2 Mafumu 7 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 7:1-20

1Ndipo Elisa anati, “Mverani mawu a Yehova. Yehova akuti, ‘Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.’ ”

2Mtsogoleri amene mfumu inkamudalira anati kwa munthu wa Mulungu, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?”

Elisa anamuyankha kuti, “Taona, iweyo udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”

Akhate Anayi Awulula za Kuthawa kwa Aaramu

3Tsono pa chipata cholowera mu mzinda wa Samariya pankakhala anthu anayi akhate. Iwo anayankhulana kuti, “Chifukwa chiyani tikungokhala pano kudikira kufa? 4Ngati tinganene kuti, ‘Tidzalowa mu mzinda,’ njala ili mu mzindamo ndipo tidzafa. Ndipo ngati tikhalebe pano, tidzafa ndithu. Choncho tiyeni tipite ku msasa wa Aaramu ndi kukadzipereka. Ngati sakatipha, tidzakhala ndi moyo, ngati akatipha, basi tikafa.”

5Iwo ananyamuka ndi kachisisira kupita ku msasa wa Aaramu. Atafika mʼmalire a msasa, taonani, sanapeze munthu ndi mmodzi yemwe, 6pakuti Ambuye anali atamveketsa phokoso la magaleta ndi akavalo ndiponso mdidi wa gulu lalikulu la ankhondo, kotero anayamba kuwuzana kuti, “Taonani, mfumu ya ku Israeli yalemba ganyu mafumu a Ahiti ndi a Aigupto kuti adzatithire nkhondo!” 7Choncho ananyamuka nathawa ndi kachisisira ndipo anasiya matenti, akavalo ndi abulu awo. Iwo anasiya msasa wawo momwe unalili nathawa kupulumutsa miyoyo yawo.

8Anthu akhate aja atafika mʼmalire mwa msasa analowa mʼtenti imodzi. Anadya ndi kumwa, natenga siliva, golide ndi zovala ndipo anachoka kupita kukazibisa. Atabwerera anakalowa mʼtenti ina ndipo anatenga zinthu mʼmenemo nakazibisanso.

9Kenaka akhate aja anawuzana kuti, “Ife sitikuchita bwino. Lero ndi tsiku la uthenga wabwino ndipo tikungokhala chete. Tikadikira mpaka kucha, tidzalangidwa. Tiyeni msanga tikafotokoze zimenezi ku nyumba yaufumu.”

10Choncho anapita nakayitana alonda a pa chipata cha mzinda ndi kufotokoza kuti, “Ife tinapita ku msasa wa Aaramu ndipo sitinapezeko munthu, kapena phokoso la wina aliyense koma tinangopeza akavalo okha pamodzi ndi abulu ali chimangire.” 11Alonda a pa chipata aja analengeza uthengawu kwa okhala mʼnyumba yaufumu.

12Mfumu inadzuka usiku ndipo inawuza atsogoleri ake a ankhondo kuti, “Ndikukuwuzani zimene Aaramu atichitira ife. Akudziwa kuti tikufa ndi njala; kotero achoka mu msasa wawo kukabisala kuthengo ndi kuti, ‘Iwowa atuluka ndithu, ndipo ife tidzawagwira amoyo ndi kulowa mu mzindamo.’ ”

13Mmodzi mwa atsogoleri ake ankhondo anayankha kuti, “Chonde uzani anthu ena atenge akavalo asanu amene atsala mu mzinda muno. Taonani, zomwe zingawachitikire zidzakhala zofanana ndi zomwe zingachitikire ena onse amene atsala. Inde iwo adzangokhala ngati Aisraeli ena onse amene awonongeka kale. Choncho tiyeni tiwatume akafufuze zomwe zachitika.”

14Choncho anasankha magaleta awiri pamodzi ndi akavalo ake, ndipo mfumu inawatuma kuti alondole gulu lankhondo la Aaramu. Mfumuyo inalamula oyendetsa akavalowo kuti, “Pitani kaoneni.” 15Anthuwa anawalondola mpaka ku Yorodani, ndipo taonani, mʼnjira monse munali zovala zokhazokha ndi zinthu zimene Aaramu ankazitaya pamene ankathawa mofulumira. Ndipo amithengawo anabwerera ndi kudzafotokozera mfumu. 16Tsono anthu a mu Samariya anatuluka nakafunkha ku msasa wa Aaramu. Kotero kuti makilogalamu atatu a ufa ankawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele ankawagulitsanso pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, monga momwe ananenera Yehova.

17Tsono mfumu inayika mtsogoleri amene ankamudalira uja kuti akhale woyangʼanira pa chipata ndipo anthu anamupondaponda ku chipata kuja, ndipo anafa, monga momwe Elisa munthu wa Mulungu ananenera mfumu itapita ku nyumba yake. 18Zinachitika molingana ndi zomwe ananena munthu wa Mulungu zija kuti “Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.”

19Mtsogoleriyu ananena kwa munthu wa Mulungu kuti, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Munthu wa Mulungu anamuyankha kuti, “Iwe udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.” 20Ndipo izi ndi zomwe zinamuchitikiradi mtsogoleriyu, pakuti anthu anamupondaponda pa chipata ndipo anafa.

New Russian Translation

4 Царств 7:1-20

1Но Елисей сказал:

– Слушай слово Господне. Так говорит Господь: «Завтра к этому времени у ворот Самарии сата7:1 Возможно, около 7 л; также в ст. 16 и 18. лучшей муки будет продаваться за шекель7:1 Около 11 г; также в ст. 16 и 18. и две саты7:1 Возможно, около 14 л; также в ст. 16 и 18. ячменя за шекель».

2Сановник, на чью руку опирался царь Израиля, сказал Божьему человеку:

– Послушай, этого не может быть, даже если Господь откроет небесные окна!

– Ты увидишь это своими глазами, – ответил Елисей, – но есть не будешь!

Конец осады

3У входа в городские ворота было четверо прокаженных. Они сказали друг другу:

– Чего нам сидеть тут и ждать смерти? 4Если мы решим: «Пойдем в город», то там голод, и мы умрем. И если мы останемся здесь, то все равно умрем. Давайте же пойдем в лагерь к арамеям и сдадимся. Если они пощадят нас, останемся в живых, а если нет, то умрем.

5В вечерних сумерках они встали и пошли в лагерь арамеев. Когда они добрались до края лагеря, там никого не было, 6потому что Владыка сделал так, что арамеи услышали шум колесниц, коней и огромного войска, и они сказали друг другу:

– Это царь Израиля нанял хеттейских и египетских царей, чтобы напасть на нас!

7Они встали и в сумерках бежали, бросив шатры, лошадей и ослов. Они бросили лагерь, как он был, и спасались бегством.

8Прокаженные добрались до края лагеря и вошли в один из шатров. Они наелись, напились и унесли оттуда серебро, золото и одежды, ушли и спрятали их. Потом они вернулись и вошли в другой шатер и, взяв кое-что и из него, ушли и спрятали это тоже. 9Затем они сказали друг другу:

– Мы поступаем неправильно. Это день хороших вестей, а мы держим их при себе. Если мы будем ждать рассвета, нас постигнет кара. Пойдем сейчас же и доложим об этом в царском дворце.

10Они пошли, позвали городских привратников и сказали им:

– Мы ходили в лагерь арамеев, но там никого не видно и не слышно; только привязанные кони, и ослы, и шатры, как они были.

11Привратники разгласили весть, и об этом было доложено во дворце. 12Царь встал ночью и сказал своим приближенным:

– Я скажу вам, что сделали арамеи. Они знают, что мы голодаем, и покинули лагерь, чтобы спрятаться в поле, думая: «Они непременно выйдут, мы возьмем их живыми и войдем в город».

13Один из его приближенных сказал:

– Пусть возьмут пять из оставшихся лошадей и узнают, что произошло. Ведь те, кто уцелел, здесь все равно разделят судьбу всего множества израильтян, которое уже погибло.

14Они взяли две колесницы с конями, и царь послал их за войском Арама. Он приказал колесничим:

– Пойдите и узнайте, что произошло.

15Они ехали по следам войска Арама до самого Иордана и видели, что вся дорога усеяна одеждами и снаряжением арамеев, которые те бросали во время стремительного бегства. Посланцы вернулись и доложили об увиденном царю. 16Народ вышел и разграбил лагерь арамеев. Сату лучшей муки стали продавать за шекель, и две саты ячменя за шекель, как и сказал Господь. 17А царь поставил своего ближайшего сановника следить за порядком в городских воротах, и там его растоптала толпа. Он умер, как и предсказывал Божий человек, когда царь приходил к нему домой. 18(Когда Божий человек говорил царю: «Завтра к этому времени у ворот Самарии сату лучшей муки будет продавать за шекель и две саты ячменя за шекель», 19тот сановник сказал Божьему человеку: «Послушай, этого не может быть, даже если Господь откроет небесные окна!» Тогда Божий человек ответил: «Ты увидишь это своими глазами, но есть не будешь!») 20Так с ним и произошло: толпа растоптала его в воротах, и он умер.