2 Akorinto 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 3:1-18

Akhristu ndi Kalata Yochokera kwa Khristu

1Kodi tayambanso kudzichitira umboni tokha? Kapena kodi ifenso tikufuna makalata otivomereza kwa inu, kapena ochokera kwa inu monga anthu ena? 2Inu ndinu kalata yathu, yolembedwa pa mitima yathu, yodziwika ndi yowerengedwa ndi aliyense. 3Inu mukuonetsa kuti ndinu kalata yochokera kwa Khristu, zotsatira za utumiki wathu, osati yolembedwa ndi inki koma ndi Mzimu wa Mulungu wamoyo, osati pa miyala yosemedwa koma mʼmitima ya anthu.

4Kulimba mtima kumeneku tili nako pamaso pa Mulungu kudzera mwa Khristu. 5Sikuti mwa ife muli kanthu kotiganizitsa kuti tingathe kugwira ntchitoyi patokha, koma kulimba mtima kwathu kumachokera kwa Mulungu. 6Iye watipatsa kulimba mtima kuti tikhale atumiki a pangano latsopano, osati malamulo olembedwa koma a Mzimu; pakuti malamulo olembedwa amapha koma Mzimu amapereka moyo.

Ulemerero wa Pangano Latsopano

7Koma ngati utumiki umene unabweretsa imfa uja, wolembedwa ndi malemba pa mwalawu, unabwera ndi ulemerero mwakuti Aisraeli sanathe kuyangʼanitsitsa nkhope ya Mose chifukwa cha ulemerero wa pa nkhopeyo, ngakhale kuti unali kunka nuzilala, 8kodi nanga utumiki wa Mzimu sudzaposa apa? 9Ngati utumiki umene umatsutsa anthu unali ndi ulemerero, nanga koposa kotani ulemerero wa utumiki wobweretsa chilungamo! 10Pakuti zimene zinali ndi ulemerero, tsopano zilibenso ulemerero pofananitsa ndi ulemerero wopambanawo. 11Ndipo ngati zosakhalitsa zinabwera ndi ulemerero, koposa kotani ulemerero wamuyayawo!

12Choncho, popeza tili ndi chiyembekezo chotere, ndife olimba mtima kwambiri. 13Ife sitili ngati Mose amene amaphimba nkhope yake kuopa kuti Aisraeli angaone kuti kunyezimira kwa nkhope yake kumazilala. 14Koma nzeru zawo zinawumitsidwa, pakuti mpaka lero chophimbira chomwecho chikanalipo pamene akuwerenga Chipangano Chakale. Sichinachotsedwebe, chifukwa chimachotsedwa ngati munthuyo ali mwa Khristu yekha. 15Ngakhale lero lomwe lino akuwerenga mabuku a Mose pali chophimbabe mitima yawo. 16Koma pamene aliyense atembenukira kwa Ambuye, “chophimbacho chimachotsedwa.” 17Tsono Ambuye ndi Mzimu, ndipo pamene pali Mzimu wa Ambuye, pali ufulu. 18Ife tonse, amene ndi nkhope zosaphimba timaonetsera ulemerero wa Ambuye, tikusinthika kufanana ndi ulemerero wake, umene ukunka nuchulukirachulukira, wochokera kwa Ambuye, amene ndi Mzimu.

New Russian Translation

2 Коринфянам 3:1-18

Служители нового завета

1Может показаться, что мы начинаем хвалить самих себя. Но разве нуждаемся мы в рекомендательных письмах для вас или же от вас, как в этом нуждаются другие?3:1 По всей вероятности лжеучители, оппоненты Павла, имели с собой какие-то рекомендательные письма. 2Вы сами – наше письмо: письмо, записанное в наших сердцах, известное и читаемое всеми людьми. 3Все видят, что вы письмо Христа, написанное в результате нашего служения не чернилами, а Духом живого Бога, и не на каменных плитках, а в человеческих сердцах.

4Такую уверенность мы имеем через Христа перед Богом. 5И не потому, что у нас самих есть нечто особенное, некая заслуга; наши способности исключительно от Бога. 6Он наделил нас способностью быть служителями нового завета. Данный завет – это не писаный Закон, нет, но он от Духа. Ведь буква убивает, а Дух дает жизнь.

7Вспомните служение высеченному буквами на камнях Закону, которое принесло смерть. Оно было учреждено в такой славе, что израильтяне не могли смотреть на сияющее лицо Моисея, хотя это сияние постепенно затухало3:7 См. Исх. 34:27-35.. Если это служение пришло в такой славе, 8то разве не будет еще славнее служение Духа? 9Если служение, которое осуждает человека, было окружено такой славой, то насколько же большей славой наделено служение, несущее человеку оправдание! 10То, что было окружено славой тогда, кажется уже не таким славным по сравнению с гораздо большей славой. 11И если временное было окружено славой, то насколько же славнее будет вечное!

12Итак, мы имеем такую надежду, которая вселяет в нас смелость, 13и мы не закрываем свои лица, как это делал Моисей, чтобы израильтяне не смотрели на угасание той славы. 14Но их умы закрыты и до сих пор, ведь когда они читают Ветхий Завет, это покрывало остается неснятым, потому что оно может быть снято только Христом. 15По сегодняшний день, когда читаются книги Моисея, сердца их закрыты покрывалом. 16Но когда человек обращается к Господу, покрывало снимается3:16 См. Исх. 34:34.. 17Господь – это Дух3:17 Иисус, будучи здесь на земле, говорил Своим ученикам, что после Его вознесения Он будет обитать через Святого Духа в верующих в Него (см. Ин. 14:16-18, 23-26). И значит, присутствие Святого Духа равносильно присутствию Иисуса Христа., и всюду, где обитает Дух Господа, – там свобода!

18И мы все с открытыми лицами видим, как в зеркале3:18 Или «отражаем, как зеркало»., сияние славы Господа и изменяемся, становясь все больше похожими на Него. Его слава в нас все возрастает, ведь она исходит от Самого Господа, а Он есть Дух!