2 Akorinto 10 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 10:1-18

Paulo Ateteza Utumiki Wake

1Mwa kufatsa ndi kuleza mtima kwa Khristu, ndikukupemphani, ine Paulo amene anthu ena amati ndimachita manyazi tikaonana maso ndi maso ndi inu, koma wosaopa pamene ndili kutali nanu! 2Ndikukupemphani kuti ndikadzafika kumeneko ndisadzachite kuyankhula mwamphamvu monga mmene ndimayembekezera kudzachita kwa anthu ena amene amaganiza kuti machitidwe athu ndi ofanana ndi anthu a dziko lapansi. 3Ngakhale ife timakhala mʼdziko lapansi, sitimenya nkhondo monga mmene dziko lapansi limachitira. 4Pakuti zida zathu zankhondo si zida za dziko lapansi. Koma ndi mphamvu zochokera kwa Mulungu zotha kugwetsa malinga. 5Timagonjetsa maganizo onse onyenga ndiponso kudzikuza kulikonse kolimbana ndi anthu kuti asadziwe Mulungu. Ndipo timagonjetsa ganizo lililonse kuti limvere Khristu. 6Ndipo ife tidzakhala okonzeka kulanga aliyense wosamvera ngati inuyo mutakhala omvera kwenikweni.

7Inu mukuweruza potengera zimene maso anu akuona. Ngati wina akutsimikiza kuti ndi wake wa Khristu, iye aganizenso kuti ifenso ndife a Khristu monga iye. 8Tsono ngakhale nditadzitama momasuka za ulamuliro umene Ambuye anatipatsa woti tikukuzeni osati kukuwonongani, ndithu sindidzachita manyazi. 9Ine sindikufuna kuoneka ngati ndikukuopsezani ndi makalata anga. 10Pakuti ena amati, “Makalata ake ndi awukali ndi amphamvu koma maonekedwe a thupi lake ndi wosagwira mtima ndipo mayankhulidwe ake ndi achabechabe.” 11Anthu oterewa ayenera kuzindikira kuti zomwe timalemba mʼmakalata tili kutali ndi zomwe tidzakhale tili komweko.

12Sitikudziyika kapena kudzifananiza tokha ndi anthu ena amene amadziyenereza okha. Pamene akudzifanizira okha podziyerekeza ndi anzawo a mʼgulu lawo lomwe, ndi opanda nzeru. 13Komabe, ifeyo sitidzitama modutsa malire ake enieni, koma kudzitama kwathu kudzalekeza mʼmalire amene Mulungu anatiyikira, malire ake ndi mpaka kwa inu. 14Pakuti sitikudzitama modutsa malire ngati kuti sitinafike kwa inu, popeza tinali oyamba kufika kwa inu ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. 15Choncho sitinyadiranso ntchito imene ena anayigwira. Chiyembekezo chathu nʼchakuti, pamene chikhulupiriro chanu chikukulirakulira, dera lathu la ntchito pakati panu lidzakulanso kwambiri, 16kuti tikalalikire Uthenga Wabwino mu zigawo zina kupitirira kwanuko. Pakuti sitikufuna kudzitama pa ntchito yogwira ena kale mʼdera la munthu wina. 17Koma, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.” 18Pakuti munthu amene amavomerezedwa, si amene amadziyenereza yekha, koma munthu amene Ambuye amuyenereza.

Slovo na cestu

2. Korintským 10:1-18

Pavlova autorita je snižována

1Ještě jedné věci bych se chtěl dotknout – týká se to mé vlastní osoby a řeknu to beze vší hořkosti a nevraživosti, v duchu Kristovy lásky. Povídá se prý o mně, že v dopisech se stavím jako kdovíjaký silák, ale když dojde k osobnímu střetnutí, jsem prý maličký a ubohý.

2Prosím vás, nenuťte mě, abych vás přesvědčil, že mi nechybí odvaha k ráznějšímu postupu proti těm, kdo přičítají mému jednání pouze lidské pohnutky. 3Ano, jsme jen obyčejní lidé, ale své boje nevyhráváme pouze vlastní sílou. 4Máme účinné zbraně, schopné porazit každého odpůrce. 5Proti nim neobstojí žádná domýšlivost, ani nejchytřejší filozofie, popírající Boží pravdu. Každého myslícího člověka jednoznačně vedeme ke Kristu jako ke konečné odpovědi a svrchované pravdě. Rozhodnete-li se společně pro poslušnost, 6jsem připraven potrestat každého, kdo nebude poslušný.

7-8Nenechte se klamat vnějším zdáním. Jestliže si kdokoliv z vás může dělat nárok, že je Kristův, pak můj nárok není o nic menší – spíš naopak! Navíc bych se ještě mohl odvolávat na přímé Boží pověření. 9Nechci ovšem vzbudit dojem, jako bych vás chtěl svými listy zastrašovat.

10„Nevšímejte si jeho dopisů,“ říkají někteří, „je to jen plané vyhrožování. Až přijde, poznáte sami, že není proč se ho bát. Slabšího kazatele jste ještě neslyšeli.“ 11Ujišťuji vás, že tentokrát budu jednat stejně přísně, jako jsem doposud psal.

12V žádném případě se nechci měřit s těmi oslňujícími kazateli, kteří ve svých projevech vychvalují sami sebe. Těm se samozřejmě nemohu vyrovnat, protože oni jsou sami sobě jediným měřítkem a vzorem vší dokonalosti. Jaká pošetilost! 13-15Mým cílem je splnit se ctí úkoly, které mi vytyčil Bůh. K nim patří i má práce v Korintu. Odpovědnost za vás si neosobuji neprávem – vždyť jsem byl první, od koho jste vůbec slyšeli o Kristu! Kdybych svou autoritu odvozoval jen z toho, že pokračuji v díle, které začal někdo jiný, dalo by se o ní možná pochybovat. Ale jako váš duchovní otec bych spíš čekal, že s vaší vírou vzroste i úcta ke mně. 16-17Pak budu moci šířit Boží poselství dál i za vaše území, do krajů, kam dosud neproniklo. Písmo nás učí, že se nemáme honosit vlastními úspěchy, ale tím, co vykonal Bůh. Když někdo vykřikuje do světa, jaký je chlapík, to ještě nic neznamená. 18Důvěru si zaslouží ten a jenom ten, komu dává své vysvědčení Bůh.