2 Mafumu 7 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 7:1-20

1Ndipo Elisa anati, “Mverani mawu a Yehova. Yehova akuti, ‘Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.’ ”

2Mtsogoleri amene mfumu inkamudalira anati kwa munthu wa Mulungu, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?”

Elisa anamuyankha kuti, “Taona, iweyo udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”

Akhate Anayi Awulula za Kuthawa kwa Aaramu

3Tsono pa chipata cholowera mu mzinda wa Samariya pankakhala anthu anayi akhate. Iwo anayankhulana kuti, “Chifukwa chiyani tikungokhala pano kudikira kufa? 4Ngati tinganene kuti, ‘Tidzalowa mu mzinda,’ njala ili mu mzindamo ndipo tidzafa. Ndipo ngati tikhalebe pano, tidzafa ndithu. Choncho tiyeni tipite ku msasa wa Aaramu ndi kukadzipereka. Ngati sakatipha, tidzakhala ndi moyo, ngati akatipha, basi tikafa.”

5Iwo ananyamuka ndi kachisisira kupita ku msasa wa Aaramu. Atafika mʼmalire a msasa, taonani, sanapeze munthu ndi mmodzi yemwe, 6pakuti Ambuye anali atamveketsa phokoso la magaleta ndi akavalo ndiponso mdidi wa gulu lalikulu la ankhondo, kotero anayamba kuwuzana kuti, “Taonani, mfumu ya ku Israeli yalemba ganyu mafumu a Ahiti ndi a Aigupto kuti adzatithire nkhondo!” 7Choncho ananyamuka nathawa ndi kachisisira ndipo anasiya matenti, akavalo ndi abulu awo. Iwo anasiya msasa wawo momwe unalili nathawa kupulumutsa miyoyo yawo.

8Anthu akhate aja atafika mʼmalire mwa msasa analowa mʼtenti imodzi. Anadya ndi kumwa, natenga siliva, golide ndi zovala ndipo anachoka kupita kukazibisa. Atabwerera anakalowa mʼtenti ina ndipo anatenga zinthu mʼmenemo nakazibisanso.

9Kenaka akhate aja anawuzana kuti, “Ife sitikuchita bwino. Lero ndi tsiku la uthenga wabwino ndipo tikungokhala chete. Tikadikira mpaka kucha, tidzalangidwa. Tiyeni msanga tikafotokoze zimenezi ku nyumba yaufumu.”

10Choncho anapita nakayitana alonda a pa chipata cha mzinda ndi kufotokoza kuti, “Ife tinapita ku msasa wa Aaramu ndipo sitinapezeko munthu, kapena phokoso la wina aliyense koma tinangopeza akavalo okha pamodzi ndi abulu ali chimangire.” 11Alonda a pa chipata aja analengeza uthengawu kwa okhala mʼnyumba yaufumu.

12Mfumu inadzuka usiku ndipo inawuza atsogoleri ake a ankhondo kuti, “Ndikukuwuzani zimene Aaramu atichitira ife. Akudziwa kuti tikufa ndi njala; kotero achoka mu msasa wawo kukabisala kuthengo ndi kuti, ‘Iwowa atuluka ndithu, ndipo ife tidzawagwira amoyo ndi kulowa mu mzindamo.’ ”

13Mmodzi mwa atsogoleri ake ankhondo anayankha kuti, “Chonde uzani anthu ena atenge akavalo asanu amene atsala mu mzinda muno. Taonani, zomwe zingawachitikire zidzakhala zofanana ndi zomwe zingachitikire ena onse amene atsala. Inde iwo adzangokhala ngati Aisraeli ena onse amene awonongeka kale. Choncho tiyeni tiwatume akafufuze zomwe zachitika.”

14Choncho anasankha magaleta awiri pamodzi ndi akavalo ake, ndipo mfumu inawatuma kuti alondole gulu lankhondo la Aaramu. Mfumuyo inalamula oyendetsa akavalowo kuti, “Pitani kaoneni.” 15Anthuwa anawalondola mpaka ku Yorodani, ndipo taonani, mʼnjira monse munali zovala zokhazokha ndi zinthu zimene Aaramu ankazitaya pamene ankathawa mofulumira. Ndipo amithengawo anabwerera ndi kudzafotokozera mfumu. 16Tsono anthu a mu Samariya anatuluka nakafunkha ku msasa wa Aaramu. Kotero kuti makilogalamu atatu a ufa ankawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele ankawagulitsanso pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, monga momwe ananenera Yehova.

17Tsono mfumu inayika mtsogoleri amene ankamudalira uja kuti akhale woyangʼanira pa chipata ndipo anthu anamupondaponda ku chipata kuja, ndipo anafa, monga momwe Elisa munthu wa Mulungu ananenera mfumu itapita ku nyumba yake. 18Zinachitika molingana ndi zomwe ananena munthu wa Mulungu zija kuti “Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.”

19Mtsogoleriyu ananena kwa munthu wa Mulungu kuti, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Munthu wa Mulungu anamuyankha kuti, “Iwe udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.” 20Ndipo izi ndi zomwe zinamuchitikiradi mtsogoleriyu, pakuti anthu anamupondaponda pa chipata ndipo anafa.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

列王紀下 7:1-20

1以利沙說:「你們要聽耶和華的話,耶和華說,『明天這個時候,在撒瑪利亞城門口,三公斤細麵粉只賣十一克銀子,六公斤大麥也賣十一克銀子。』」 2一個攙扶王的將領對上帝的僕人說:「即使耶和華打開天上的窗戶,也不可能發生這樣的事!」以利沙說:「你必親眼看見,卻吃不到。」

撒瑪利亞城獲救

3城門口有四個痲瘋病人,他們商量說:「我們為什麼坐在這裡等死呢? 4如果我們進城,城裡正鬧饑荒,我們會餓死;但我們坐在這裡也是死,不如去投靠亞蘭軍。如果他們不殺我們,我們就能活命;如若不然,死就死吧!」 5傍晚時分,他們動身去亞蘭人的營地,到了營地外邊,卻發現人影全無。 6原來,主使亞蘭人聽見大隊人馬和戰車的聲音。他們以為以色列王雇用了人的諸王和埃及人的諸王來攻營, 7便在傍晚時分撇下帳篷、馬和驢,棄營而逃。 8那幾個痲瘋病人到了營地,走進一個帳篷,又吃又喝,把那裡的金銀和衣服拿走收藏起來,再回來進入另一個帳篷,把財物拿走收藏起來。

9後來,他們彼此說:「我們這樣做不對。今天是個報好消息的日子,我們卻不作聲。若等到天亮,我們會受懲罰的。走,我們給王報信去。」 10他們就去喊城門守衛,對他們說:「我們到了亞蘭人的營中,裡面不見人影也沒有人聲,只有拴著的馬和驢,帳篷依然在那裡。」 11城門守衛就高聲宣告消息,有人去稟告王。 12王連夜起來,對臣僕說:「我告訴你們是怎麼回事。亞蘭人知道我們正鬧饑荒,就故意離開軍營,埋伏在田野,等我們以色列人出城後,好活捉我們,並攻入城中。」

13一個臣僕說:「不如派人騎著城中僅存的五匹馬出去打探一下。反正他們和城中剩下的以色列人一樣快要死了。」 14他們預備了兩輛馬車,王便命人出去追蹤亞蘭軍、查明實情。 15探子一路追到約旦河,沿路看見到處都是亞蘭軍倉皇逃走時丟棄的衣服和裝備,便回去稟告王。 16於是,民眾出城搶掠亞蘭人的營地。那時,三公斤細麵粉只賣十一克銀子,六公斤大麥也只賣十一克銀子,正如耶和華所言。 17王派那位攙扶他的將領守在城門口維持秩序,那將領卻被湧出的人群踩死,應驗了上帝的僕人在王去見他時所說的話。 18上帝的僕人曾對王說:「明天這個時候,在撒瑪利亞城門口,三公斤細麵粉只賣十一克銀子,六公斤大麥也只賣十一克銀子。」

19但那將領對上帝的僕人說:「即使耶和華打開天上的窗戶,也不可能發生這樣的事!」上帝的僕人說:「你必親眼看見,卻吃不到。」 20這話果然應驗在他身上,他被人群踩死在城門口。