2 Mafumu 18 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 18:1-37

Hezekiya Mfumu ya Yuda

1Mʼchaka chachitatu cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Hezekiya mwana wa Ahazi mfumu ya Yuda analowa ufumu. 2Anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Abi, mwana wa Zekariya. 3Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake. 4Anachotsa malo opembedzerako mafano, anaphwanya miyala yachipembedzo ndiponso anadula mafano a Asera. Iye anaphwanya njoka yamkuwa imene Mose anapanga, pakuti mpaka kufikira nthawi imeneyi Aisraeli amafukiza lubani kwa njoka imeneyi. (Imatchedwa Nehusitani).

5Hezekiya anadalira Yehova Mulungu wa Israeli. Kotero panalibe wina wofanana naye pakati pa mafumu onse a Yuda, asanakhale mfumu kapena atakhala kale mfumu. 6Iye anakangamira Yehova ndipo sanamusiye koma anasunga malamulo amene Yehova anapatsa Mose. 7Ndipo Yehova anali naye ndipo kulikonse kumene anapita zinthu zinkamuyendera bwino. Iye anagalukira mfumu ya ku Asiriya ndipo sanayitumikirenso. 8Iye anakantha Afilisti kuyambira ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa. Anakafika mpaka ku Gaza ndi ku malire ake.

9Mʼchaka chachinayi cha Mfumu Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chiwiri cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Salimenezeri, mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Samariya ndi kuwuzinga 10Asiriya analanda mzindawu patatha zaka zitatu. Choncho mzinda wa Samariya unalandidwa chaka chachisanu ndi chimodzi cha Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya mfumu ya Israeli. 11Mfumu ya ku Asiriya inatenga Aisraeli kupita nawo ku ukapolo ku Asiriya ndipo anakawakhazika ku Hala, ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi. 12Izi zinachitika chifukwa sanamvere zonena za Yehova Mulungu wawo, koma anaphwanya pangano lake ndi zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anawalamula. Iwo sanamvere malamulowo kapena kuwagwiritsa ntchito.

13Mʼchaka chakhumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, nayilanda. 14Choncho Hezekiya mfumu ya Yuda anatumiza uthenga kwa mfumu ya ku Asiriya ku Lakisi wonena kuti, “Ine ndalakwa. Chokani kuno ndipo ndidzakupatsani chilichonse chimene munene.” Mfumu ya ku Asiriya inalamula mfumu Hezekiya, mfumu ya Yuda, kuti azipereka makilogalamu a siliva okwana 3,000 ndi makilogalamu a golide 1,000. 15Mfumu Hezekiya inapereka siliva yense amene anapezeka mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba zosungiramo chuma cha mfumu.

16Nthawi imeneyi Hezekiya mfumu ya Yuda anakanganula golide amene anakuta zitseko ndi mphuthu za chipata cha Nyumba ya Yehova namupereka kwa mfumu ya ku Asiriya.

Senakeribu Aopseza Yerusalemu

17Mfumu ya ku Asiriya inatuma Taritani, Rabusarisi ndi Rabusake pamodzi ndi gulu lalikulu la ankhondo, kwa Mfumu Hezekiya ku Yerusalemu kuchokera ku Lakisi. Iwo anafika ku Yerusalemu nakayima pafupi ndi ngalande ya madzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu waukulu wopita ku malo a Munda wa Mmisiri Wochapa. 18Iwo anayitana mfumu, ndipo Eliyakimu mwana wa Hilikiya woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa anthuwo.

19Ndipo Rabusake anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti,

“ ‘Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, ‘Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?’ 20Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine? 21Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.’ ” 22Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, “Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu.” Kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, “Muzipembedza pa guwa lansembe ili mu Yerusalemu?”

23“ ‘Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo! 24Ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo? 25Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga malo ano popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.’ ”

26Pamenepo Eliyakimu mwana wa Hilikiya, Sebina ndi Yowa anawuza Rabusakeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”

27Koma Rabusake anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”

28Tsono Rabusake anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya! 29Zimene mfumu ikunena ndi izi: ‘Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni mʼdzanja langa. 30Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’

31“ ‘Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake, 32mpaka nditabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanuli, dziko la tirigu ndi vinyo watsopano, dziko la chakudya ndi minda ya mipesa, dziko la mitengo ya olivi ndi uchi. Sankhani moyo osati imfa!

“Musamvere zonena Hezekiya, pakuti iye akukusocheretsani ponena kuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ 33Kodi mulungu wa anthu a mtundu wina uliwonse wapulumutsapo dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya? 34Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu, Hena ndi Ivani? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa? 35Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja langa? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”

36Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”

37Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu, mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza Hezekiya zonse zimene anayankhula Rabusake uja.

New Russian Translation

4 Царств 18:1-37

Езекия – царь Иудеи

(2 Пар. 29:1-2; 31:1, 20-21)

1На третьем году правления царя Израиля Осии, сына Элы, в Иудее начал царствовать Езекия, сын Ахаза. 2Ему было двадцать пять лет, когда он стал царем, и правил он в Иерусалиме двадцать девять лет. Его мать звали Ави18:2 Вариант имени Авия., она была дочерью Захарии. 3Он делал то, что было правильным в глазах Господа, как и его предок Давид. 4Он убрал святилища на возвышенностях, разбил священные камни и срубил столбы Ашеры. Он разломал на куски бронзового змея, которого сделал Моисей, потому что до того самого времени израильтяне возжигали перед ним благовония. Он назывался Нехуштан18:4 По-еврейски это название означает «медный змей». См. Чис. 21:4-9..

5Езекия доверял Господу, Богу Израиля. Не было подобного ему среди всех царей Иудеи ни до него, ни после него. 6Он крепко держался Господа и неотступно следовал за Ним; он исполнял повеления, которые Господь дал через Моисея. 7И Господь был с ним: он преуспевал во всем, за что бы ни брался. Он восстал против царя Ассирии и отказался ему служить. 8Он бил филистимлян до самого города Газы и ее окрестностей, от сторожевой башни до укрепленного города.

Ассирийцы захватывают Самарию

(4 Цар. 17:5-7)

9На четвертом году правления царя Езекии – седьмом году правления Осии, сына Элы, царя Израиля, – Салманассар, царь Ассирии, двинулся на Самарию и осадил ее. 10Через три года ассирийцы взяли ее. Так на шестом году правления Езекии – девятом году правления Осии, царя Израиля, – была взята Самария. 11Царь Ассирии увел Израиль в плен в свою страну и поселил их в Халахе, в Гозане, что на реке Хаворе, и в городах мидян. 12Это произошло потому, что они не слушали Господа, своего Бога, но нарушили Его завет – все, что повелел Моисей, слуга Господа. Они и не слушали, и не исполняли.

Синаххериб угрожает Иерусалиму

(2 Пар. 32:1-19; Ис. 36:1-22)

13На четырнадцатом году правления царя Езекии18:13 В 701 г. до н. э. Синаххериб18:13 Синаххериб был сыном и преемником Саргона II. Он правил с 705 по 681 гг. до н. э., царь Ассирии, напал на все укрепленные города Иудеи и захватил их. 14Езекия, царь Иудеи, послал в город Лахиш сказать царю Ассирии:

– Я виновен. Оставь меня, и я заплачу тебе все, что ты от меня потребуешь.

Царь Ассирии взыскал с Езекии, царя Иудеи, триста талантов18:14 Около 10 т. серебра и тридцать талантов18:14 Около 1 т. золота. 15Езекия отдал ему все серебро, какое нашлось в доме Господа и в сокровищницах царского дворца. 16Тогда же Езекия, царь Иудеи, ободрал все золото, которым покрыл двери и дверные косяки храма Господа, и отдал его царю Ассирии.

17Но, тем не менее, царь Ассирии послал из Лахиша к царю Езекии в Иерусалим верховного военачальника, начальника придворных и главного виночерпия18:17 Главный виночерпий был одним из самых важных лиц при дворе, которому царь доверял свою жизнь. с большим войском. Они подошли к Иерусалиму и остановились у водопровода Верхнего пруда, на дороге к Сукновальному полю. 18Они позвали царя, и к ним вышли распорядитель дворца, Элиаким, сын Хелкии, писарь Шевна и летописец Иоах, сын Асафа.

19Главный виночерпий сказал им:

– Скажите Езекии: «Так говорит великий царь, царь Ассирии: „Откуда у тебя эта уверенность? 20Ты думаешь, что пустые слова – то же самое, что военное искусство и сила? На кого же ты надеешься, что восстал против меня? 21Вот, ты надеешься на Египет, эту надломленную трость, которая пронзит ладонь всякому, кто на нее обопрется! Фараон, царь Египта, таков со всеми, кто на него надеется. 22А если вы скажете мне: «Мы надеемся на Господа, нашего Бога», то не Его ли святилища на возвышенностях и жертвенники убрал Езекия, сказав Иудее и Иерусалиму: «Поклоняйтесь только перед этим жертвенником, что в Иерусалиме»?“

23Итак, заключи сделку с господином моим, царем Ассирии: я дам тебе две тысячи коней, только найдешь ли ты для них всадников? 24Как ты сможешь отразить хотя бы наименьшего начальника из слуг господина моего, даже надеясь на египетские колесницы и всадников?18:24 Или: «колесничих». 25Да и разве не по воле Господа я двинулся на это место, чтобы уничтожить его? Господь Сам сказал мне пойти на эту страну и уничтожить ее».

26Тогда Элиаким, сын Хелкии, Шевна и Иоах сказали главному виночерпию:

– Пожалуйста, говори с твоими слугами по-арамейски, ведь мы понимаем этот язык. Не говори с нами по-еврейски при народе, что на стене.

27Но главный виночерпий ответил:

– Разве мой господин послал меня сказать это только вашему господину и вам, а не людям, находящимся на стене, которые, как и вы сами, будут есть свой кал и пить свою мочу?

28Главный виночерпий встал и громко закричал по-еврейски:

– Слушайте слово великого царя, царя Ассирии! 29Так говорит царь: «Не давайте Езекии обманывать вас. Он не может избавить вас от моей руки. 30Не давайте Езекии убедить вас положиться на Господа, когда он говорит: „Господь непременно спасет нас; этот город не будет отдан в руки царя Ассирии“. 31Не слушайте Езекию».

Так говорит царь Ассирии: «Заключите со мной мир и выходите ко мне. Тогда все вы будете есть со своей лозы и инжирных деревьев и пить воду из своего колодца, 32пока я не приду и не возьму вас в страну, такую же, как ваша, в страну зерна и вина, страну хлеба и виноградников, страну оливковых деревьев и меда. Выберите жизнь, а не смерть! Не слушайте Езекию, потому что он сбивает вас с толку, говоря: „Господь спасет нас“. 33Разве какой-либо бог другого народа избавил свою страну от руки царя Ассирии? 34Где боги Хамата и Арпада? Где боги Сепарваима, Ены и Иввы? Разве кто-нибудь избавил от моей руки Самарию? 35Кто из богов всех этих стран смог избавить от меня свою страну? Как же Господь сможет избавить от моей руки Иерусалим?»

36Но народ молчал и не говорил в ответ ничего, потому что царь приказал: «Не отвечайте ему».

37И распорядитель дворца Элиаким, сын Хелкии, писарь Шевна и летописец Иоах, сын Асафа, пришли к Езекии в разорванных одеждах и передали ему то, что сказал главный виночерпий.