2 Akorinto 12 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 12:1-21

Masomphenya a Paulo ndi Minga ya Mʼthupi Mwake

1Ndiyenera kupitiriza kudzitamandira. Ngakhale palibe choti ndipindule, ndipitiriza kufotokoza za masomphenya ndi mavumbulutso ochokera kwa Ambuye. 2Ndikudziwa munthu mwa Khristu amene zaka khumi ndi zinayi zapitazo anatengedwa kupita kumwamba kwachitatu. Sindikudziwa ngati zinachitika ali mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu. 3Ndipo ndikumudziwa munthu ameneyu. Sindikudziwa ngati zinachitika mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu. 4Munthuyu anatengedwa kupita ku paradizo. Ndipo anamva zinthu zosatheka kuneneka, zinthu zimene munthu saloledwa kunena. 5Ndidzatamanda za munthu ngati ameneyu, koma sindidzadzitamandira ine mwini kupatula za kufowoka kwanga. 6Ngakhale nditafuna kudzitamandira, sindingakhale chitsiru, chifukwa ndikunena zoona. Koma ndimapewa kuti pasapezeke munthu wondiganizira moposera chimene ndili chifukwa cha zimene ndimachita kapena kuyankhula, 7kapena chifukwa cha mavumbulutso aakulu kuposa awa. Choncho, kuti ndisadzitukumule, ndinayikidwa minga mʼthupi langa, wamthenga wa Satana, kuti adzindizunza. 8Katatu konse ndinapempha Ambuye kuti andichotsere. 9Koma anandiwuza kuti, “Chisomo changa ndi chokukwanira, pakuti mphamvu zanga zimaoneka kwathunthu mwa munthu wofowoka.” Choncho ndidzadzitamandira mokondwera chifukwa cha zofowoka zanga, kuti mʼkutero mphamvu ya Khristu ikhale pa ine. 10Tsono, chifukwa cha Khristu, ndimakondwera pamene ndili wofowoka, pamene akundinyoza, pamene ndikumva zowawa, ndi pamene akundizunza ndi kundisautsa. Pakuti pamene ndili wofowoka ndiye kuti ndili wamphamvu.

Paulo Akhudzidwa ndi Akorinto

11Ndadzisandutsa wopusa, koma inu mwandichititsa zimenezi. Ndinu amene munayenera kundichitira umboni. Ngakhale kuti sindine kanthu, koma sindine wochepetsetsa kwa “atumwi apamwamba” aja. 12Ndinapirira pokuonetserani zizindikiro za mtumwi weniweni, pochita pakati panu zizindikiro, zodabwitsa ndi ntchito zamphamvu. 13Kodi inu munaoneka ochepa motani ku mipingo ina, kupatula kuti sindinali cholemetsa kwa inu? Mundikhululukire cholakwa chimenechi!

14Ndakonzeka tsopano kudzakuyenderani kachitatu, ndipo sindidzakhala cholemetsa kwa inu chifukwa ndikungofuna inuyo osati zinthu zanu. Pakuti ana sasamalira makolo koma makolo ndiwo asamalira ana. 15Motero ndidzakondwera kukupatsani zanga zonse zimene ndili nazo ndi kudziperekanso ine mwini chifukwa cha inu. Kodi ine ndikamakukondani kwambiri chotere, inuyo mudzandikonda pangʼono? 16Ena mwa inu amavomereza kuti sindinali cholemetsa. Komabe ena amaganiza kuti ndine wochenjera, ndipo ndinakuchenjererani. 17Kodi ndinakudyerani masuku pamutu kudzera mwa wina aliyense amene ndinamutumiza kwa inu? 18Ndinamupempha Tito kuti abwere kwanuko ndipo ndinamutumiza pamodzi ndi mʼbale wathu. Kodi kapena Tito anakudyerani masuku pamutu? Kodi iye ndi ine sitinachite zinthu mofanana ndi Mzimu mmodzi yemweyo?

19Kodi mukuyesa kuti nthawi yonseyi takhala tikudzitchinjiriza tokha? Takhala tikuyankhula pamaso pa Mulungu monga anthu amene ali mwa Khristu; ndipo abwenzi okondedwa, chilichonse chimene timachita ndi chofuna kukulimbikitsani. 20Pakuti ndikuona kuti pamene ndibwera sindidzakupezani monga mmene ndikufunira kuti muzikhalira, ndipo simungadzandione monga mmene mukufunira kundionera. Ndikuopa kuti pangadzakhale mkangano, nsanje, kupserana mitima, kugawikana, ugogodi, miseche, kudzitukumula ndi chisokonezo. 21Ndikuopa kuti pamene ndidzabwerenso, Mulungu adzandichepetsa pamaso panu, ndipo ndidzamva chisoni ndi ambiri amene anachimwa kale ndipo sanalape zonyansa, zachigololo ndi zilakolako zoyipa zimene anachita.

New Russian Translation

2 Коринфянам 12:1-21

О видениях Павла и жале в его теле

1Я вынужден продолжать хвалиться, хоть мне это ничего не дает. Перейду к видениям и откровениям от Господа. 2Я знаю человека12:2 Павел из скромности говорит здесь о себе в третьем лице (см. 12:7)., христианина, который четырнадцать лет тому назад был поднят на третье небо12:2 Третье небо – здесь говорится о высшей сфере, о небесах небес, т. е. о рае, месте, где пребывает Бог (ср. Пс. 67:34).; не знаю, был ли он в теле или же вне тела, это знает лишь Бог. 3Я знаю, что этот человек – опять же я не знаю, в теле или вне тела, это знает Бог – 4был взят в рай и слышал неизреченные слова, которые человеку нельзя пересказывать. 5Таким человеком я буду хвалиться, но собой хвалиться не буду, разве что своими слабостями. 6Даже если бы я и хотел хвалиться, это было бы разумно, потому что я бы говорил правду. Но я не буду этого делать, чтобы никто не подумал, что я хочу казаться значительнее, чем представляюсь людям, когда они меня видят или слышат.

7И чтобы я не зазнавался тем, что получил такие великие откровения, дано мне жало в тело12:7 Некоторые толкователи видят здесь указание на противодействие и гонения со стороны оппонентов Павла (ср. Чис. 33:55; Иез. 28:24)., ангел сатаны, чтобы мучить меня. 8Я три раза умолял Господа избавить меня от этого, 9но Он отвечал мне: «Достаточно для тебя Моей благодати, ведь сила Моя лучше всего проявляется в слабости». Поэтому я и хвалюсь с такой радостью своей слабостью, чтобы во мне была сила Христа. 10Поэтому я доволен и слабостями, и оскорблениями, и нуждами, и преследованиями, и трудностями, переносимыми мною ради Христа, потому что, когда я слаб, тогда я силен.

Переживание Павла о коринфской церкви

11Итак, я дошел до глупости, но вы сами меня к этому принудили. Вам следовало бы самим похвалить меня, ведь я ничем не хуже «сверхапостолов», хотя на самом-то деле я ничто. 12Вам были показаны отличительные признаки истинного апостола: предельное терпение, знамения, чудеса и силы. 13Так чего же вы были лишены в сравнении с другими церквами, не считая того, что я сам не был вам в тягость? Простите меня за эту обиду!

14Я собираюсь навестить вас в третий раз и надеюсь не быть вам в тягость. Я хочу не того, что у вас есть, а вас самих. Не дети должны копить деньги для своих родителей, а родители – для детей. 15Поэтому я готов охотно потратить на вас все и даже истощить самого себя ради вас. Неужели же вы любите меня меньше оттого, что я люблю вас больше? 16Как бы то ни было, я не был вам в тягость, но, может, вы скажете, что я своей хитростью все равно вас в чем-то обманул?

17Может, я выманивал у вас деньги через людей, которых я к вам посылал? 18Я посылал к вам Тита и с ним еще одного брата. Может, Тит воспользовался чем-то вашим? Разве не совершали мы с ним наше служение в одном и том же духе и не ходили одним путем?

19Сейчас вы, наверное, думаете о том, что мы защищаем себя перед вами. Мы – христиане и говорим вам перед Богом: возлюбленные, все, что мы делаем, мы делаем для вашего укрепления. 20Я боюсь, что, когда буду у вас, вы окажетесь не такими, как я бы хотел, и мне придется поступать с вами не так, как хотелось бы вам. Боюсь, что в вашей среде я застану споры, зависть, гнев, раздоры, клевету, сплетни, надменность и беспорядок. 21Боюсь, что когда я снова буду у вас, Бог унизит меня перед вами, и мне придется оплакивать многих, кто согрешил прежде, но так и не раскаялся в своей нечистоте, разврате и распутстве, в которых были повинны.