2 Mafumu 8 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 8:1-29

Mayi wa ku Sunemu Atenganso Munda wake

1Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.” 2Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.

3Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake. 4Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.” 5Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake.

Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.” 6Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo.

Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”

Hazaeli Apha Beni-Hadadi

7Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,” 8inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’ ”

9Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’ ”

10Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.” 11Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.

12Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?”

Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”

13Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?”

Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”

14Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.” 15Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.

Yehoramu Mfumu ya ku Yuda

16Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda. 17Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu. 18Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova. 19Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.

20Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu. 21Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo. 22Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.

23Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? 24Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Ahaziya Mfumu ya ku Yuda

25Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira. 26Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli. 27Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.

28Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu. 29Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu.

Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

列王紀下 8:1-29

書念婦人得回產業

1以利沙曾經救活了一位書念婦人的兒子。他對那婦人說:「你和家人要離開這裡去別處寄居,因為耶和華已決定使這裡遭受七年饑荒。」 2那婦人遵照上帝僕人的話,舉家遷往非利士,在那裡寄居了七年。 3七年後,她從非利士返回,去向王請求收回自己的房屋和田地。 4那時,王正與上帝僕人的侍者基哈西談話,讓基哈西以利沙所做的一切大事講給他聽。 5基哈西正在向王講述以利沙如何使死人復活的時候,那位書念婦人剛好進宮求見王,基哈西便說:「我主我王,這就是那婦人,這是她那個被以利沙救活的兒子。」 6王問那婦人,她便原原本本地將那件事稟告王。王委派一位臣僕處理她的事情,並吩咐說:「凡屬於這婦人的東西,包括從她離開本地直到今天她田地的所有出產,要全部還給她。」

以利沙對哈薛的預言

7一天,以利沙到了大馬士革。當時亞蘭便·哈達正在生病,他得知上帝的僕人來了, 8便對哈薛說:「你帶著禮物去見上帝的僕人,請他求問耶和華,看看我這病能否痊癒。」 9哈薛用四十頭駱駝馱著大馬士革的各種美物前去拜見以利沙。到了那裡,他站在以利沙面前說:「你兒子亞蘭便·哈達派我來問你,他的病能否痊癒?」

10以利沙哈薛說:「你去告訴他,他一定會痊癒。不過,耶和華告訴我他會死。」 11他目不轉睛地盯著哈薛,盯得他很不安。然後,上帝的僕人哭了。 12哈薛問:「我主為什麼哭呢?」以利沙說:「因為我知道你會加害以色列人。你會放火燒他們的堡壘,用刀殺戮他們的壯丁,摔死他們的孩童,剖開他們的孕婦。」 13哈薛說:「你僕人算什麼,不過是一條狗,怎能做這樣的大事呢?」以利沙說:「耶和華告訴我,你要做亞蘭王。」 14哈薛辭別以利沙回去了。王問他:「以利沙對你說什麼?」他答道:「以利沙告訴我,你一定會痊癒。」 15第二天,哈薛拿了一床浸透水的被子,蒙在王的臉上,王窒息而死。於是哈薛篡位。

約蘭做猶大王

16以色列亞哈的兒子約蘭執政第五年,猶大約沙法讓位給兒子約蘭17約蘭三十二歲登基,在耶路撒冷執政八年。 18他與亞哈家一樣步以色列諸王的後塵,因為他娶了亞哈的女兒為妻,做耶和華視為惡的事。 19但耶和華因祂僕人大衛的緣故而不願毀滅猶大,因為祂曾應許讓大衛的子孫永遠做王。 20約蘭執政期間,以東人反叛猶大,自己立王。 21約蘭率領所有戰車前往撒益,他和戰車長們被以東人包圍。他們乘夜出擊,突出重圍,各自逃回家去。 22以東人至今仍脫離猶大的統治。立拿人也在那個時候叛變了。

23約蘭其他的事及其一切所作所為都記在猶大列王史上。 24約蘭與祖先同眠後,葬在大衛城他的祖墳裡。他兒子亞哈謝繼位。

亞哈謝做猶大王

25以色列亞哈的兒子約蘭執政第十二年,猶大約蘭的兒子亞哈謝登基。 26他二十二歲登基,在耶路撒冷執政一年。他母親叫亞她利雅,是以色列暗利的孫女。 27亞哈謝亞哈家的女婿,他步亞哈家的後塵,做耶和華視為惡的事。

28他聯合亞哈的兒子約蘭基列拉末亞蘭哈薛交戰。約蘭受了傷, 29便回到耶斯列療傷。猶大亞哈謝前去探望。