2 Akorinto 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 1:1-24

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, pamodzi ndi mʼbale wathu Timoteyo,

Kulembera mpingo wa Mulungu mu Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse mu Akaya monse.

2Mukhale ndi chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Mulungu Mwini Chitonthozo

3Alemekezeke Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, Atate achifundo chonse, Mulungu wachitonthozo chonse. 4Iye amatitonthoza ife mʼmavuto athu onse, kuti ifenso tithe kutonthoza amene ali pavuto lililonse ndi chitonthozo chimene ife tilandira kwa Mulungu. 5Pakuti monga momwe tili mʼmasautso pamodzi ndi Khristu, momwemonso Khristu amatitonthoza kwambiri. 6Ngati ife tikusautsidwa, nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe ndi kupulumutsidwa. Ngati ife tikutonthozedwa nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe, ndi chitonthozo chimene chimabweretsa mwa inu kupirira kosawiringula pa zosautsa zomwe timasauka nazo ife. 7Ndipo chiyembekezo chathu pa inu nʼcholimba chifukwa tikudziwa kuti monga momwe mumamva zowawa pamodzi nafe, momwemonso mumatonthozedwa nafe pamodzi.

8Abale, sitikufuna kuti mukhale osadziwa za masautso amene tinakumana nawo mʼchigawo cha Asiya. Tinapanikizidwa koopsa kuposa muyeso woti nʼkutha kupirira, mwakuti sitinkadziwa kuti nʼkukhalabe ndi moyo. 9Zoonadi, tinamva mʼmitima mwathu chilango cha imfa. Koma izi zimachitika kuti tisangodzidalira mwa ife tokha koma Mulungu yemwe amaukitsa akufa. 10Mulungu watilanditsa ku zoopsa zotere za imfa, ndipo adzatilanditsanso. Ife tayika chiyembekezo chathu pa Iyeyo kuti adzapitiriza kutilanditsabe. 11Mutithandize potipempherera. Pamenepo ambiri adzathokoza mʼmalo mwathu, chifukwa cha chisomo chake poyankha mapemphero a anthu ambiri.

Paulo Afotokoza za Kusintha kwa Ulendo Wake

12Tsono chonyadira chathu nʼchakuti, chikumbumtima chathu chimatitsimikizira kuti timakhala bwino mʼdziko lapansi, makamaka pa ubale wathu ndi inu. Takhala moona mtima ndi oyera mtima. Sitinachite chomwechi mwa nzeru ya dziko lapansi koma monga mwa chisomo cha Mulungu. 13Pakuti sitikukulemberani zoti simungawerenge kapena kumvetsetsa. 14Monga mwamva pangʼono chabe, ndikuyembekeza kuti mudzamvetsa kwenikweni, kuti mutha kutinyadira monga ife tidzakunyadirani, pa tsiku la Ambuye Yesu.

15Popeza ndinatsimikiza mtima za ichi, nʼchifukwa chake ndinafuna kuti poyamba, ndidzakuchezereni kuti mupindule pawiri. 16Ndinafuna kuti ndidzakuchezereni pa ulendo wanga wopita ku Makedoniya ndi kudzakuonaninso pochokera ku Makedoniyako kuti inu mudzandithandize pa ulendo wanga wopita ku Yudeya. 17Kodi pamene ndinkakonzekera zimenezi, mukuganiza kuti ndinkachita mwachibwana? Kapena kuti ndinkaganiza ngati mwa dziko lapansi; kuti ndikhoza kumanena kuti, “Inde, Inde,” nthawi yomweyo nʼkumatinso “Ayi, Ayi?”

18Koma zoona monga Mulungu ali wokhulupirika, uthenga wathu kwa inu siwakuti, “Inde” nʼkutinso “Ayi.” 19Pakuti Yesu Khristu mwana wa Mulungu amene ine, Silivano ndi Timoteyo tinamulalikira pakati panu sali “Inde” yemweyonso “Ayi.” Koma nthawi zonse mwa Iye muli “Inde.” 20Pakuti ngakhale malonjezo a Mulungu atachuluka chotani, onsewo ndi “Inde” mwa Khristu. Kotero kuti mwa Iye, ife timati “Ameni” kuchitira Mulungu ulemu. 21Tsono ndi Mulungu amene anachititsa kuti inu ndi ife tiyime molimba mwa Khristu. Anatidzoza ife, 22nayikanso Mzimu wake mʼmitima mwathu kutitsimikizira za mʼtsogolo.

23Mulungu ndi mboni yanga kuti sindinabwererenso ku Korinto kuno kuti ndisakumvetseni chisoni. 24Sikuti ife tikufuna kukhala olamulira chikhulupiriro chanu, koma timagwira nanu ntchito pamodzi kuti mukhale achimwemwe, chifukwa ndinu okhazikika kwambiri mʼchikhulupiriro.

New Russian Translation

2 Коринфянам 1:1-24

1От Павла, по воле Бога апостола Христа Иисуса, и от брата Тимофея.

Церкви Божьей в Коринфе и всем святым в Ахаии1:1 Ахаия – римская провинция, включавшая в себя большую часть той территории, на которой расположена современная Греция..

2Благодать и мир вам от Бога Отца и от Господа Иисуса Христа.

Хвала Богу, дающему утешение

3Благословен Бог и Отец Господа нашего Иисуса Христа, Отец милосердия и Бог всяческого утешения. 4Он утешает нас во всех наших тяготах, чтобы и мы, в свою очередь, могли утешить других в их горе тем утешением, которым Бог утешает нас. 5Ведь как умножаются наши страдания ради Христа, так умножается Христом и наше утешение. 6Жизненные трудности мы переносим ради вашего утешения и спасения. Утешение, которое мы получаем, тоже дается нам ради вашего утешения. Оно поможет и вам стойко перенести те же страдания, которые приходится переносить нам. 7Мы твердо надеемся на вас и знаем, что как вы разделяете с нами наши страдания, так разделяете и наше утешение.

8Братья, я хочу, чтобы вы знали о том, что мы пережили в провинции Азия1:8 Азия – здесь имеется в виду не материк, а римская провинция на западе Малой Азии (часть современной территории Турции).. Выпавшие там на нашу долю страдания настолько превосходили все наши силы, что мы потеряли надежду остаться в живых. 9Казалось, что мы уже получили смертный приговор, но так было для того, чтобы мы научились полагаться не на себя, а на Бога, Который воскрешает мертвых. 10Он избавил нас от смертельной опасности и впредь избавит. На Него мы надеемся, и Он спасет нас. 11Только вы помогайте нам своими молитвами, чтобы многие возблагодарили Бога за то, что Он был так милостив к нам по их молитвам.

Изменение в планах Павла

12Мы хвалимся тем – и наша совесть может быть этому порукой, – что мы и в этом мире, и в особенности в наших отношениях с вами, поступали честно1:12 Или: «свято». и искренне, и это нам было дано от Бога. Мы поступали не по «мудрости» этого мира, но по Божьей благодати. 13Во всем, что мы вам написали, нет ничего, что вы, прочитав, не смогли бы понять. Я надеюсь, что, поняв нас до конца, – 14а отчасти вы нас уже понимаете, – в День возвращения Господа Иисуса вы сможете хвалиться нами так же, как и мы вами.

15Я уверен в этом и поэтому хотел бы сначала прийти к вам, чтобы вы дважды получили благодать. 16Я собирался побывать у вас по пути в Македонию, а затем еще раз посетить вас на обратном пути, и тогда вы помогли бы мне отправиться в Иудею. 17Может, вам кажется, что это решение было необдуманным? Или, может, я, как это водится у людей, говорю в одно и то же время то «да», то «нет»? 18Заверяю вас перед Богом, Который верен: то, что говорю вам, я говорю без колебаний. 19В Сыне Божьем Иисусе Христе, Которого вам возвещали я, Силуан и Тимофей, нет никакой неопределенности, в Нем всегда лишь только «да». 20Все обещания Божьи подтвердились в Иисусе Христе! Поэтому и мы говорим через Него во славу Бога: «Аминь».

21Бог делает и нас, и вас непоколебимыми во Христе. Он совершил над нами помазание 22и запечатлел нас Своей печатью. Он вложил в наши сердца Своего Духа как залог того, что Он нам обещал.

23Бог свидетель того, что лишь жалея вас, я до сих пор не приходил с наказанием в Коринф. 24Мы не хотим повелевать вашей верой, нет, мы делаем все лишь для вашей радости, потому что вы твердо стоите в вере.