2 Mafumu 22 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 22:1-20

Buku la Malamulo Lipezeka

1Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati. 2Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.

3Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati, 4“Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu. 5Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova, 6amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova. 7Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”

8Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga. 9Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.” 10Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.

11Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake. 12Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti, 13“Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”

14Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.

15Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti, 16‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga. 17Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’ 18Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva: 19Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova. 20Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’ ”

Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.

New Russian Translation

4 Царств 22:1-20

Иосия – царь Иудеи

(2 Пар. 34:1-2, 8-13)

1Иосии было восемь лет, когда он стал царем, и правил он в Иерусалиме тридцать один год. Его мать звали Иедида, она была дочерью Адаи, родом из Боцката. 2Иосия делал то, что было правильным в глазах Господа, и ходил всеми путями своего предка Давида, не уклоняясь ни вправо, ни влево.

3На восемнадцатом году своего правления царь Иосия послал писаря Шафана, сына Ацалии, внука Мешуллама, в дом Господа, сказав:

4– Ступай к первосвященнику Хелкии, пусть он пересчитает деньги, принесенные в дом Господа, которые привратники собрали у народа. 5Пусть их отдадут людям, которые были назначены наблюдать за работами при доме, а они пусть заплатят рабочим, которые ремонтируют дом Господа, – 6плотникам, строителям и каменщикам. Пусть они также покупают дерево и тесаный камень, чтобы восстанавливать дом. 7Отчета за доверенные им деньги с них требовать не нужно, потому что они действуют честно.

Книга Закона найдена в храме

(2 Пар. 34:14-28)

8Первосвященник Хелкия сказал писарю Шафану:

– Я нашел в доме Господа книгу Закона22:8 Вероятно первосвященник нашел весь Закон, но, возможно, это было лишь Второзаконие, последняя часть Пятикнижия (см. Втор. 31:24-26)..

Он отдал ее Шафану, и тот ее прочитал. 9После этого писарь Шафан пришел к царю и доложил ему:

– Твои слуги взяли деньги, какие нашлись в доме Господа, и передали их наблюдателям за работами и работникам.

10Затем писарь Шафан сказал царю:

– Священник Хелкия дал мне одну книгу.

И Шафан стал читать из нее перед царем.

11Услышав слова из книги Закона, царь разорвал на себе одежду. 12Он приказал священнику Хелкии, Ахикаму, сыну Шафана, Ахбору, сыну Михая, писарю Шафану и царскому слуге Асаи:

13– Идите, вопросите Господа за меня, за народ и за всю Иудею о том, что написано в найденной книге. Велик Господень гнев, который обрушился на нас из-за того, что наши отцы не слушали слов этой книги, они не поступали так, как она предписывает нам.

14И священник Хелкия, Ахикам, Ахбор, Шафан и Асая пошли к пророчице Олдане, жене Шаллума, сына Тиквы, внука Хархаса, хранителя одежд. Она жила в Иерусалиме, во Втором округе. 15Она сказала им:

– Так говорит Господь, Бог Израиля: «Скажите человеку, который послал вас ко Мне: 16„Так говорит Господь: Я наведу на это место и на его обитателей беду, как написано в книге, которую читал царь Иудеи. 17Из-за того, что они оставили Меня, возжигали благовония другим богам и вызывали Мой гнев всем, что сделали их руки, Мой гнев на это место вспыхнет и не угаснет“. 18Скажите царю Иудеи, который послал вас вопросить Господа: „Так говорит Господь, Бог Израиля, о словах, которые ты слышал: 19Так как твое сердце смягчилось и ты смирил себя перед Господом, услышав, как Я сказал против этого места и его обитателей, что им суждены опустошение и проклятие, и так как ты разорвал свои одежды и плакал предо Мной, то и Я услышал тебя, – возвещает Господь. – 20Поэтому Я возьму тебя к твоим отцам, и тебя похоронят в мире. Твои глаза не увидят всей той беды, которую Я наведу на это место“».

И они передали ее ответ царю.