1 Yohane 5 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yohane 5:1-21

Chikhulupiriro mwa Mwana wa Mulungu

1Aliyense amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Khristu, iyeyo ndi mwana wa Mulungu, ndipo aliyense amene amakonda Atate amakondanso Mwana wake. 2Chodziwira kuti timakonda ana a Mulungu nʼchakuti timakonda Mulungu ndi kusunga malamulo ake. 3Pakuti kukonda Mulungu ndiye kusunga malamulo ake. Ndipo malamulo ake siwolemetsa, 4chifukwa aliyense amene ndi mwana wa Mulungu amagonjetsa dziko lapansi. Chikhulupiriro chathu ndicho timagonjetsera dziko lapansi. 5Ndani amagonjetsa dziko lapansi? Yekhayo amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu.

6Uyu ndiye anabwera mwa madzi ndi magazi, ndiye Yesu Khristu. Sanabwere mwa madzi okha, koma mwa madzi ndi magazi. Ndipo ndi Mzimu Woyera amene akuchitira umboni, chifukwa Mzimu Woyera ndi choonadi. 7Pakuti pali atatu amene amachitira umboni. 8Mzimu Woyera, madzi ndi magazi; ndipo atatu amavomerezana. 9Timalandira umboni wa anthu, koma umboni wa Mulungu ndi wopambana. Umboniwo ndi umene anachitira Mwana wake. 10Aliyense amene amakhulupirira Mwana wa Mulungu ali nawo umboniwu mu mtima mwake, koma aliyense amene sanakhulupirire Mulungu amayesa kuti Mulunguyo ndi wonama, chifukwa sanakhulupirire umboni umene Mulungu anachitira wa Mwana wake. 11Ndipo umboniwo ndi uwu: Mulungu anatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowu uli mwa Mwana wake. 12Iye amene ali ndi Mwana ali ndi moyo, amene alibe Mwana wa Mulungu alibe moyo.

Mawu Otsiriza

13Ine ndikulemba zimenezi kwa inu, amene mwakhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha. 14Ife timalimba mtima tikamafika pamaso pa Mulungu, popeza kuti ngati tipempha kanthu kalikonse monga mwa chifuniro chake, amatimvera. 15Ndipo ngati tikudziwa kuti amatimvera, chilichonse chimene timapempha, tikudziwanso kuti tili nacho chimene tamupempha Iye.

16Ngati wina aona mʼbale wake akuchita tchimo losadzetsa imfa, apemphere ndipo Mulungu adzamupatsa moyo mʼbale wakeyo. Ndikunena za ochita tchimo losadzetsa imfa. Pali tchimo lodzetsa imfa. Ine sindikunena kuti apemphere ayi. 17Chilichonse chosalungama ndi tchimo ndipo pali tchimo losadzetsa imfa.

18Tikudziwa kuti aliyense amene ndi mwana wa Mulungu sachimwirachimwirabe. Yesu, Mwana wa Mulungu, amamusunga ndipo woyipa uja sangamukhudze. 19Tikudziwa kuti ndife ana a Mulungu ndi kuti dziko lonse lapansi lili pansi pa ulamuliro wa woyipayo. 20Tikudziwa kuti Mwana wa Mulungu anafika ndipo anatipatsa nzeru, kuti timudziwe Iye amene ali woona. Ndipo ife tili mwa Iye amene ndi woona, Mwana wake, Yesu Khristu. Iye ndi Mulungu woona ndi moyo wosatha.

21Ana okondedwa, dzisungeni bwino, osapembedza mafano.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約翰一書 5:1-21

勝過世界的人

1每一個信耶穌是基督的人,都是從上帝生的。凡愛生他之上帝的,也愛上帝所生的。 2當我們愛上帝,遵行祂的命令時,便知道自己也愛祂的兒女。 3因為我們遵行上帝的命令就是愛上帝,祂的命令並不難遵守。 4因為凡是從上帝生的人都能勝過世界,使我們得勝的是我們的信心。 5誰能勝過世界呢?不就是那些信耶穌是上帝的兒子的人嗎?

上帝的見證

6耶穌基督是藉著水和血來的。祂不單是藉著水來的,也是藉著水和血來的,並且有聖靈為祂做見證,聖靈就是真理。 7這樣,做見證的共有三樣: 8聖靈、水和血。這三者是一致的。 9我們既然接受人的見證,就更該接受上帝的見證,因為上帝為祂的兒子作了見證。 10信上帝兒子的人心裡有這見證,不信上帝的人等於把上帝當作撒謊的,因為他不信上帝為祂兒子做的見證。 11這見證就是:上帝已經把永恆的生命賜給我們,這生命在祂兒子裡面。 12人有上帝的兒子,就有這生命;沒有上帝的兒子,就沒有這生命。

永恆的生命

13我把這些事寫給你們這些信上帝兒子之名的人,是要你們知道自己有永生。 14我們若按著上帝的旨意祈求,祂必垂聽,這是我們對上帝的信心。 15我們既然知道上帝垂聽我們一切的祈求,就知道我們能得到所求的。

16若有人看見信徒犯了不至於死的罪,就當為他禱告,上帝必將生命賜給他。有的罪會導致死亡,我並不是說你們要為這樣的罪禱告。 17一切不義的事都是罪,但有的罪不會導致死亡。

18我們知道從上帝生的不會繼續犯罪,因為上帝的兒子保護他,那惡者無法害他。 19我們知道自己屬於上帝,全世界都在那惡者手中。

20我們知道上帝的兒子已經來了,並且賜給了我們悟性,使我們能認識真神。我們在真神裡面,就是在祂兒子耶穌基督裡面。祂是真神,也是永生。

21孩子們啊,你們要遠離偶像!