2 Mafumu 22 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 22:1-20

Buku la Malamulo Lipezeka

1Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati. 2Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.

3Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati, 4“Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu. 5Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova, 6amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova. 7Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”

8Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga. 9Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.” 10Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.

11Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake. 12Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti, 13“Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”

14Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.

15Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti, 16‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga. 17Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’ 18Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva: 19Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova. 20Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’ ”

Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.

New International Version – UK

2 Kings 22:1-20

The Book of the Law found

1Josiah was eight years old when he became king, and he reigned in Jerusalem for thirty-one years. His mother’s name was Jedidah daughter of Adaiah; she was from Bozkath. 2He did what was right in the eyes of the Lord and followed completely the ways of his father David, not turning aside to the right or to the left.

3In the eighteenth year of his reign, King Josiah sent the secretary, Shaphan son of Azaliah, the son of Meshullam, to the temple of the Lord. He said: 4‘Go up to Hilkiah the high priest and make him get ready the money that has been brought into the temple of the Lord, which the doorkeepers have collected from the people. 5Make them entrust it to the men appointed to supervise the work on the temple. And make these men pay the workers who repair the temple of the Lord6the carpenters, the builders and the masons. Also make them purchase timber and dressed stone to repair the temple. 7But they need not account for the money entrusted to them, because they are honest in their dealings.’

8Hilkiah the high priest said to Shaphan the secretary, ‘I have found the Book of the Law in the temple of the Lord.’ He gave it to Shaphan, who read it. 9Then Shaphan the secretary went to the king and reported to him: ‘Your officials have paid out the money that was in the temple of the Lord and have entrusted it to the workers and supervisors at the temple.’ 10Then Shaphan the secretary informed the king, ‘Hilkiah the priest has given me a book.’ And Shaphan read from it in the presence of the king.

11When the king heard the words of the Book of the Law, he tore his robes. 12He gave these orders to Hilkiah the priest, Ahikam son of Shaphan, Akbor son of Micaiah, Shaphan the secretary and Asaiah the king’s attendant: 13‘Go and enquire of the Lord for me and for the people and for all Judah about what is written in this book that has been found. Great is the Lord’s anger that burns against us because those who have gone before us have not obeyed the words of this book; they have not acted in accordance with all that is written there concerning us.’

14Hilkiah the priest, Ahikam, Akbor, Shaphan and Asaiah went to speak to the prophet Huldah, who was the wife of Shallum son of Tikvah, the son of Harhas, keeper of the wardrobe. She lived in Jerusalem, in the New Quarter.

15She said to them, ‘This is what the Lord, the God of Israel, says: tell the man who sent you to me, 16“This is what the Lord says: I am going to bring disaster on this place and its people, according to everything written in the book the king of Judah has read. 17Because they have forsaken me and burned incense to other gods and aroused my anger by all the idols their hands have made,22:17 Or by everything they have done my anger will burn against this place and will not be quenched.” 18Tell the king of Judah, who sent you to enquire of the Lord, “This is what the Lord, the God of Israel, says concerning the words you heard: 19because your heart was responsive and you humbled yourself before the Lord when you heard what I have spoken against this place and its people – that they would become a curse22:19 That is, their names would be used in cursing (see Jer. 29:22); or, others would see that they are cursed. and be laid waste – and because you tore your robes and wept in my presence, I also have heard you, declares the Lord. 20Therefore I will gather you to your ancestors, and you will be buried in peace. Your eyes will not see all the disaster I am going to bring on this place.” ’

So they took her answer back to the king.