2 Mafumu 4 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 4:1-44

Mafuta a Mkazi Wamasiye

1Mkazi wa mmodzi mwa ana a aneneri anafuwula kwa Elisa kuti, “Mtumiki wanu, mwamuna wanga wamwalira ndipo inu mukudziwa kuti ankaopa Yehova. Koma tsopano munthu amene mwamuna wanga anakongolako zinthu zake, akubwera kudzatenga ana anga awiri aamuna kuti akhale akapolo ake.”

2Elisa anayankha mayiyo kuti, “Kodi ufuna ndikuchitire chiyani? Tandiwuza uli ndi chiyani mʼnyumba mwako?”

Mayiyo anayankha kuti, “Mdzakazi wanu alibe kanthu kalikonse koma timafuta pangʼono chabe.”

3Elisa anati, “Pita kabwereke mitsuko yonse yopanda kanthu kwa anzako. Usakabwereke mitsuko yochepa. 4Kenaka ukalowe mʼnyumba mwako ndi kudzitsekera iwe ndi ana ako. Mukakatero mukakhuthulire mafuta mʼmitsuko yonseyo, ndipo mtsuko uliwonse ukadzaza muzikawuyika pambali.”

5Mayi uja anachoka kwa Elisa nakadzitsekera ndi ana ake. Anthu anabweretsa mitsuko kwa iye ndipo ankathiramo mafuta. 6Mitsuko yonse itadzaza, mayiyo anawuza mwana wake kuti, “Bweretsa mtsuko wina.”

Koma iye anayankha kuti, “Mitsuko yonse yatha.” Pamenepo mafuta analeka kutuluka.

7Mayiyo anapita nakamuwuza munthu wa Mulungu amene anamuyankha kuti, “Pita, kagulitse mafutawo ndipo ukabweze ngongole ija. Ndalama zotsalazo zikakhale zako ndi ana ako.”

Elisa Aukitsa Mwana wa Mayi wa ku Sunemu

8Tsiku lina Elisa anapita ku Sunemu. Kumeneko kunkakhala mayi wina wachuma amene anawumiriza Elisa kuti adye chakudya. Choncho nthawi iliyonse imene Elisa amadutsa kumeneko, ankayima ndi kudya. 9Mayiyo anawuza mwamuna wake kuti, “Taonani, ine ndikudziwa kuti munthu amene amadutsa pano nthawi zambiriyu ndi munthu woyera wa Mulungu. 10Tiyeni timumangire kachipinda kakangʼono pa denga la nyumbayi ndi kumuyikiramo bedi ndi tebulo, mpando ndi nyale. Akabwera kuno azikhala mʼmenemo.”

11Tsiku lina pamene Elisa anafika ku Sunemu, iye anakalowa mʼchipinda chake chija nagona mʼmenemo. 12Iye anati kwa mtumiki wake Gehazi, “Muyitane Msunemuyu.” Ndipo anapita kukamuyitana mayiyo, ndipo anabwera nayima pamaso pa Elisa. 13Elisa anati kwa Gehazi, “Muwuze mayiyo kuti, ‘Wavutika potichitira zonsezi. Nanga tsopano ifeyo tikuchitire chiyani? Kodi ukufuna kuti tikadziwitse mfumu kapena mtsogoleri wa ankhondo zimene watichitirazi?’ ”

Mayiyo anayankha kuti, “Ine ndimakhala mwamtendere pakati pa abale anga.”

14Elisa anafunsanso Gehazi kuti, “Kodi tingamuchitire chiyani?”

Gehazi anati, “Ndithu, mayiyu alibe mwana ndipo mwamuna wake ndi wokalamba.”

15Pamenepo Elisa anati, “Muyitane.” Choncho Gehazi anamuyitana, ndipo iye anabwera nayima pa khomo. 16Elisa anati kwa mayiyo, “Nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, udzakhala utanyamula mwana wamwamuna mʼmanja mwako.”

Mayiyo anatsutsa zimenezi nanena kuti, “Ayi mbuye wanga. Inu munthu wa Mulungu, musanamize mdzakazi wanu!”

17Koma mayi uja anakhala woyembekezera, ndipo chaka chotsatiracho, nthawi ngati yomweyo anabereka mwana wamwamuna monga momwe Elisa anamuwuzira.

18Mwana uja anakula, ndipo tsiku lina anapita kwa abambo ake amene anali ndi anthu odula tirigu. 19Mwanayo anafuwula kwa abambo ake kuti, “Mayo! Mutu wanga ine! Mayo! Mutu wanga ine!”

Abambo akewo anawuza wantchito wake kuti, “Munyamule ndi kukamupereka kwa amayi ake.” 20Wantchito uja atamunyamula ndi kumupereka kwa amayi ake. Mwanayo anakhala pa miyendo ya amayi akeyo mpaka masana, ndipo pambuyo pake anamwalira. 21Mayiyo ananyamula mwanayo nakamugoneka pa bedi la munthu wa Mulungu uja. Kenaka anatseka chitseko iye nʼkuchokapo.

22Iye anayitanitsa mwamuna wake namuwuza kuti, “Tumizireni wantchito mmodzi ndi bulu mmodzi kuti ndipite mofulumira kwa munthu wa Mulungu nʼkubwererako.”

23Mwamuna wakeyo anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani ukupita kwa iyeyo lero? Lero si tsiku la Chikondwerero cha Mwezi Watsopano kapena tsiku la Sabata.”

Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”

24Mayiyo anamangirira chishalo pa bulu ndipo anawuza wantchito wake kuti, “Yendetsa bulu mofulumira. Usachepetse liwiro pokhapokha nditakuwuza.” 25Choncho ananyamuka nakafika kwa munthu wa Mulungu uja ku Phiri la Karimeli.

Munthu wa Mulungu ataona mayiyo patali, anawuza mtumiki wake Gehazi kuti, “Taona! Msunemu uyo! 26Thamanga msanga ukakumane naye ndipo ukamufunse kuti, ‘Kodi muli bwino? Kodi mwamuna wanu ali bwino? Kodi mwana wanu ali bwino?’ ”

Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”

27Atafika kwa munthu wa Mulunguyo pa phiripo, mayiyo anagwira mapazi a Elisa. Gehazi anabwera kuti amukankhe, koma munthu wa Mulungu anati, “Musiye! Iyeyu ali pa mavuto aakulu, koma Yehova wandibisira zimenezi ndipo sanandiwuze chifukwa chake.”

28Tsono mayiyo anati, “Mbuye wanga, kodi ine ndinakupemphani mwana? Kodi sindinakuwuzeni kuti musandinamize?”

29Elisa anawuza Gehazi kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga ndodo yanga mʼdzanja lako ndipo thamanga. Ngati ukumana ndi munthu wina aliyense, usamupatse moni, ndipo ngati wina akupatsa moni, usayankhe. Ukagoneke ndodo yanga pa nkhope ya mwanayo.”

30Koma mayi wake wa mwana uja anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Choncho Elisa ananyamuka natsatira mayiyo.

31Gehazi anatsogola nakagoneka ndodoyo pa nkhope ya mwanayo, koma sipanamveke mawu kapena kugwedezeka kuonetsa kuti ali moyo. Choncho Gehazi anabwerera kukakumana ndi Elisa ndipo anamuwuza kuti, “Mwanayo sanatsitsimuke.”

32Ndipo Elisa atafika ku nyumbako, taonani, mwanayo anali wakufa atamugoneka pa bedi lake. 33Elisa analowa mʼnyumbamo natseka chitseko. Anali awiri okha mʼchipindamo ndipo iye anapemphera kwa Yehova. 34Kenaka anakwera pa bedi ndi kumugonera mwanayo, pakamwa pake panakhudzana ndi pakamwa pa mwanayo, maso ake anakhudzana ndi maso a mwanayo, ndipo manja ake anakhudzana ndi manja a mwanayo. Pamene ankadzitambalitsa yekha pa mwanayo, thupi la mwanayo linayamba kufunda. 35Elisa anatembenuka nayenda uku ndi uku kamodzi mʼchipindamo ndipo kenaka anakweranso pa bedi nagoneranso mwanayo. Mwanayo anayetsemula kasanu ndi kawiri ndipo anatsekula maso ake.

36Elisa anayitana Gehazi ndipo anati, “Muyitane Msunemuyo.” Ndipo anaterodi. Mayiyo atabwera, Elisa anati, “Tenga mwana wako.” 37Mayiyo analowa, nagwada pa mapazi a Elisa, naweramitsa mutu wake pansi. Kenaka ananyamula mwana wake natuluka.

Imfa mu Mʼphika

38Elisa anabwerera ku Giligala ndipo ku dera limenelo kunali njala. Elisa akukumana ndi ana a aneneri, anati kwa mtumiki wake, “Ika mʼphika waukulu pa moto ndipo uwaphikire chakudya anthu awa.”

39Mmodzi mwa ana aneneriwo anapita kuthengo kukafuna ndiwo ndipo anakapeza mpesa wakuthengo. Iye anathyolako zipatso zake nadzaza nsalu yake. Atabwerera, anazidula zipatsozo naziyika mu mʼphika, ngakhale kuti panalibe amene ankazidziwa. 40Anawapakulira anthu chakudyacho, koma atayamba kudya, anthuwo anafuwula kuti, “Inu munthu wa Mulungu muli imfa mu mʼphikamu!” Ndipo sakanatha kudya chakudyacho.

41Elisa anati, “Bweretsani ufa.” Iye anathira ufa mu mʼphikamo ndipo anati, “Perekani chakudyachi kwa anthu kuti adye.” Ndipo mu mʼphikamo munalibenso zoopsa.

Kudyetsa Anthu 100

42Munthu wina wochokera ku Baala-Salisa anabwera atamutengera munthu wa Mulungu malofu a barele makumi awiri opangidwa kuchokera ku zokolola zoyamba kucha, pamodzinso ndi ngala zatsopano za tirigu. Elisa anati kwa munthuyo, “Apatse anthu kuti adye.”

43Mtumiki wake anafunsa kuti, “Kodi ndikachigawe motani chakudyachi kwa anthu 100?”

Koma Elisa anamuwuzanso kuti, “Apatse anthu adye. Pakuti izi ndi zimene Yehova akunena kuti, ‘Iwo adzadya chakudyachi ndipo china chidzatsalako.’ ” 44Tsono iye anachipereka kwa anthuwo ndipo anadya china nʼkutsalako, molingana ndi mawu a Yehova.

Bibelen på hverdagsdansk

2. Kongebog 4:1-44

Elisa hjælper en enke

1En kvinde, som var enke efter en af profeterne, kom en dag hen til Elisa og sagde: „Herre, du ved selv, at min mand tjente Gud af hele sit hjerte, men han havde sat sig i gæld, og nu forlanger kreditoren, at begge mine sønner skal sælges som slaver, fordi vi ikke kan betale, hvad vi skylder ham.”

2„Hvad kan jeg gøre for dig?” spurgte Elisa. „Sig mig, hvor meget har du derhjemme?”

„Jeg har ingenting,” svarede hun, „bortset fra en lille krukke med olivenolie.”

3Så sagde Elisa: „Gå ud og lån alle de tomme beholdere, du kan, af dine naboer. 4Gå derefter hjem og luk dig inde i dit hus sammen med dine sønner. Hæld så olivenolien fra din lille krukke over i de tomme beholdere og sæt dem til side, efterhånden som de bliver fulde.”

5Det gjorde enken så. Sønnerne rakte hende beholderne, og hun fyldte dem en efter en. 6Snart var de alle fyldt til randen.

„Er der ikke flere beholdere?” spurgte hun.

„Nej, det var den sidste,” svarede de. Så kom der ikke mere olivenolie ud af hendes krukke.

7Enken gik derefter hen og fortalte det til profeten. „Gå hen og sælg olivenolien og betal din gæld,” sagde han. „De penge, der bliver tilovers, kan du og dine sønner leve af.”

Elisa opvækker en død dreng i Shunem

8Elisa kom tit igennem Shunem på sine rejser, og en af byens velstående kvinder plejede at inviterede ham til middag, hver gang han kom forbi. 9På et tidspunkt sagde kvinden til sin mand: „Jeg ved, at det er en hellig profet, som ofte spiser her. 10Jeg synes, vi skal indrette et lille gæsteværelse til ham på taget og sætte en seng, et bord, en stol4,10 Borde og stole blev dengang kun brugt i de kongelige paladser, i byrådet og hos velhavende folk, så det var noget helt særligt, denne kvinde gjorde ud af Elisa. Normalt sad folk på tæpper eller puder på gulvet og spiste. og en lampe derop, så han har sit eget værelse, når han kommer her på gennemrejse.”

11Næste gang Elisa kom på besøg, gik han op på værelset og lagde sig på sengen for at hvile sig. 12Så sagde han til sin tjener, Gehazi: „Kald på vores værtinde og sig, at jeg vil tale med hende.” Da hun indfandt sig, 13sagde Elisa til Gehazi: „Sig til hende, at vi værdsætter alt det, hun har gjort for os, og spørg hende så, om jeg kan gøre noget for hende til gengæld. Hun kan bare sige til, hvis hun ønsker, at jeg skal lægge et godt ord ind for hende hos kongen eller hos hærføreren.”

„Nej, jeg mangler ikke noget. Jeg har det godt her,” svarede hun.

14„Hvad kan vi så gøre for hende?” spurgte Elisa sin tjener. Han svarede: „Hun har ingen søn—og hendes mand er efterhånden gammel.”

15„Kald på hende igen,” beordrede Elisa.

Da hun stillede sig i døren, 16tiltalte Elisa hende direkte. „Næste år ved denne tid vil du stå med en søn på armen,” sagde han.

„Åh, du Guds profet,” indvendte hun, „giv mig ikke falske forhåbninger.”

17Men Elisas ord stod ved magt. Snart efter blev kvinden gravid, og det følgende år fødte hun en søn—nøjagtig som Elisa havde forudsagt.

18Nogle år senere var drengen en dag med sin far på høstarbejde. 19Pludselig beklagede drengen sig over en voldsom hovedpine, og faderen sagde til en af tjenerne: „Bær ham hjem til hans mor.”

20Det gjorde tjeneren, og hans mor sad med ham på skødet indtil middagstid. Da døde han. 21Så bar hun ham op i gæsteværelset, lagde drengen på profetens seng og lukkede døren, 22hvorefter hun sendte følgende besked ud til sin mand: „Send straks en tjener og et æsel hjem, så jeg kan komme af sted til profeten. Jeg er snart tilbage igen.”

23„Hvorfor vil du have fat i ham i dag?” spurgte manden tilbage. „Det er jo hverken helligdag eller sabbat.”

Hun svarede: „Tag det bare roligt.”

24Så sadlede hun æslet, satte sig op og sagde til tjeneren: „Skynd dig at trække af sted med æslet. Du skal ikke standse, før jeg siger til.”

25Da hun nærmede sig Karmels bjerg, fik Elisa øje på hende i det fjerne. „Se, det er kvinden fra Shunem, der kommer der,” sagde han til sin tjener Gehazi. 26„Løb hen og hils på hende og spørg, hvordan det går med hendes mand og den lille dreng.” Det gjorde Gehazi. „Tak, vi har det godt,” svarede kvinden tilbage.

27Men da hun nåede frem til Elisa på bjerget, faldt hun på knæ foran ham og klamrede sig til hans fødder. Gehazi prøvede at trække hende væk, men profeten sagde: „Lad hende være. Hun er i stor nød, og Herren har ikke fortalt mig, hvad der er i vejen.”

28Da sagde kvinden til Elisa: „Herre, var det mig, der bad om at få en søn? Sagde jeg ikke, at du ikke måtte give mig falske forhåbninger?”

29„Gør dig klar til at tage af sted,” sagde Elisa til Gehazi. „Tag min stav med og skynd dig hen og læg staven på drengens ansigt. Spild ikke tiden med snak undervejs.”

30Men drengens mor sagde: „Så sandt Herren lever, og du selv er i live, jeg vender ikke hjem, uden at du kommer med.” Så fulgte Elisa med hende.

31Gehazi skyndte sig at gå i forvejen, og da han kom til huset, lagde han staven på drengens ansigt, men der var intet livstegn. Så vendte Gehazi om og gik Elisa i møde: „Drengen kom ikke til live,” sagde han.

32Da Elisa kom ind i huset, så han den døde dreng, som lå på hans seng. 33Han gik ind i værelset og lukkede døren. Så bad han til Herren, 34og da han havde bedt, lagde han sig hen over drengen—med sin mund på drengens mund, med sine øjne over drengens øjne og med sine hænder på drengens hænder. Da begyndte varmen at vende tilbage i drengens krop. 35Så rejste Elisa sig og gik frem og tilbage i værelset. Derefter lagde han sig igen hen over drengen som før. Denne gang nyste drengen syv gange og slog øjnene op.

36Derpå sagde profeten til Gehazi: „Kald på kvinden.” Da drengens mor kom ind i værelset, sagde Elisa: „Her er din søn.” 37Da faldt hun på knæ foran Elisa, hvorefter hun tog sin søn og gik ud.

Profeteleverne oplever to mirakler

38Elisa vendte derefter tilbage til Gilgal. På den tid var der hungersnød i landet. En dag, da han havde undervist profeteleverne, sagde han til Gehazi: „Sæt den store gryde på ilden og lav en ret mad til de unge mennesker.”

39En af eleverne gik ud for at samle urter og fandt en vild slyngplante med agurklignende frugter. Han plukkede så mange af de ukendte frugter, han kunne bære i sin kappe. Da han kom tilbage, skar han dem i stykker og kom dem i gryden. 40Men så snart mændene smagte maden, råbte de forfærdet: „Mester, maden er giftig.”

41„Skaf mig noget mel,” befalede Elisa. Da han havde hældt melet i gryden, sagde han: „Nu kan I godt spise det.” Og ingen af dem blev syge.

42En dag kom en mand fra Ba’al-Shalisha til Elisa med en sæk nyhøstede bygkerner og 20 små brød, der var lavet af årets første byghøst. Elisa bad Gehazi om at servere brødene for profeteleverne.

43„Hvordan skal jeg kunne mætte hundrede mennesker med den smule mad?” indvendte Gehazi.

„Gør nu, som jeg har sagt,” vedblev Elisa, „for Herren siger, at der vil være rigeligt til alle og tilmed blive noget til overs.”

44Og ganske rigtigt. Som Herren havde sagt, sådan gik det.