2 Atesalonika 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Atesalonika 3:1-18

Tipempherereni

1Potsiriza, abale, mutipempherere kuti uthenga wa Ambuye ufalikire msanga ndi kulemekezedwa monga momwe munachitira inu. 2Ndipo pempherani kuti tilanditsidwe mʼmanja mwa anthu ovuta ndi oyipa, pakuti si onse amene ali nacho chikhulupiriro. 3Koma Ambuye ndi wokhulupirika, ndipo adzakulimbikitsani ndi kukutetezani kwa woyipayo. 4Tili ndi chikhulupiriro mwa Ambuye kuti mukuchita zonse ndipo mudzapitirira kuchita zimene tinakulamulirani. 5Ambuye atsogolere mitima yanu kuti mudziwe chikondi cha Mulungu ndiponso kupirira kumene Khristu amapereka.

Awachenjeza za Kusagwira Ntchito

6Abale, tikukulamulani mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, kuti mupewe mʼbale aliyense amene ndi waulesi ndi wachisokonezo, wosafuna kutsata zimene tinakuphunzitsani. 7Pakuti inu mukudziwa zimene muyenera kuchita pofuna kutitsatira. Ife sitinali alesi pamene tinali nanu 8ndipo sitinadye chakudya cha aliyense osalipira. Komatu tinkagwira ntchito mwamphamvu usiku ndi usana kuti tisakhale cholemetsa kwa aliyense. 9Sitinachite zimenezi chifukwa choti tinalibe mphamvu zolamula kuti mutithandize koma kuti tikhale chitsanzo choti mutsatire. 10Pakuti ngakhale pamene tinali nanu, tinakupatsani lamulo lakuti, “Munthu wosafuna kugwira ntchito, asadye.”

11Ife tikumva kuti pakati panu pali ena amene ndi alesi. Iwo safuna kugwira ntchito, koma amangolowerera pa za eni. 12Mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, tikuwalamula ndi kuwakakamiza kuti azigwira ntchito mwabata ndi kumadya chakudya chodzigwirira ntchito okha. 13Koma inu abale, musatope nʼkuchita zabwino.

14Ngati wina aliyense akana kumvera malangizo athu a mʼkalatayi, mumuonetsetse ameneyo ndipo musayanjane naye kuti achite manyazi. 15Komatu musamutenge kukhala mdani, koma muchenjezeni ngati mʼbale.

Malonje Otsiriza

16Tsopano Ambuye mwini mtendere akupatseni mtendere nthawi zonse mwa njira iliyonse. Ambuye akhale ndi inu nonse.

17Ine Paulo, ndikulemba malonje awa ndi dzanja langa, chimene ndi chizindikiro chodziwika mʼmakalata anga onse. Umo ndi mmene ndimalembera.

18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

帖撒羅尼迦後書 3:1-18

請求代禱

1弟兄姊妹,最後我還要請你們為我們禱告,好使主的道像在你們那裡一樣迅速傳開,受到尊崇, 2並使我們能避開那些邪惡的人,因為不是人人都有信心。

3主是信實的,祂必使你們剛強,保護你們脫離那惡者。 4我們靠著主深信你們現在遵行了我們的吩咐,而且以後還會繼續遵行。

5願主引導你們的心領悟上帝的愛和基督的堅忍。

不可遊手好閒

6弟兄姊妹,現在我們奉主耶穌基督的名吩咐你們,要遠離那些遊手好閒、不遵守我們教導的信徒。 7你們自己知道應該怎樣效法我們,因為我們在你們那裡的時候,並沒有懶懶散散, 8也沒有白吃誰的飯,而是晝夜辛勤工作,免得成為你們任何人的負擔。 9我們並不是沒有權利接受供應,而是要給你們樹立學習的榜樣。 10我們在你們那裡的時候,曾吩咐過你們:不肯工作的人沒有資格吃飯。 11我們聽說在你們當中有些人遊手好閒,無所事事,卻專管閒事。 12我們奉主耶穌基督的名吩咐並勸誡這些人要安分守己,自食其力。

13弟兄姊妹,你們要堅持行善,不要灰心。 14如果有人不聽從這信上的教導,要注意提防他,不要和他來往,好使他羞愧。 15只是不可把他當作仇人,要像對待弟兄姊妹一樣勸誡他。

問候

16願平安之主隨時隨地親自賜你們平安!願主與你們同在! 17我保羅在這裡親筆問候你們,這是我的筆跡,我所有的信都以此為記號。

18願我們主耶穌基督的恩典與你們眾人同在!