2 Mafumu 18 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 18:1-37

Hezekiya Mfumu ya Yuda

1Mʼchaka chachitatu cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Hezekiya mwana wa Ahazi mfumu ya Yuda analowa ufumu. 2Anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Abi, mwana wa Zekariya. 3Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake. 4Anachotsa malo opembedzerako mafano, anaphwanya miyala yachipembedzo ndiponso anadula mafano a Asera. Iye anaphwanya njoka yamkuwa imene Mose anapanga, pakuti mpaka kufikira nthawi imeneyi Aisraeli amafukiza lubani kwa njoka imeneyi. (Imatchedwa Nehusitani).

5Hezekiya anadalira Yehova Mulungu wa Israeli. Kotero panalibe wina wofanana naye pakati pa mafumu onse a Yuda, asanakhale mfumu kapena atakhala kale mfumu. 6Iye anakangamira Yehova ndipo sanamusiye koma anasunga malamulo amene Yehova anapatsa Mose. 7Ndipo Yehova anali naye ndipo kulikonse kumene anapita zinthu zinkamuyendera bwino. Iye anagalukira mfumu ya ku Asiriya ndipo sanayitumikirenso. 8Iye anakantha Afilisti kuyambira ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa. Anakafika mpaka ku Gaza ndi ku malire ake.

9Mʼchaka chachinayi cha Mfumu Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chiwiri cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Salimenezeri, mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Samariya ndi kuwuzinga 10Asiriya analanda mzindawu patatha zaka zitatu. Choncho mzinda wa Samariya unalandidwa chaka chachisanu ndi chimodzi cha Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya mfumu ya Israeli. 11Mfumu ya ku Asiriya inatenga Aisraeli kupita nawo ku ukapolo ku Asiriya ndipo anakawakhazika ku Hala, ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi. 12Izi zinachitika chifukwa sanamvere zonena za Yehova Mulungu wawo, koma anaphwanya pangano lake ndi zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anawalamula. Iwo sanamvere malamulowo kapena kuwagwiritsa ntchito.

13Mʼchaka chakhumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, nayilanda. 14Choncho Hezekiya mfumu ya Yuda anatumiza uthenga kwa mfumu ya ku Asiriya ku Lakisi wonena kuti, “Ine ndalakwa. Chokani kuno ndipo ndidzakupatsani chilichonse chimene munene.” Mfumu ya ku Asiriya inalamula mfumu Hezekiya, mfumu ya Yuda, kuti azipereka makilogalamu a siliva okwana 3,000 ndi makilogalamu a golide 1,000. 15Mfumu Hezekiya inapereka siliva yense amene anapezeka mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba zosungiramo chuma cha mfumu.

16Nthawi imeneyi Hezekiya mfumu ya Yuda anakanganula golide amene anakuta zitseko ndi mphuthu za chipata cha Nyumba ya Yehova namupereka kwa mfumu ya ku Asiriya.

Senakeribu Aopseza Yerusalemu

17Mfumu ya ku Asiriya inatuma Taritani, Rabusarisi ndi Rabusake pamodzi ndi gulu lalikulu la ankhondo, kwa Mfumu Hezekiya ku Yerusalemu kuchokera ku Lakisi. Iwo anafika ku Yerusalemu nakayima pafupi ndi ngalande ya madzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu waukulu wopita ku malo a Munda wa Mmisiri Wochapa. 18Iwo anayitana mfumu, ndipo Eliyakimu mwana wa Hilikiya woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa anthuwo.

19Ndipo Rabusake anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti,

“ ‘Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, ‘Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?’ 20Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine? 21Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.’ ” 22Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, “Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu.” Kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, “Muzipembedza pa guwa lansembe ili mu Yerusalemu?”

23“ ‘Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo! 24Ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo? 25Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga malo ano popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.’ ”

26Pamenepo Eliyakimu mwana wa Hilikiya, Sebina ndi Yowa anawuza Rabusakeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”

27Koma Rabusake anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”

28Tsono Rabusake anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya! 29Zimene mfumu ikunena ndi izi: ‘Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni mʼdzanja langa. 30Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’

31“ ‘Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake, 32mpaka nditabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanuli, dziko la tirigu ndi vinyo watsopano, dziko la chakudya ndi minda ya mipesa, dziko la mitengo ya olivi ndi uchi. Sankhani moyo osati imfa!

“Musamvere zonena Hezekiya, pakuti iye akukusocheretsani ponena kuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ 33Kodi mulungu wa anthu a mtundu wina uliwonse wapulumutsapo dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya? 34Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu, Hena ndi Ivani? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa? 35Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja langa? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”

36Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”

37Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu, mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza Hezekiya zonse zimene anayankhula Rabusake uja.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

列王紀下 18:1-37

希西迦做猶大王

1以拉的兒子以色列何細亞執政第三年,猶大亞哈斯的兒子希西迦登基。 2他二十五歲登基,在耶路撒冷執政二十九年。他母親叫亞比雅18·2 「亞比雅」此處的希伯來文為亞比,是亞比雅的變體。,是撒迦利雅的女兒。 3希西迦效法他祖先大衛,做耶和華視為正的事。 4他拆除邱壇,砸碎神柱,砍倒亞舍拉神像,打碎摩西造的銅蛇,因為當時以色列人仍向銅蛇燒香,稱之為尼忽士旦18·4 「尼忽士旦」可能是「蛇」和「銅」的組合詞。5希西迦信靠以色列的上帝耶和華,在他前後的猶大諸王沒有一個可與他相比。 6他對耶和華忠心不渝,遵守耶和華頒給摩西的誡命。 7耶和華與他同在,他凡事順利。他反抗亞述王的統治,不再臣服於他。 8他擊敗非利士人,從他們的瞭望塔和堅城,一直打到迦薩及其四境。

9希西迦執政第四年,即以拉的兒子以色列何細亞執政第七年,亞述撒縵以色起兵攻打撒瑪利亞城,將城包圍。 10三年之後,就是希西迦執政第六年,以色列何細亞執政第九年,撒瑪利亞失陷。 11亞述王把以色列人擄到亞述,將他們安置在哈臘歌散哈博河一帶以及瑪代人的城邑裡。 12這都是因為以色列人沒有聽從他們的上帝耶和華,違背了祂的約,不遵行祂僕人摩西所吩咐的一切。

亞述人攻打耶路撒冷

13希西迦王執政第十四年,亞述西拿基立起兵攻取了猶大所有的堅城。 14希西迦王差遣使者去拉吉亞述王說:「我知罪了,求你退兵!我願意滿足你的任何要求。」亞述王向希西迦索要十噸銀子和一噸金子。 15希西迦將耶和華殿裡和王宮庫房裡的所有銀子都給了他, 16又刮下他包在耶和華殿門和門柱上的金子,一併送去。 17亞述王派他的元帥、都統和將軍從拉吉率領大軍到耶路撒冷希西迦。到了耶路撒冷後,他們駐紮在上池的水溝旁、通往漂布場的路上。 18他們要求見王。希勒迦的兒子宮廷總管以利亞敬、書記舍伯那亞薩的兒子史官約亞出來見他們。 19亞述的將軍說:「你們去告訴希西迦,偉大的亞述王說,『你憑什麼這樣自信呢? 20你所謂的戰略和軍力不過是空話。你究竟倚靠誰,竟敢背叛我? 21看啊,你所倚靠的埃及只不過是一根破裂的蘆葦,誰倚靠它,誰的手就會被刺傷。倚靠埃及王法老的下場都是這樣。』 22也許你會說,『我們倚靠我們的上帝耶和華。』希西迦不是拆除了祂的廟宇和祭壇,又吩咐猶大耶路撒冷的人要在耶路撒冷的祭壇前敬拜祂嗎? 23來,跟我主人亞述王打個賭,你若能找到兩千騎士,我就給你兩千匹馬! 24你們即使依靠埃及的戰車和騎兵,又怎能打敗我主人的一個最小的將領呢? 25更何況我來攻打、毀滅這地方不正是耶和華的意思嗎?耶和華吩咐我攻打、毀滅這地方。」

26以利亞敬舍伯那約亞亞述的將軍說:「求你用亞蘭語跟僕人們說話,我們都聽得懂。求你不要用希伯來語跟我們說話,免得城牆上的人聽見。」 27亞述的將軍卻說:「難道我主人派我來只對你們和你們的王說這些話嗎?不也是對城牆上的人說嗎?他們和你們一樣都要吃自己的糞,喝自己的尿。」 28於是,他站著用希伯來語大喊:「你們要聽偉大的亞述王的話。 29王說,『你們不要被希西迦欺騙,他不能從我手中救你們。 30不要聽希西迦的話去倚靠耶和華,說什麼耶和華必拯救你們,這城必不會落在亞述王手中。』 31不要聽希西迦的話。亞述王說,『你們要跟我講和,出來歸順我,你們就可以吃自己葡萄樹和無花果樹的果子,喝自己井裡的水。 32以後我會來領你們到一個地方,那裡和這裡一樣有五穀和新酒、餅和葡萄園。你們就可以存活,不至於死。希西迦說耶和華會拯救你們,不要聽信他的話。 33有哪個國家的神明曾經從亞述王手中救他的國家嗎? 34哈馬亞珥拔的神明在哪裡呢?西法瓦音希拿以瓦的神明又在哪裡呢?他們從我手中救出撒瑪利亞了嗎? 35這些國家的神明哪個從我手中救了自己的國家呢?難道耶和華能從我手中救耶路撒冷嗎?』」 36民眾默不作聲,因為希西迦曾吩咐他們不要答話。 37總管以利亞敬、書記舍伯那和史官約亞都撕裂衣服,去向希西迦稟告亞述的將軍說的話。