2 Atesalonika 3 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Atesalonika 3:1-18

Tipempherereni

1Potsiriza, abale, mutipempherere kuti uthenga wa Ambuye ufalikire msanga ndi kulemekezedwa monga momwe munachitira inu. 2Ndipo pempherani kuti tilanditsidwe mʼmanja mwa anthu ovuta ndi oyipa, pakuti si onse amene ali nacho chikhulupiriro. 3Koma Ambuye ndi wokhulupirika, ndipo adzakulimbikitsani ndi kukutetezani kwa woyipayo. 4Tili ndi chikhulupiriro mwa Ambuye kuti mukuchita zonse ndipo mudzapitirira kuchita zimene tinakulamulirani. 5Ambuye atsogolere mitima yanu kuti mudziwe chikondi cha Mulungu ndiponso kupirira kumene Khristu amapereka.

Awachenjeza za Kusagwira Ntchito

6Abale, tikukulamulani mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, kuti mupewe mʼbale aliyense amene ndi waulesi ndi wachisokonezo, wosafuna kutsata zimene tinakuphunzitsani. 7Pakuti inu mukudziwa zimene muyenera kuchita pofuna kutitsatira. Ife sitinali alesi pamene tinali nanu 8ndipo sitinadye chakudya cha aliyense osalipira. Komatu tinkagwira ntchito mwamphamvu usiku ndi usana kuti tisakhale cholemetsa kwa aliyense. 9Sitinachite zimenezi chifukwa choti tinalibe mphamvu zolamula kuti mutithandize koma kuti tikhale chitsanzo choti mutsatire. 10Pakuti ngakhale pamene tinali nanu, tinakupatsani lamulo lakuti, “Munthu wosafuna kugwira ntchito, asadye.”

11Ife tikumva kuti pakati panu pali ena amene ndi alesi. Iwo safuna kugwira ntchito, koma amangolowerera pa za eni. 12Mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, tikuwalamula ndi kuwakakamiza kuti azigwira ntchito mwabata ndi kumadya chakudya chodzigwirira ntchito okha. 13Koma inu abale, musatope nʼkuchita zabwino.

14Ngati wina aliyense akana kumvera malangizo athu a mʼkalatayi, mumuonetsetse ameneyo ndipo musayanjane naye kuti achite manyazi. 15Komatu musamutenge kukhala mdani, koma muchenjezeni ngati mʼbale.

Malonje Otsiriza

16Tsopano Ambuye mwini mtendere akupatseni mtendere nthawi zonse mwa njira iliyonse. Ambuye akhale ndi inu nonse.

17Ine Paulo, ndikulemba malonje awa ndi dzanja langa, chimene ndi chizindikiro chodziwika mʼmakalata anga onse. Umo ndi mmene ndimalembera.

18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse.

Slovo na cestu

2. Tesalonickým 3:1-18

Věřící mají pevně stát

1Závěrem, bratři, prosíme o vaše přímluvné modlitby, aby se Boží poselství rychle šířilo a všude vítězilo jako u vás 2a abychom byli ušetřeni úkladů zvrácených a zlých lidí. Vždyť ne všichni stojí věrně na Boží straně, 3ale Pán je věrný. On vás posilní a ochrání od zlého. 4My patříme Pánu stejně jako vy, a proto spoléháme, že se našimi slovy řídíte a budete řídit i dál. 5Přejeme si, aby vaše srdce bylo naplněno Boží láskou a Kristovou trpělivostí.

Pavlovo varování před leností

6Dále přikazujeme jménem Ježíše Krista, abyste se stranili všech, kteří si neberou k srdci naše naučení a ubíjejí čas zahálkou. 7Dali jsme vám přece sami příklad, jak máte žít; nikdy jste nás neviděli zahálet 8a přiživovat se u jiných. – Ve dne v noci jsme si tvrdou prací vydělávali na chléb, abychom nikoho nevyjídali. 9Ne, že bychom neměli právo žádat od vás zaopatření, ale chtěli jsme vám dát příklad k napodobování. 10Taky jsme vám vždycky zdůrazňovali: Kdo nechce pracovat, ať nejí! 11A přece teď slyšíme, že jsou mezi vámi darmojedi, kterým práce nevoní. 12Takové vyzýváme a Kristovým jménem jim nařizujeme, aby nezaháleli a na svůj chléb si řádně vydělávali. 13Vám, však bratři, připomínáme: v konání dobra nepolevujte.

Lenochům vyjádřete nesouhlas, ale nadále je milujte

14Kdyby se někdo zdráhal podřídit tomu, co píšeme, dejte mu pocítit, že mezi vás nepatří; snad se pak zastydí. 15Ale nejednejte s ním jako s nepřítelem; spíš ho varujte jako bratra, na němž vám záleží.

16Ať vám Pán pokoje dá svůj pokoj vždycky a všude a zůstává s vámi. 17Tento pozdrav připisuji ve všech dopisech vlastní rukou na důkaz, že jsou skutečně ode mne. 18Milost našeho Pána, Ježíše Krista, ať vás provází.

Váš Pavel