2 Mafumu 12 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 12:1-21

Yowasi Akonzanso Nyumba ya Yehova

1Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba. 2Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza. 3Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.

4Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova. 5Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”

6Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo. 7Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.” 8Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.

9Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova. 10Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba. 11Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba, 12amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.

13Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova. 14Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo. 15Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri. 16Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.

17Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. 18Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.

19Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? 20Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo. 21Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

4 Царств 12:1-21

1На седьмом году правления Иеву Иоаш стал царём и правил в Иерусалиме сорок лет. Его мать звали Цивия, она была родом из Беэр-Шевы. 2Иоаш делал то, что было правильным в глазах Вечного, всё время, пока его наставлял священнослужитель Иодай. 3Лишь святилища на возвышенностях не были убраны, и народ продолжал приносить там жертвы и возжигать благовония.

Иоаш восстанавливает храм

(2 Лет. 24:4-14)

4Иоаш сказал священнослужителям:

– Соберите все деньги, что приносятся как священный дар в храм Вечного, – деньги, собранные по переписи, деньги, полученные по обетам, и деньги, которые были добровольно пожертвованы на храм. 5Пусть возьмут деньги у жертвующих и используют их на восстановление храма там, где найдётся повреждение.

6Но к двадцать шестому году правления царя Иоаша священнослужители всё ещё не восстановили храм.

7И вот царь Иоаш призвал священнослужителя Иодая и прочих священнослужителей и сказал им:

– Почему вы не восстанавливаете храм? Не берите больше денег у жертвующих, а передайте их на восстановление храма.

8Священнослужители согласились, что не будут больше ни принимать от народа денег, ни отвечать за восстановление храма.

9Священнослужитель Иодай взял ящик и проделал в его крышке дыру. Он поставил его у жертвенника, с правой стороны от входа в храм Вечного, и священнослужители, которые охраняли вход, клали в ящик все деньги, приносимые в храм Вечного. 10Всякий раз, когда они видели, что в ящике много денег, приходили царский писарь и главный священнослужитель, считали деньги, принесённые в храм Вечного, и клали их в мешки. 11Когда деньги были пересчитаны, они отдавали их тем, кто смотрел за работами в храме. А те платили работавшим в храме Вечного, – плотникам и строителям, 12тем, кто клал стены, и тем, кто тесал камни. Они также покупали дерево и тёсаные камни для восстановления храма Вечного и оплачивали все прочие расходы на восстановление храма.

13Но ни серебряных кубков, ни ножниц для фитилей, ни кропильных чаш, ни труб, ни иных вещей из золота или серебра для храма Вечного не изготовляли на деньги, приносимые в храм. 14Деньги платили рабочим, которые восстанавливали храм. 15От тех, кому отдавали деньги для выплаты рабочим, не требовали отчёта, потому что они действовали честно. 16Деньги от жертв повинности и жертв за грех не вносились в храм Вечного – они шли священнослужителям.

Иоаш спасает Иерусалим от Хазаила

(2 Лет. 24:23-24)

17В то время Хазаил, царь Сирии, напал на город Гат и захватил его. Затем он решил идти на Иерусалим. 18Но Иоаш, царь Иудеи, взял все священные вещи, посвящённые его предками – Иосафатом, Иорамом и Охозией, царями Иудеи, дары, которые посвятил он сам, и всё золото, которое нашлось в сокровищницах храма Вечного и царского дворца, и послал их Хазаилу, царю Сирии, который после этого отошёл от Иерусалима.

Смерть Иоаша

(2 Лет. 24:25-27)

19Прочие события царствования Иоаша и всё, что он сделал, записано в «Книге летописей царей Иудеи». 20Его приближённые составили против него заговор и убили его в Бет-Милло, что на дороге, которая спускается к Силле. 21Иозавад, сын Шимеаты, и Иехозавад, сын Шомеры, – вот те приближённые, которые убили его. Он был похоронен со своими предками в Городе Давуда. И царём вместо него стал его сын Амасия.