2 Mafumu 12 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 12:1-21

Yowasi Akonzanso Nyumba ya Yehova

1Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba. 2Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza. 3Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.

4Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova. 5Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”

6Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo. 7Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.” 8Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.

9Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova. 10Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba. 11Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba, 12amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.

13Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova. 14Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo. 15Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri. 16Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.

17Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. 18Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.

19Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? 20Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo. 21Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

列王紀下 12:1-21

約阿施做猶大王

1以色列耶戶執政第七年,約阿施登基,在耶路撒冷執政四十年。他母親叫西比亞,是別示巴人。 2耶何耶大祭司的教導下,約阿施一生做耶和華視為正的事。 3但他沒有拆毀邱壇,人們仍在那裡獻祭燒香。

4約阿施對祭司們說:「你們要收集那些奉獻到耶和華殿的聖銀,即人口普查時收取的銀子、個人還願的銀子和自願奉獻的銀子。 5每位祭司要從奉獻的人手中收取銀子,用來修殿。」 6可是,直到約阿施執政第二十三年,祭司仍未動工。 7約阿施召來耶何耶大祭司及其他祭司,對他們說:「你們為什麼還不修殿呢?不要再向奉獻的人收銀子了,要把所收的銀子交出來修殿。」 8祭司們答應不再向民眾收錢,但也不動工修殿。

9耶何耶大祭司在耶和華殿的入口右邊的祭壇旁放了一個箱子,箱蓋上開了個洞。守門的祭司將奉獻到耶和華殿的所有銀子放進箱子裡。 10箱子裡的銀子多了,王的書記和大祭司就把銀子點好,裝在袋子裡。 11他們將秤好的銀子交給修耶和華殿的督工。督工把報酬轉交給在殿裡工作的木匠、建築工人、 12泥水匠和石匠,購買修耶和華殿用的木料和鑿好的石頭,並支付其他的修殿費用。 13獻到耶和華殿裡的銀子沒有用於製造殿裡的銀碗、蠟剪、盆、號及其他金銀器皿, 14只用於修殿。 15督工們辦事忠誠可靠,不需要跟他們清算賬目。 16贖過祭和贖罪祭的銀子沒有帶到耶和華的殿裡,而是歸給祭司。

17那時,亞蘭哈薛攻陷了迦特,準備進攻耶路撒冷18猶大約阿施把先王約沙法約蘭亞哈謝和他自己奉獻的聖物以及耶和華殿裡和王宮庫房裡的所有金子都送給了亞蘭哈薛哈薛便從耶路撒冷退兵。

19約阿施其他的事及其一切作為都記在猶大的列王史上。 20約阿施的臣僕謀反,在去悉拉途中的米羅宮殺了他。 21殺他的是示米押的兒子約撒甲朔默的兒子約薩拔約阿施葬在大衛城他的祖墳裡。他兒子亞瑪謝繼位。