2 Mafumu 5 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 5:1-27

Naamani Achiritsidwa Khate Lake

1Tsono Naamani anali mtsogoleri wa gulu lankhondo a mfumu ya ku Aramu. Iye anali munthu wodalirika pamaso pa mbuye wake ndipo anali wokondedwa kwambiri, chifukwa kudzera mwa iye Yehova anapambanitsa Aaramu. Anali msilikali wolimba mtima, koma anali ndi khate.

2Tsono magulu a Aaramu anapita ku nkhondo ndipo anakagwira ukapolo mtsikana wamngʼono wa ku Israeli, ndipo ankatumikira mkazi wa Naamani. 3Mtsikanayo anawuza mkazi wa Naamani kuti, “Mbuye wanga akanapita kukaonana ndi mneneri amene amakhala ku Samariya, akanachiritsidwa khate lawo.”

4Naamani anapita kwa mbuye wake kukamuwuza zomwe mtsikana wochokera ku Israeli ananena. 5Mfumu ya ku Aramu inayankha kuti, “Iwe uyenera kupita. Ine ndilembera kalata mfumu ya ku Israeli.” Choncho Naamani ananyamuka kupita ku Samariya, atatenga ndalama za siliva 30,000, ndalama zagolide 6,000 ndiponso zovala khumi za pa chikondwerero. 6Kalata imene anapita nayo kwa mfumu ya ku Israeli inali ndi mawu awa: “Taonani, ndikutumiza Naamani mtumiki wanga pamodzi ndi kalatayi kwa inu kuti mumuchiritse khate lake.”

7Mfumu ya ku Israeli itangowerenga kalatayo, inangʼamba mkanjo wake ndipo inati, “Kodi ine ndine Mulungu? Kodi ndingathe kupha kapena kupereka moyo? Chifukwa chiyani munthu ameneyu wanditumizira munthu woti ndimuchiritse khate lake? Taonani, iyeyu akungofuna kuti apeze chifukwa choyambanirana nane!”

8Elisa munthu wa Mulungu atamva kuti mfumu ya ku Israeli yangʼamba mkanjo wake, anatumiza uthenga uwu: “Chifukwa chiyani mwangʼamba mkanjo wanu? Mutumizeni munthuyo kwa ine ndipo iyeyo adzadziwa kuti muli mneneri mu Israeli.” 9Choncho Naamani anapita pamodzi ndi akavalo ake ndi magaleta nakayima pa khomo la nyumba ya Elisa. 10Elisa anatumiza uthenga kwa iye woti, “Pita, kasambe kasanu ndi kawiri mu mtsinje wa Yorodani, thupi lako lidzachira ndi kukhalanso monga kale ndipo udzayeretsedwa.”

11Koma Naamani anachoka mokwiya ndipo anati, “Ine ndimaganiza kuti munthuyu atuluka ndipo ayimirira nayitana dzina la Yehova Mulungu wake, nayendetsa dzanja lake pamwamba pa nthendayi ndi kundichiritsa khate langa. 12Kodi Abana ndi Faripara, mitsinje ya ku Damasiko, siyoposa mitsinje ina yonse ya ku Israeli? Kodi sindikanasamba mʼmitsinje imeneyo ndi kuyeretsedwa?” Kotero anatembenuka nachoka ali wokwiya kwambiri.

13Antchito ake anamuyandikira namufunsa kuti, “Abambo anga, mneneri akanakulamulani chinthu chachikulu, kodi inu simukanachita? Nanga nʼzovuta motani zomwe mneneri wanena kuti ‘Kasambeni ndipo mudzayeretsedwa!’ ” 14Choncho Naamani anapita ku Yorodani nakadzimiza mʼmadzimo kasanu nʼkawiri, monga momwe munthu wa Mulungu anamuwuzira. Thupi lake linakhalanso monga kale ndipo linakhala losalala ngati la kamnyamata.

15Pamenepo Naamani ndi atumiki ake onse anabwerera kwa munthu wa Mulungu uja. Naamani anayima pamaso pa Elisa ndipo anati, “Tsopano ndikudziwa kuti kulibe Mulungu wina pa dziko lonse lapansi koma mu Israeli mokha. Chonde, tsopano landirani mphatso ya mtumiki wanu.”

16Mneneri anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene ine ndimamutumikira, sindidzalandira zimenezi.” Ndipo ngakhale Naamani anamukakamiza, iye anakanabe.

17Naamani anati, “Ngati inu simulandira, chonde lolani mtumiki wanu kuti atengeko dothi lokwanira kunyamula abulu awiri, popeza mtumiki wanu sadzaperekanso nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa mulungu wina koma Yehova. 18Koma Yehova andikhululukire ine pa chinthu ichi: Pamene mbuye wanga alowa mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni ine ndimapita naye ndipo ndimakagwada naye limodzi. Pamene ndikugwada mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni, Yehova azikhululukira mtumiki wanu pa chinthu chimenechi.”

19Elisa anati, “Pita mu mtendere.”

Choncho anachoka nayenda pangʼono. 20Koma Gehazi, mtumiki wa Elisa munthu wa Mulungu, anaganiza mu mtima mwake kuti, “Taonani, mbuye wanga wamulekerera Naamani Mwaramuyu, posalandira zomwe anabweretsa. Pali Yehova wamoyo, ine ndimuthamangira ndipo ndikatengako zinthu kwa iye.”

21Choncho Gehazi anamuthamangira Naamani uja. Naamani ataona Gehazi akumuthamangira, anatsika mʼgaleta lake ndi kukakumana naye. Iye anafunsa Gehazi kuti, “Kodi nʼkwabwino?”

22Gehazi anayankha kuti, “Inde nʼkwabwino. Mbuye wanga wandituma kuti ndidzakuwuzeni kuti, ‘Anyamata awiri mwa ana a aneneri angondipeza kumene kuchokera ku dziko la mapiri la Efereimu. Chonde apatseniko ndalama za siliva 3,000 ndi zovala ziwiri za pa phwando.’ ”

23Naamani anati, “Kuli bwino utenge ndalama zasiliva 6,000.” Iye anakakamiza Gehazi kuti alandire, ndipo kenaka anamanga matumba awiri a ndalama zasiliva pamodzi ndi zovala zinayi za pa mphwando. Naamani anazipereka kwa antchito ake awiri ndipo anazinyamula nayenda patsogolo pa Gehazi. 24Gehazi atafika ku phiri, anawalanda antchito aja zinthu zija nazibisa mʼnyumbamo. Iye anawawuza anthu aja kuti abwerere ndipo anapita. 25Kenaka analowa mʼnyumbamo nakayima pamaso pa mbuye wake Elisa.

Elisa anafunsa kuti, “Kodi Gehazi unali kuti?”

Iye anayankha kuti, “Mtumiki wanu sanapite kwina kulikonse.”

26Koma Elisa anati kwa Gehazi, “Kodi mzimu wanga sunali nawe pamene munthu uja anatsika mʼgaleta lake ndi kukumana nawe? Kodi ino ndi nthawi yolandira ndalama, kapena kulandira zovala, mitengo ya olivi, minda ya mpesa, nkhosa, ngʼombe kapena antchito aamuna kapena antchito aakazi? 27Khate la Naamani lidzakumatirira iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.” Ndipo Gehazi anachoka pamaso pa Elisa ali ndi khate lotuwa ngati phulusa.

New Russian Translation

4 Царств 5:1-27

Исцеление Наамана от проказы

1Нааман был военачальником царя Арама. Он был великим и уважаемым человеком в глазах своего господина, потому что через него Господь даровал Араму победу. Он был доблестным воином, но болел проказой5:1 Еврейское слово обозначает несколько различных кожных болезней; его точное значение неясно. Также в других местах книги..

2Отряды арамеев во время одного из набегов взяли в Израиле в плен маленькую девочку, и она служила жене Наамана. 3Она сказала госпоже:

– Если бы только моему господину повидать пророка, который в Самарии! Он исцелил бы его от проказы.

4Нааман пошел к господину и передал ему то, что сказала девочка из Израиля.

5– Конечно, иди, – ответил царь Арама. – Я напишу письмо царю Израиля.

И Нааман пошел, взяв с собой десять талантов5:5 Около 340 кг. серебра, шесть тысяч шекелей5:5 Около 70 кг. золота и десять смен одежды. 6В письме, которое он принес царю Израиля, говорилось: «Когда ты получишь это письмо, знай, что я послал к тебе моего слугу Наамана, чтобы ты вылечил его от проказы».

7Когда царь Израиля прочитал это письмо, он разорвал на себе одежду и сказал:

– Разве я Бог, чтобы умерщвлять и оживлять? Почему он посылает ко мне, чтобы я исцелял от проказы? Смотрите, он пытается затеять со мной ссору!

8Когда Елисей, Божий человек, услышал о том, что царь Израиля разорвал на себе одежду, он послал сказать ему:

– Почему ты разорвал на себе одежду? Пошли этого человека ко мне, и он узнает, что есть пророк в Израиле.

9Нааман пришел с конями и колесницами и остановился у двери Елисеева дома. 10Елисей отправил посланца сказать ему:

– Пойди, омойся семь раз в Иордане, твое тело исцелится, и ты станешь чист.

11Но Нааман разгневался и ушел, говоря:

– Я думал, что он непременно выйдет ко мне, встанет, призовет имя Господа, своего Бога, поводит рукой над этим местом и исцелит меня от проказы. 12Разве Авана5:12 Другое чтение: «Амана». и Фарфар, реки Дамаска, не лучше всех вод Израиля? Разве я не мог омыться в них, чтобы очиститься?

Он повернулся и в гневе ушел. 13Слуги Наамана подошли к нему и сказали:

– Отец, если бы пророк сказал тебе сделать нечто великое, разве бы ты этого не сделал? А он лишь сказал тебе: «Омойся и будешь чист».

14Тогда он пошел и семь раз окунулся в Иордане, как сказал ему Божий человек, – и его тело исцелилось и стало чистым, как у младенца. 15Нааман со слугами вернулся к Божьему человеку. Он встал перед ним и сказал:

– Теперь я знаю, что во всем мире нет Бога, кроме как в Израиле. А теперь, прошу, прими от твоего слуги подарок.

16Пророк ответил:

– Верно, как и то, что жив Господь, Которому я служу, – я ничего не приму.

И хотя Нааман уговаривал его, он отказался.

17– Если ты не желаешь, – сказал Нааман, – то прошу тебя, пусть твоему слуге дадут столько земли5:17 Большинство неизраильтян верило, что божеству можно поклоняться только на земле, принадлежащей этому божеству, или же соорудив ему жертвенник из этой земли., сколько сможет увезти пара мулов, потому что твой слуга никогда больше не будет приносить всесожжения и жертвы никакому богу, кроме Господа. 18Пусть только Господь простит твоего слугу за одно: когда мой господин входит в храм Риммона5:18 Риммон – бог-громовержец арамеев., чтобы поклониться там, и опирается на мою руку, я кланяюсь тоже. Когда я буду кланяться в храме Риммона, пусть Господь простит за это твоего слугу.

19– Иди с миром, – сказал Елисей.

Гиезий наказан проказой

Когда Нааман уже отошел на некоторое расстояние, 20Гиезий, слуга Елисея, Божьего человека, сказал себе: «Мой господин отпустил этого арамея Наамана слишком легко, не взяв у него никаких даров. Верно, как и то, что жив Господь, – я побегу за ним и возьму у него что-нибудь». 21Гиезий помчался за Нааманом. Когда Нааман увидел, как он бежит к нему, он слез с колесницы, чтобы встретить его.

– Все ли благополучно? – спросил он.

22– Все благополучно, – ответил Гиезий. – Мой господин послал меня сказать: «Два молодых ученика пророков пришли ко мне из нагорий Ефрема. Прошу тебя, дай им талант серебра5:22 Около 34 кг. и две смены одежды».

23– Конечно! Бери два таланта, – сказал Нааман.

Он уговорил Гиезия взять два таланта серебра в двух мешках, вместе с двумя сменами одежды. Он отдал их двум слугам, и они понесли их перед Гиезием. 24Когда Гиезий пришел на холм, он взял это у слуг и положил у себя дома. Он отпустил людей, и они ушли. 25После этого он вошел и встал перед своим господином Елисеем.

– Где ты был, Гиезий? – спросил Елисей.

– Твой слуга никуда не ходил, – ответил Гиезий.

26Но Елисей сказал ему:

– Разве не был с тобой мой дух, когда тот человек слез с колесницы, чтобы встретить тебя? Время ли брать деньги или принимать одежды, оливковые рощи, виноградники, отары, стада, слуг или служанок? 27Так пусть проказа Наамана пристанет к тебе и твоим потомкам навеки.

И когда Гиезий вышел от Елисея, он был бел от проказы, как снег.