1 Yohane 5 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yohane 5:1-21

Chikhulupiriro mwa Mwana wa Mulungu

1Aliyense amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Khristu, iyeyo ndi mwana wa Mulungu, ndipo aliyense amene amakonda Atate amakondanso Mwana wake. 2Chodziwira kuti timakonda ana a Mulungu nʼchakuti timakonda Mulungu ndi kusunga malamulo ake. 3Pakuti kukonda Mulungu ndiye kusunga malamulo ake. Ndipo malamulo ake siwolemetsa, 4chifukwa aliyense amene ndi mwana wa Mulungu amagonjetsa dziko lapansi. Chikhulupiriro chathu ndicho timagonjetsera dziko lapansi. 5Ndani amagonjetsa dziko lapansi? Yekhayo amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu.

6Uyu ndiye anabwera mwa madzi ndi magazi, ndiye Yesu Khristu. Sanabwere mwa madzi okha, koma mwa madzi ndi magazi. Ndipo ndi Mzimu Woyera amene akuchitira umboni, chifukwa Mzimu Woyera ndi choonadi. 7Pakuti pali atatu amene amachitira umboni. 8Mzimu Woyera, madzi ndi magazi; ndipo atatu amavomerezana. 9Timalandira umboni wa anthu, koma umboni wa Mulungu ndi wopambana. Umboniwo ndi umene anachitira Mwana wake. 10Aliyense amene amakhulupirira Mwana wa Mulungu ali nawo umboniwu mu mtima mwake, koma aliyense amene sanakhulupirire Mulungu amayesa kuti Mulunguyo ndi wonama, chifukwa sanakhulupirire umboni umene Mulungu anachitira wa Mwana wake. 11Ndipo umboniwo ndi uwu: Mulungu anatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowu uli mwa Mwana wake. 12Iye amene ali ndi Mwana ali ndi moyo, amene alibe Mwana wa Mulungu alibe moyo.

Mawu Otsiriza

13Ine ndikulemba zimenezi kwa inu, amene mwakhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha. 14Ife timalimba mtima tikamafika pamaso pa Mulungu, popeza kuti ngati tipempha kanthu kalikonse monga mwa chifuniro chake, amatimvera. 15Ndipo ngati tikudziwa kuti amatimvera, chilichonse chimene timapempha, tikudziwanso kuti tili nacho chimene tamupempha Iye.

16Ngati wina aona mʼbale wake akuchita tchimo losadzetsa imfa, apemphere ndipo Mulungu adzamupatsa moyo mʼbale wakeyo. Ndikunena za ochita tchimo losadzetsa imfa. Pali tchimo lodzetsa imfa. Ine sindikunena kuti apemphere ayi. 17Chilichonse chosalungama ndi tchimo ndipo pali tchimo losadzetsa imfa.

18Tikudziwa kuti aliyense amene ndi mwana wa Mulungu sachimwirachimwirabe. Yesu, Mwana wa Mulungu, amamusunga ndipo woyipa uja sangamukhudze. 19Tikudziwa kuti ndife ana a Mulungu ndi kuti dziko lonse lapansi lili pansi pa ulamuliro wa woyipayo. 20Tikudziwa kuti Mwana wa Mulungu anafika ndipo anatipatsa nzeru, kuti timudziwe Iye amene ali woona. Ndipo ife tili mwa Iye amene ndi woona, Mwana wake, Yesu Khristu. Iye ndi Mulungu woona ndi moyo wosatha.

21Ana okondedwa, dzisungeni bwino, osapembedza mafano.

New Russian Translation

1 Иоанна 5:1-21

Победа верующих над миром

1Кто верит в то, что Иисус – Христос5:1 То есть обещанный Мессия., тот рожден от Бога, а кто любит Отца, тот любит и рожденных от Него. 2А то, что мы любим Божьих детей, узнаем из того, что любим Бога и исполняем Его повеления. 3Любовь к Богу проявляется в исполнении Его повелений. Повеления Его необременительны, 4потому что тот, кто рожден от Бога, побеждает мир, и эта победа одержана благодаря нашей с вами вере. 5Кто же побеждает мир, как не тот, кто верит, что Иисус – Сын Божий?

Свидетельство Бога о Своем Сыне

6Иисус Христос пришел через воду и кровь5:6 Вода и кровь – возможные варианты истолкования: вода и кровь указывают 1) на крещение и смерть Христа; 2) на смерть Христа (Ин. 19:34).. Он пришел не только через воду, но через воду и кровь. И свидетель этому – Дух, потому что Дух есть истина. 7Итак, есть три свидетеля: 8Дух, вода и кровь – и все они свидетельствуют об одном5:7-8 В нескольких поздних рукописях: «Есть три свидетеля на небе: Отец, Слово и Святой Дух. И эти трое – одно. И есть три свидеделя на земле: дух, вода и кровь, и эти свидетельствуют об одном».. 9Если мы верим свидетельству людей, то свидетельство Бога намного сильнее, потому что это свидетельство Бога: Он засвидетельствовал о Своем Сыне. 10Кто верит в Божьего Сына, у того это свидетельство в нем самом, а кто не верит Богу, тот представляет Бога лжецом, потому что он не верит тому, что Бог говорит о Своем Сыне. 11Вот это свидетельство: Бог дал нам вечную жизнь, и жизнь эта – в Его Сыне. 12У кого есть Сын, у того есть жизнь, а у кого нет Сына, у того нет и жизни.

Молитва за грешников

13Я написал это вам, верящим во имя Божьего Сына, чтобы вы знали, что у вас есть вечная жизнь. 14Мы приходим к Богу с полной уверенностью в том, что если просим Его о чем-либо в согласии с Его волей, то Он нас слышит. 15И если мы знаем, что Он слышит нас, о чем бы мы ни просили, то знаем, что имеем то, что просим у Него.

16Когда вы видите своего брата согрешающим, и если этот грех не ведет к смерти, то молитесь об этом брате, и Бог даст ему жизнь. Я говорю здесь о таких грехах, которые не ведут к смерти5:16 Грех к смерти – возможно, здесь говорится о физической смерти (Деян. 5:1-11; 1 Кор. 11:30) или о непростительном грехе, как в Мк. 3:28-30; Евр. 6:4-9; 10:26.. Есть грех, последствием которого может быть только смерть, и я не говорю вам молиться о грешнике, виновном в таком грехе. 17Всякий неправедный поступок – грех, но не все грехи влекут за собой смерть5:17 Букв.: «но есть грех, не влекущий к смерти»..

Заключение

18Мы знаем, что всякий рожденный от Бога не любит грешить. Рожденный от Бога хранит себя5:18 Или: «Рожденный от Бога оберегает его»., и лукавый5:18 То есть «дьявол». не прикасается к такому человеку. 19Мы знаем, что мы от Бога, а весь мир лежит во власти лукавого. 20Мы знаем и то, что Сын Божий пришел и открыл нам разум, чтобы мы познали Того, Кто истинен. И мы в Том, Кто истинен – в Его Сыне Иисусе Христе. Он – истинный Бог и вечная жизнь!

21Дети, берегите себя от идолов.