2 Akorinto 6 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 6:1-18

1Pogwira naye ntchito pamodzi, tikukudandaulirani kuti musangolandira chisomo cha Mulungu pachabe. 2Pakuti akunena kuti,

“Pa nthawi yanga yabwino yokomera anthu mtima ndinakumvera,

ndipo pa nthawi yopulumutsa ndinakuthandiza.

Taonani, ndikukuwuzani kuti, ino ndiyo nthawi yabwino ya Ambuye, lero ndiye tsiku la chipulumutso.”

Masautso a Paulo

3Ife sitikuyika chokhumudwitsa pa njira ya wina aliyense, kuti utumiki wathu usanyozeke. 4Mʼmalo mwake, mwanjira iliyonse timasonyeza kuti ndife atumiki a Mulungu popirira kwambiri mʼmasautso, mʼzowawa ndi mʼzodetsa nkhawa. 5Pomenyedwa, kuponyedwa mʼndende ndi mʼzipolowe. Pogwira ntchito mwamphamvu, posagona usiku onse, posowa chakudya; 6pokhala moyo woyera mtima, pomvetsa zinthu, wokoma mtima ndi wachifundo mwa Mzimu Woyera ndi mwachikondi choonadi 7ndi poyankhula choonadi mwamphamvu ya Mulungu. Zida zimene zili mʼdzanja lamanja ndi lamanzere ndizo chilungamo. 8Timatumikira Mulungu ngakhale ena amatinyoza ndi ena amatilemekeza, ena amatinenera chipongwe, enanso amatiyamikira. Ena amatitenga kukhala ngati onena zoona, ndipo enanso amatitenga kukhala ngati onena zabodza. 9Amatiyesa osadziwika komatu ndife odziwika kwambiri. Amatiyesa wooneka ngati tikufa, koma tikupitirirabe ndi moyo, okanthidwa, koma osaphedwa. 10Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.

11Tayankhula momasuka kwa inu, Akorinto, ndipo tanena zonse za kumtima kwathu. 12Ife sitikukubisirani chikondi chathu pa inu, koma inu mukubisa chikondi chanu pa ife. 13Pofuna kufanana zochita ndi kuyankhula monga kwa ana anga, nanunso muzinena za kukhosi kwanu.

Kukhala Pamodzi ndi Osakhulupirira

14Musamasenze goli pamodzi ndi osakhulupirira. Kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kulungama ndi kusalungama? Kapena kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kuwala ndi mdima? 15Pali mgwirizano wanji pakati pa Khristu ndi Beliyali? Kapena munthu wokhulupirira angayanjane bwanji ndi munthu wosakhulupirira? 16Pali mgwirizano wanji pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ya mafano? Popezatu ndife Nyumba ya Mulungu wamoyo. Monga Mulungu wanena kuti,

“Ndidzakhala mwa iwo

ndipo ndidzayendayenda pakati pawo,

ndipo ndidzakhala Mulungu wawo,

ndipo adzakhala anthu anga.”

17Nʼchifukwa chake

“Tulukani pakati pawo

ndi kudzipatula,

akutero Ambuye.

Musakhudze chodetsedwa chilichonse,

ndipo ndidzakulandirani.”

18Ndipo

“Ndidzakhala Atate anu,

ndipo inu mudzakhala ana anga aamuna ndi aakazi,

akutero Ambuye, Wamphamvuzonse.”

New International Reader’s Version

2 Corinthians 6:1-18

1We work together with God. So we are asking you not to receive God’s grace and then do nothing with it. 2He says,

“When I had mercy on you, I heard you.

On the day I saved you, I helped you.” (Isaiah 49:8)

I tell you, now is the time God has mercy. Now is the day he saves.

Paul’s Sufferings

3We don’t put anything in anyone’s way. So no one can find fault with our work for God. 4Instead, we make it clear that we serve God in every way. We serve him by standing firm in troubles, hard times and suffering. 5We don’t give up when we are beaten or put in prison. When people stir up trouble in the streets, we continue to serve God. We work hard for him. We go without sleep and food. 6We remain pure. We understand completely what it means to serve God. We are patient and kind. We serve him in the power of the Holy Spirit. We serve him with true love. 7We speak the truth. We serve in the power of God. We hold the weapons of godliness in the right hand and in the left. 8We serve God in times of glory and shame. We serve him whether the news about us is bad or good. We are true to our calling. But people treat us as if we were pretenders. 9We are known, but people treat us as if we were unknown. We are dying, but we continue to live. We are beaten, but we are not killed. 10We are sad, but we are always full of joy. We are poor, but we make many people rich. We have nothing, but we own everything.

11Believers at Corinth, we have spoken freely to you. We have opened our hearts wide to you. 12We are not holding back our love from you. But you are holding back your love from us. 13I speak to you as if you were my children. It is only fair that you open your hearts wide to us also.

Paul Warns Against Worshiping False Gods

14Do not be joined to unbelievers. What do right and wrong have in common? Can light and darkness be friends? 15How can Christ and Satan agree? Or what does a believer have in common with an unbeliever? 16How can the temple of the true God and the statues of other gods agree? We are the temple of the living God. God has said,

“I will live with them.

I will walk among them.

I will be their God.

And they will be my people.” (Leviticus 26:12; Jeremiah 32:38; Ezekiel 37:27)

17So,

“Come out from among them

and be separate,

says the Lord.

Do not touch anything that is not pure and ‘clean.’

Then I will receive you.” (Isaiah 52:11; Ezekiel 20:34,41)

18And,

“I will be your Father.

You will be my sons and daughters,

says the Lord who rules over all.” (2 Samuel 7:14; 7:8)