2 Mafumu 20 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 20:1-21

Kudwala kwa Hezekiya

1Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”

2Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, 3“Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.

4Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti, 5“Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova. 6Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’ ”

7Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.

8Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”

9Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”

10Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”

11Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.

Akazembe Ochokera ku Babuloni

12Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo. 13Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.

14Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?”

Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”

15Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?”

Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”

16Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena: 17Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova. 18Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”

19Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’ ”

20Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? 21Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

New Russian Translation

4 Царств 20:1-21

Болезнь и исцеление Езекии

(2 Пар. 32:24; Ис. 38:1-8, 21-22)

1В те дни Езекия заболел и был при смерти. Пророк Исаия, сын Амоца, пришел к нему и сказал:

– Так говорит Господь: «Распорядись своим домом, потому что ты умираешь; ты не выздоровеешь».

2Езекия отвернулся лицом к стене и взмолился Господу:

3– Вспомни, о Господи, как я ходил пред Тобой в верности и от всего сердца и делал то, что было угодным в Твоих глазах!

И Езекия горько заплакал.

4Прежде чем Исаия успел пройти средний двор, к нему было слово Господа:

5– Возвратись и скажи Езекии, вождю Моего народа: «Так говорит Господь, Бог твоего предка Давида: Я услышал твою молитву и увидел твои слезы; Я исцелю тебя. На третий день ты пойдешь в дом Господа. 6Я прибавлю к твоей жизни пятнадцать лет. Я избавлю тебя и этот город от руки царя Ассирии. Я защищу этот город ради Себя и ради Моего слуги Давида».

7Исаия сказал:

– Сделайте царю пласт инжира.

Они взяли, приложили его к нарыву, и царь выздоровел. 8Тогда Езекия спросил Исаию:

– Каково знамение того, что Господь исцелит меня и я пойду на третий день в Господень дом?

9Исаия ответил:

– Вот тебе знамение от Господа, что Господь исполнит то, что обещал: скажи, пройти ли тени десять ступенек вперед или отступить на десять ступенек назад?

10– Тени легко пройти на десять ступенек вперед, – сказал Езекия. – Нет, пусть она отступит на десять ступенек назад.

11Пророк Исаия воззвал к Господу, и Господь отвел тень назад на те десять ступенек, что она спустилась по лестнице Ахаза.

Немудрый поступок Езекии

(Ис. 39:1-8)

12В то время вавилонский царь Меродах-Баладан20:12 Так в ряде древних переводов (ср. также Ис. 39:1); в нормативном еврейском тексте: «Беродах-Баладан»., сын Баладана, отправил Езекии письма и подарок, потому что услышал о его болезни. 13Езекия радушно принял20:13 Или: «выслушал». послов и показал им все, что было у него в хранилищах, – серебро, золото, пряности и драгоценные масла, – и свою оружейную палату, и все, что хранилось в его сокровищницах. Ни во дворце, ни во всем его царстве не осталось ничего такого, чего бы он им не показал.

14Пророк Исаия пришел к царю и спросил:

– Что говорили эти люди и откуда они к тебе приходили?

– Из далекой страны, – ответил Езекия. – Они приходили из Вавилона.

15Пророк спросил:

– Что они видели у тебя во дворце?

– У меня во дворце они видели все, – ответил Езекия. – В моих сокровищницах нет ничего, чего бы я им не показал.

16Тогда Исаия сказал Езекии:

– Слушай слово Господа: 17«Непременно наступит время, когда все, что у тебя во дворце, и все, что накопили до сегодняшнего дня твои отцы, будет унесено в Вавилон. Не останется ничего, – говорит Господь. – 18А некоторые из твоих потомков, которые родятся у тебя, твоя плоть и кровь, будут уведены и станут евнухами во дворце царя Вавилона».

19– Слово Господа, которое ты передал, хорошее, – ответил Езекия и подумал20:19 Букв.: «сказал».: «Ну и что, раз в мои дни будут мир и безопасность?»

Смерть Езекии

(2 Пар. 32:32-33)

20Что же до прочих событий правления Езекии, всех его свершений, включая то, как он сделал пруд и водопровод, по которому провел воду в город, то разве не записаны они в «Книге летописей царей Иудеи»?

21Езекия упокоился со своими предками, и Манассия, его сын, стал царем вместо него.