2 Mafumu 21 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 21:1-26

Manase Mfumu ya Yuda

1Manase anakhala mfumu ali ndi zaka khumi ndi ziwiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 55. Amayi ake anali Hefiziba. 2Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira mchitidwe wonyansa wa mitundu imene Yehova anayipirikitsa pofika Aisraeli. 3Iyetu anamanganso malo opembedzera mafano amene Hezekiya abambo ake anawawononga. Anamangira Baala maguwa a nsembe ndi mtengo wa fano la Asera monga anachitira Ahabu mfumu ya Israeli ndipo ankapembedza zolengedwa zonse zamlengalenga. 4Anamanga maguwa ansembewa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Mu Yerusalemu ndidzayikamo Dzina langa.” 5Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova, Manase anamangamo maguwa opembedzerapo zinthu zamlengalenga. 6Iye anapsereza mwana wake pa moto ngati nsembe, ankachita za matsenga, ankawombeza mawula, ankapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndiponso ankapembedza mizimu. Iyeyo anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova ndipo anakwiyitsa Yehovayo.

7Iye anatenga fano losema la Asera limene analipanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Yehova, Nyumba imene Yehova ananena kwa Davide ndi mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba iyi ndi mu Yerusalemu ndiwo malo amene ndasankha pakati pa mafuko onse a Aisraeli kuyikamo Dzina langa kwamuyaya. 8Sindidzalola kuti Aisraeli achotsedwe mʼdziko lawo limene ndinapatsa makolo awo ngati iwowo adzasamala kuchita zinthu zonse zimene ndinawalamula ndi kusunga malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anawapatsa.” 9Koma anthu sanamvere. Manase anawasocheretsa, kotero kuti anachita zoyipa zambiri kupambana anthu a mitundu ina amene Yehova anawawononga pamene Aisraeli ankafika.

10Yehova anayankhula kudzera mwa atumiki ake, aneneri kuti, 11“Manase mfumu ya Yuda wachita machimo onyansawa ndipo wachita zoyipa kupambana Aamori amene analipo kale iye asanabadwe ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda ndi mafano ake. 12Choncho Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taonani, ndikubweretsa pa Yerusalemu ndi Yuda mavuto akuti aliyense amene adzawamve adzathedwa nzeru. 13Ndidzalanga Yerusalemu ndi Yuda pogwiritsa ntchito muyeso umene ndinalangira Samariya ndi Ahabu pamodzi ndi nyumba yake. Ndidzayeretsa Yerusalemu monga mmene munthu amachitira popukuta mbale ndipo atayipukuta amayivundikira pansi. 14Ndidzawataya anthu otsala amene ndi cholowa changa ndipo ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo. Adzachotsedwa ndipo adaniwo adzawalanda zinthu zonse 15chifukwa anachita zoyipa pamaso panga ndipo akhala akundikwiyitsa kuchokera tsiku limene makolo awo anatuluka mu Igupto mpaka lero lino.’ ”

16Kuwonjezera apo, Manase anakhetsa kwambiri magazi a anthu osalakwa mpaka magaziwo kuyenderera mu Yerusalemu kuyambira mbali ina mpaka mbali ina, kuphatikiza pa kuchimwitsa Yuda, kotero kuti anthu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.

17Ntchito zina za Manase ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? 18Manase anagona ndi makolo ake ndipo anayikidwa mʼmanda mʼmunda wa Uza, ku nyumba yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Amoni Mfumu ya Yuda

19Amoni anakhala mfumu ali ndi zaka 22 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka ziwiri. Amayi ake anali Mesulemeti mwana wa Haruzi, wochokera ku Yotiba. 20Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Manase abambo ake. 21Anatsatira makhalidwe onse a abambo ake. Ankapembedza mafano amene abambo akewo ankawapembedza ndipo ankawagwadira. 22Iyeyo anasiya Yehova Mulungu wa makolo ake ndipo sanayende mʼnjira ya Yehova.

23Nduna za Amoni zinamuchita chiwembu ndipo zinamupha mʼnyumba yake. 24Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anachitira chiwembu Mfumu Amoni, nayika Yosiya mwana wake kukhala mfumu mʼmalo mwake.

25Ntchito zina za Amoni ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? 26Iye anayikidwa mʼmanda ake mʼmunda wa Uza. Ndipo Yosiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

New Russian Translation

4 Царств 21:1-26

Манассия – царь Иудеи

(2 Пар. 33:1-10, 18-20)

1Манассии было двенадцать лет, когда он стал царем, и правил он в Иерусалиме пятьдесят пять лет. Его мать звали Хефциба. 2Он делал зло в глазах Господа, следуя омерзительным обычаям народов, которых Господь прогнал от израильтян. 3Он отстроил святилища на возвышенностях, которые разрушил его отец Езекия, воздвиг жертвенники Баалу и сделал столб Ашеры, по примеру Ахава, царя Израиля. Он поклонялся всему небесному воинству и служил ему, 4построил жертвенники в доме Господа, о котором Господь сказал: «В Иерусалиме Я помещу Мое имя». 5В обоих дворах дома Господа он построил жертвенники всему небесному воинству. 6Он принес сына в огненную жертву, гадал, и ворожил, и общался с вызывателями умерших и волшебниками. Он сделал много зла в глазах Господа, вызывая Его гнев.

7Он взял резной столб Ашеры, который сделал, и поставил его в доме, о котором Господь говорил Давиду и его сыну Соломону: «В этом доме и в Иерусалиме, который Я избрал среди всех родов Израиля, Я помещу Мое имя навеки. 8Я не дам впредь ногам израильтян выйти из той земли, которую Я дал их отцам, если только они будут исполнять все, что Я повелел им, и соблюдать Закон, который дал им Мой слуга Моисей».

9Но народ не послушал. Манассия сбил их с пути, и они стали делать больше зла, чем те народы, которых Господь истребил перед израильтянами. 10Господь говорил через Своих слуг пророков:

11– Манассия, царь Иудеи, совершил омерзительные грехи. Он сделал больше зла, чем аморреи, которые были перед ним, и ввел Иудею в грех своими идолами. 12Поэтому так говорит Господь, Бог Израиля: «Я наведу на Иерусалим и Иудею такую беду, что у того, кто услышит о ней, зазвенит в ушах. 13Я отмерю наказание Иерусалиму, так же, как отмерил Самарии, и буду пользоваться такой же мерой праведности, как и для дома Ахава21:13 Букв.: «Я протяну над Иерусалимом мерную нить Самарии и свинцовый отвес дома Ахава». Мерная нить и свинцовый отвес, обычно используемые в строительстве, здесь становятся символами разрушения.. Я вытру Иерусалим, как вытирают блюдо – вытирают и переворачивают. 14Я покину оставшихся от Моего наследия и отдам их в руки врагов. Все их враги будут обирать их и грабить, 15потому что они делали зло в Моих глазах и вызывали Мой гнев с того дня, как их отцы вышли из Египта, по сегодняшний день».

16Манассия пролил столько безвинной крови, что наполнил Иерусалим от края до края, – и это не считая греха, к которому он склонил Иудею, чтобы они делали зло в глазах Господа.

17Что же до прочих событий правления Манассии и всего, что он сделал, и греха, который он совершил, то разве не записаны они в «Книге летописей царей Иудеи»? 18Манассия упокоился со своими предками и был похоронен в саду своего дворца, в саду Уззы. И Амон, его сын, стал царем вместо него.

Амон – царь Иудеи

(2 Пар. 33:21-25)

19Амону было двадцать два года, когда он стал царем, и правил он в Иерусалиме два года. Его мать звали Мешуллемет, она была дочерью Харуца, родом из Иотбы. 20Амон делал зло в глазах Господа, как и его отец Манассия. 21Он ходил всеми путями своего отца, служил идолам, которым служил его отец, и поклонялся им. 22Он оставил Господа, Бога его отцов, и не ходил путем Господа.

23Приближенные Амона составили против него заговор и убили царя в его дворце. 24Но народ страны перебил всех, кто был в заговоре против царя Амона, и сделал царем вместо него его сына Иосию.

25Что же до прочих деяний Амона, то разве не записаны они в «Книге летописей царей Иудеи»? 26Его похоронили в его гробнице в саду Уззы. И Иосия, его сын, стал царем вместо него.