1 Yohane 4 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yohane 4:1-21

Kuyesa Mizimu

1Anzanga okondedwa, musakhulupirire mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ikuchokera kwa Mulungu, chifukwa aneneri onama ambiri afalikira mʼdziko lapansi. 2Mungathe kuzindikira Mzimu wa Mulungu motere: Mzimu uliwonse umene umavomereza kuti Yesu Khristu anabwera mʼthupi, ndi wochokera kwa Mulungu, 3koma mzimu uliwonse umene suvomereza Yesu, siwochokera kwa Mulungu. Uwu ndi mzimu wa wokana Khristu umene munawumva kuti ukubwera ndipo ngakhale tsopano wabwera kale mʼdziko lapansi.

4Inu ana okondedwa, ndinu ochokera kwa Mulungu ndipo mwawagonjetsa aneneri onyengawa, chifukwa Iye amene ali mwa inu ndi wamkulu kuposa amene ali mʼdziko lapansi. 5Aneneri onyengawa ndi ochokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake amayankhula za dziko lapansi, ndipo dziko lapansi limawamvera. 6Ife ndi ochokera kwa Mulungu, ndipo aliyense amene amadziwa Mulungu amamvera zimene timayankhula. Koma aliyense amene sachokera kwa Mulungu samvera zimene timayankhula. Mmenemu ndiye mmene timasiyanitsira pakati pa mzimu wachoonadi ndi Mzimu wachinyengo.

Mulungu ndiye Chikondi

7Anzanga okondedwa, tiyeni tikondane wina ndi mnzake, pakuti chikondi chimachokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi ndi mwana wa Mulungu ndipo amadziwa Mulungu. 8Aliyense amene alibe chikondi sadziwa Mulungu, chifukwa Mulungu ndiye chikondi. 9Mmene Mulungu anaonetsera chikondi chake pakati pathu ndi umu: Iye anatumiza Mwana wake mmodzi yekha ku dziko lapansi kuti mwa Iyeyo tikhale ndi moyo. 10Chikondi ndi ichi: osati kuti ife ndife amene tinamukonda Mulungu, koma kuti Iyeyo ndiye amene anatikonda ndipo anatumiza Mwana wake kuti akhale nsembe yopepesera machimo athu. 11Anzanga okondedwa, popeza Mulungu anatikonda chotere, ifenso tiyenera kukondana wina ndi mnzake. 12Palibe amene anaonapo Mulungu, koma tikakondana wina ndi mnzake, ndiye kuti Mulungu amakhala mwa ife ndipo chikondi chake chafika pachimake penipeni mwa ife.

13Ife tikudziwa kuti timakhala mwa Iye ndipo Iyeyo amakhala mwa ife chifukwa anatipatsa Mzimu wake. 14Ndipo taona ndipo tikuchitira umboni, kuti Atate anatuma Mwana wake kuti akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi. 15Ngati aliyense avomereza kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu, Mulungu amakhala mwa iye ndipo iyeyo amakhala mwa Mulungu. 16Tikudziwa ndipo timadalira chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ife.

Mulungu ndiye chikondi. Aliyense amene amakhala moyo wachikondi, ali mwa Mulungu ndipo Mulungu amakhala mwa iye. 17Chikondi chafika pachimake penipeni pakati pathu, kotero kuti pa tsiku lachiweruzo tidzakhala olimba mtima chifukwa mʼdziko lapansi moyo wathu uli ngati wa Khristu. 18Mulibe mantha mʼchikondi. Koma chikondi ndi changwiro chimachotsa mantha, chifukwa mantha amabwera chifukwa choopa chilango. Munthu amene ali ndi mantha, chikondi chake sichangwiro.

19Ife timakonda Mulungu chifukwa ndiye anayamba kutikonda. 20Ngati wina anena kuti, “Ine ndimakonda Mulungu,” koma namadana ndi mʼbale wake ndi wabodza ameneyo. Pakuti aliyense amene sakonda mʼbale wake, amene akumuona, sangathenso kukonda Mulungu amene sanamuone. 21Ndipo Iye anatipatsa lamulo lakuti: Aliyense amene amakonda Mulungu ayenera kukondanso mʼbale wake.

New Russian Translation

1 Иоанна 4:1-21

Как распознать истинный и ложный дух

1Любимые, не каждому духу верьте, но проверяйте, от Бога ли эти духи, потому что много лжепророков вышло в мир. 2Вы можете распознать Духа Божьего так: Дух, признающий, что Иисус Христос пришел в человеческом теле4:2 Букв.: «во плоти»., – это Дух от Бога. 3Но дух, не признающий Иисуса, – не от Бога. Это дух антихриста, о котором вы слышали, что он придет, и он уже есть в мире.

4Дети, вы от Бога, и вы победили этих лжепророков, потому что Тот, Кто в вас, больше того, кто в мире. 5Они от мира и поэтому говорят так, как говорят в мире, и мир слушает их. 6Но мы от Бога, и кто знает Бога, тот нас слушает, кто же не от Бога, тот не слушает нас. Так мы распознаем Духа истины и духа лжи.

Бог есть любовь

7Дорогие, будем же любить друг друга, потому что любовь от Бога, и каждый, кто любит, рожден от Бога и знает Бога. 8Кто не любит, тот не знает Бога, потому что Бог есть любовь! 9Бог проявил Свою любовь к нам в том, что послал в мир Своего единственного Сына, чтобы мы через Него получили жизнь. 10Любовь заключается не в том, что мы полюбили Бога, но в том, что Бог полюбил нас и послал Своего Сына в умилостивление за наши грехи. 11Дорогие, если Бог нас так любит, то и мы должны любить друг друга. 12Бога никто никогда не видел, но если мы любим друг друга, то в нас живет Сам Бог, и Его любовь в нас совершенна.

13Он дал нам от Своего Духа, и поэтому мы знаем, что мы в Нем, а Он в нас. 14Мы сами видели и свидетельствуем, что Отец послал Сына Спасителем мира. 15Кто признает Иисуса как Сына Божьего, в том пребывает Бог, и сам этот человек – в Боге. 16Мы узнали и поверили, что Бог нас любит.

Бог есть любовь, и тот, кто пребывает в любви, пребывает в Боге, и Бог пребывает в нем. 17Любовь достигла среди нас совершенства, так что мы можем со всей уверенностью встречать День Суда, потому что каков Он, таковы и мы в этом мире. 18В любви нет страха, но совершенная любовь прогоняет его, потому что страх связан с наказанием, и кто боится, тот еще не достиг совершенства в любви.

19Мы любим потому, что Он первый нас полюбил. 20Кто говорит: «Я люблю Бога», но ненавидит своего брата, тот лжец. Кто не любит своего брата, которого он видел, тот не может любить Бога, Которого не видел. 21И вот повеление, которое Он нам оставил: «Кто любит Бога, тот должен любить и своего брата».