сына Ахава, когда Иосафат еще был царем Иудеи, в Иудее начал царствовать Иорам, сын Иосафата. 17Ему было тридцать два года, когда он стал царем, и правил он в Иерусалиме восемь лет. 18Он ходил путем царей Израиля, по примеру дома Ахава, потому что женился на дочери Ахава. Он делал зло в глазах Господа. 19Но ради Своего слуги Давида Господь не хотел погубить Иудею. Он обещал сохранить светильник ему и его потомкам навеки.

20Во времена Иорама Эдом восстал против правления Иудеи и поставил себе царя. 21Тогда Иорам пошел в Цаир со всеми своими колесницами. Ночью он приготовился и напал на эдомитян и на начальников их колесниц, которые окружили его, но его войско бежало домой. 22И до сих пор Эдом не покорен правлению Иудеи. Ливна восстала в то же самое время.

23Что же до прочих событий правления Иорама и его дел, то разве не записаны они в «Книге летописей царей Иудеи»? 24Иорам упокоился со своими предками и был похоронен с ними в Городе Давида. Охозия, его сын, стал царем вместо него.

Охозия – царь Иудеи

(2 Пар. 22:1-6)

25На двенадцатом году правления израильского царя Иорама, сына Ахава, над Иудеей начал царствовать Охозия, сын Иорама. 26Охозии было двадцать два года когда он стал царем, и правил он в Иерусалиме один год. Его мать звали Аталия; она была внучкой Омри, царя Израиля. 27Он ходил путем дома Ахава и делал зло в глазах Господа, по примеру дома Ахава8:27 Аталия, мать Охозии, была дочерью Ахава (см. ст. 18)., ведь он породнился с домом Ахава через брак.

28Охозия ходил с Иорамом, сыном Ахава, воевать против Хазаила, царя Арама, под Рамот Галаадский. Арамеи ранили Иорама, 29и царь Иорам вернулся в Изреель, чтобы оправиться от ран, которые ему нанесли при Рамоте8:29 Евр.: «Рама», вариант названия Рамот., когда он сражался с Хазаилом, царем Арама.

Охозия, сын Иорама, царя Иудеи, отправился в Изреель навестить Иорама, сына Ахава, потому что тот был ранен.