2 Mafumu 19 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 19:1-37

Kupulumutsidwa kwa Yerusalemu

1Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova. 2Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi. 3Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera. 4Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’ ”

5Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya, 6Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine. 7Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’ ”

8Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.

9Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa: 10“Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’ 11Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka? 12Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa? 13Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”

Pemphero la Hezekiya

14Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova. 15Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi. 16Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.

17“Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo. 18Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu. 19Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”

Yankho la Mulungu Kudzera mwa Yesaya

20Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’ ” 21Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa:

“Namwali wa Ziyoni

akukunyoza ndi kukuseka iwe.

Mwana wamkazi wa Yerusalemu

akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.

22Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani?

Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako

ndi kumuyangʼana monyada?

Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!

23Kudzera mwa amithenga ako

wonyoza Ambuye.

Ndipo wanena kuti,

‘Ndi magaleta ochuluka

ndinakwera mapiri ataliatali,

pa msonga za mapiri a Lebanoni.

Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri,

mitengo yake ya payini yabwino kwambiri.

Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni,

mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.

24Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo

ndipo ndinamwa madzi a kumeneko.

Ndi mapazi anga

ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’ ”

25“ ‘Kodi sunamvepo?

Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale.

Ndinazikonzeratu masiku amakedzana;

tsopano ndachita kuti zichitikedi,

iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa

kukhala milu ya miyala.

26Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu,

athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi.

Ali ngati mbewu za mʼmunda,

ngati udzu wanthete,

ali ngati udzu womera pa denga,

umene umawuma usanakule nʼkomwe.’ ”

27“ ‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako,

kutuluka kwako ndi kulowa kwako,

ndi mkwiyo wako pa Ine.

28Chifukwa chakuti wandikwiyira

ndipo ndamva za mwano wako,

ndidzakola mphuno yako ndi mbedza

ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako,

ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa

njira yomwe unadzera pobwera.’

29“Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi:

“Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa,

ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera.

Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola,

mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.

30Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale

adzazika mizu ndi kubereka zipatso.

31Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala,

ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.”

“Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.

32“Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi:

“ ‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu

kapena kuponyamo muvi.

Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake

kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.

33Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera;

sadzalowa mu mzinda umenewu,

akutero Yehova.

34Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa,

chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’ ”

35Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda! 36Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.

37Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

2 Reyes 19:1-37

Isaías profetiza la liberación de Jerusalén

19:1-13Is 37:1-13

1Cuando el rey Ezequías escuchó esto, se rasgó las vestiduras, se vistió de luto y fue al templo del Señor. 2Además, envió a Eliaquín, administrador del palacio, al cronista Sebna y a los sacerdotes más ancianos, todos vestidos de luto, para hablar con el profeta Isaías hijo de Amoz. 3Y le dijeron: «Así dice Ezequías: “Hoy es un día de angustia, castigo y deshonra, como cuando los hijos están a punto de nacer y no se tienen fuerzas para dar a luz. 4Tal vez el Señor tu Dios oiga todas las palabras del comandante en jefe, a quien su señor, el rey de Asiria, envió para insultar al Dios viviente. ¡Que el Señor tu Dios lo castigue por las palabras que ha oído! Eleva, pues, una oración por el remanente del pueblo que aún sobrevive”».

5Cuando los funcionarios del rey Ezequías fueron a ver a Isaías, 6este les dijo: «Decidle a vuestro señor que así dice el Señor: “No temas por las blasfemias que has oído, pronunciadas contra mí por los subalternos del rey de Asiria. 7¡Mira! Voy a poner un espíritu en él, para que cuando oiga cierto rumor regrese a su propio país. ¡Allí haré que lo maten a filo de espada!”»

8Cuando el comandante en jefe se enteró de que el rey de Asiria había salido de Laquis, se retiró y encontró al rey luchando contra Libná.

9Luego Senaquerib recibió el informe de que Tiracá, rey de Cus, había salido para luchar contra él, así que una vez más envió mensajeros a Ezequías 10para que le dijeran: «Tú, Ezequías, rey de Judá: No dejes que tu Dios, en quien confías, te engañe cuando dice: “No caerá Jerusalén en manos del rey de Asiria”. 11Sin duda te habrás enterado de lo que han hecho los reyes de Asiria en todos los países, destruyéndolos por completo. ¿Y acaso vas a librarte tú? 12¿Libraron sus dioses a las naciones que mis antepasados han destruido: Gozán, Jarán, Résef y la gente de Edén que vivía en Telasar? 13¿Dónde están el rey de Jamat, el rey de Arfad, el rey de la ciudad de Sefarvayin, o de Hená o Ivá?»

Oración de Ezequías

19:14-19Is 37:14-20

14Ezequías tomó la carta de mano de los mensajeros y la leyó. Luego subió al templo del Señor, la desplegó delante del Señor, 15y en su presencia oró así: «Señor, Dios de Israel, entronizado sobre los querubines: solo tú eres el Dios de todos los reinos de la tierra. Tú has hecho los cielos y la tierra. 16Presta atención, Señor, y escucha; abre tus ojos, Señor, y mira; escucha las palabras que Senaquerib ha mandado a decir para insultar al Dios viviente.

17»Es verdad, Señor, que los reyes asirios han asolado todas estas naciones y sus tierras. 18Han arrojado al fuego sus dioses y los han destruido, porque no eran dioses, sino solo madera y piedra, obra de manos humanas. 19Ahora, pues, Señor y Dios nuestro, por favor, sálvanos de su mano, para que todos los reinos de la tierra sepan que solo tú, Señor, eres Dios».

Muerte de Senaquerib

19:20-37Is 37:21-38

19:35-372Cr 32:20-21

20Entonces Isaías hijo de Amoz le envió este mensaje a Ezequías: «Así dice el Señor, Dios de Israel: “Por cuanto me has rogado respecto a Senaquerib, rey de Asiria, te he escuchado. 21Esta es la palabra que yo, el Señor, he pronunciado contra él:

»”La virginal hija de Sión

te desprecia y se burla de ti.

La hija de Jerusalén

menea la cabeza al verte huir.

22¿A quién has insultado?

¿Contra quién has blasfemado?

¿Contra quién has alzado la voz

y levantado los ojos con orgullo?

¡Contra el Santo de Israel!

23Has enviado a tus mensajeros

a insultar al Señor, diciendo:

‘Con mis numerosos carros de combate

escalé las cumbres de las montañas,

¡las laderas del Líbano!

Talé sus cedros más altos,

sus cipreses más selectos.

Alcancé sus refugios más lejanos,

y sus bosques más frondosos.

24Cavé pozos en tierras extranjeras,

y en esas aguas apagué mi sed.

Con las plantas de mis pies

sequé todos los ríos de Egipto’.

25»”¿No te has dado cuenta?

¡Hace mucho tiempo que lo he preparado!

Desde tiempo atrás lo vengo planeando,

y ahora lo he llevado a cabo;

por eso tú has dejado en ruinas

las ciudades fortificadas.

26Sus habitantes, impotentes,

están desalentados y avergonzados.

Son como plantas en el campo,

como tiernos pastos verdes,

como hierba que brota sobre el techo

y que se quema antes de crecer.

27»”Yo sé bien cuándo te sientas,

cuándo sales, cuándo entras,

y cuánto ruges contra mí.

28Porque has rugido contra mí

y tu insolencia ha llegado a mis oídos,

te pondré una argolla en la nariz

y un freno en la boca,

y por el mismo camino por donde viniste

te haré regresar.

29»”Esta será la señal para ti, Ezequías:

»”Este año comeréis lo que crezca por sí solo,

y el segundo año lo que de allí brote.

Pero al tercer año sembraréis y cosecharéis,

plantaréis viñas y comeréis su fruto.

30Una vez más los sobrevivientes de la tribu de Judá

echarán raíces abajo, y arriba darán fruto.

31Porque de Jerusalén saldrá un remanente,

del monte Sión un grupo de sobrevivientes.

Esto lo hará mi celo,

celo del Señor Todopoderoso.

32»”Yo, el Señor, declaro esto acerca del rey de Asiria:

»”No entrará en esta ciudad

ni lanzará contra ella una sola flecha.

No se enfrentará a ella con escudos

ni construirá contra ella una rampa de asalto.

33Volverá por el mismo camino que vino;

¡en esta ciudad no entrará!

Yo, el Señor, lo afirmo.

34Por mi causa y por consideración a David mi siervo

defenderé esta ciudad y la salvaré”».

35Esa misma noche, el ángel del Señor salió y mató a ciento ochenta y cinco mil hombres del campamento asirio. A la mañana siguiente, cuando los demás se levantaron, ¡allí estaban tendidos todos los cadáveres! 36Así que Senaquerib, rey de Asiria, levantó el campamento y se retiró. Volvió a Nínive y permaneció allí. 37Pero un día, mientras adoraba en el templo de su dios Nisroc, sus hijos Adramélec y Sarézer lo mataron a espada y escaparon a la tierra de Ararat. Y su hijo Esarjadón le sucedió en el trono.