1 Yohane 3 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yohane 3:1-24

1Taonani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate anatikonda nacho, kuti titchedwe ana a Mulungu! Ndipo nʼchimene ife tili! Nʼchifukwa chake dziko lapansi silitidziwa chifukwa silinamudziwe Iye. 2Abale okondedwa, tsopano ndife ana a Mulungu, ndipo sichinaoneke chimene tidzakhala. Koma tikudziwa kuti Yesu akadzaonekera, tidzafanana naye, pakuti tidzamuona Iyeyo monga momwe alili. 3Aliyense amene ali ndi chiyembekezo ichi mwa Iye adziyeretse yekha, monga Iye ali woyera.

4Aliyense amene amachimwa amaphwanya lamulo; pakuti tchimo ndi kuphwanya lamulo. 5Koma inu mukudziwa kuti Yesu anabwera kuti adzachotse machimo athu. Ndipo mwa Iye mulibe tchimo. 6Aliyense wokhala mwa Khristu sachimwa. Aliyense amene amachimwa sanamuone kapena kumudziwa.

7Ana okondedwa, musalole kuti aliyense akusocheretseni. Munthu amene amachita chilungamo ndi wolungama, monga Khristu ali wolungama. 8Iye amene amachimwa ndi wa Satana, chifukwa mdierekezi wakhala akuchimwa kuyambira pa chiyambi. Mwana wa Mulungu anaonekera kuti awononge ntchito za mdierekezi. 9Aliyense amene ndi mwana wa Mulungu, sachimwirachimwira, popeza mbewu ya Mulungu ili mwa iye, sangathe kuchimwa, chifukwa ndi mwana wa Mulungu. 10Mmenemu ndi mmene timadziwira ana a Mulungu ndi amene ali ana a mdierekezi. Aliyense amene sachita chilungamo si mwana wa Mulungu; ngakhalenso amene sakonda mʼbale wake.

Kukondana Wina ndi Mnzake

11Uthenga umene munawumva kuyambira pachiyambi ndi uwu: Tizikondana wina ndi mnzake. 12Musakhale ngati Kaini, amene anali wa woyipayo ndipo anapha mʼbale wake. Nanga anamupha chifukwa chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoyipa ndipo zochita za mʼbale wake zinali zolungama. 13Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu. 14Ife tikudziwa kuti tinatuluka mu imfa ndi kulowa mʼmoyo, chifukwa timakonda abale athu. Aliyense amene sakonda mʼbale wake akanali mu imfa. 15Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha.

16Mmene timadziwira chikondi chenicheni ndi umu: Yesu anapereka moyo wake chifukwa cha ife. Ndipo nafenso tiyenera kupereka miyoyo yathu chifukwa cha abale athu. 17Ngati wina ali ndi chuma ndipo nʼkuona mʼbale wake akusowa, koma wosamvera chisoni, kodi mwa iyeyo muli chikondi cha Mulungu? 18Ana okondedwa, chikondi chathu chisakhale cha pakamwa pokha koma cha ntchito zathu ndi mʼchoonadi. 19Pamenepo tidzadziwa kuti tili pa choonadi ndipo tidzakhala okhazikika mtima pamaso pa Mulungu, 20nthawi zonse pamene mtima wathu utitsutsa. Pakuti Mulungu ndi wamkulu kuposa mitima yathu ndipo Iye amadziwa zonse.

21Anzanga okondedwa, ngati mitima yathu sikutitsutsa, tili nako kulimbika mtima pamaso pa Mulungu. 22Ndipo timalandira chilichonse chimene tichipempha kwa Iye, chifukwa timamvera malamulo ake ndi kuchita zimene zimamukondweretsa. 23Ndipo lamulo lake ndi ili: kukhulupirira dzina la Mwana wake, Yesu Khristu, ndi kukondana wina ndi mnzake monga Iye anatilamulira. 24Iwo amene amamvera malamulo ake amakhala mwa Iye, ndipo Iye amakhala mwa iwo. Ndipo mmenemu ndi momwe timadziwira kuti Iye akukhala mwa ife. Timadziwa mwa Mzimu Woyera amene anatipatsa.

Knijga O Kristu

1 Ivanova 3:1-24

Božja djeca

1Gledajte koliku nam je ljubav Otac darovao: da se možemo nazvati Božjom djecom, a to i jesmo. Ali ljudi koji pripadaju ovom svijetu ne poznaju Boga, pa ne mogu ni razumjeti da smo mi njegova djeca. 2Da, ljubljeni moji, već smo sada Božja djeca, a što ćemo biti poslije, još se nije očitovalo. Ali jedno znamo: kad se očituje, bit ćemo njemu slični jer ćemo ga vidjeti onakvim kakav on doista jest. 3Tko ima tu nadu u njega, čisti se od grijeha, kao što je i on čist.

4Tko god čini grijeh, krši Božji zakon, jer je grijeh protivan Božjemu zakonu. 5Znate da je Isus došao da odnese naše grijehe i da u njemu nema grijeha. 6Tko god ostaje u njemu, ne čini grijeh. A tko griješi, nije ga ni vidio ni upoznao.

7Djeco draga, ne dopustite da vas itko glede toga zavede. Tko čini pravdu, čini je zato što je pravedan kao što je i Krist pravedan. 8Nastavlja li tko živjeti u grijehu, to pokazuje da pripada đavlu koji je u grijehu od početka. Ali Božji Sin je došao uništiti đavolska djela. 9Tko je rođen od Boga, ne živi u grijehu jer je u njemu Božje sjeme, pa više u grijehu i ne može živjeti; u njemu je započeo novi život—rođen je od Boga. 10Božja se djeca od đavolske raspoznaju po ovome: tko ne čini pravde i tko ne voli svoju braću, ne pripada Bogu.

Ljubav prema drugima

11Jer tu smo poruku, da volimo jedni druge, primili još na početku. 12Ne smijemo biti poput Kajina, koji je pripadao Zlome i ubio svojega brata. Zašto ga je ubio? Jer su mu djela bila zla, a djela njegova brata pravedna. 13Ne čudite se stoga, draga braćo, ako vas svijet mrzi.

14Volimo li svoju braću, znat ćemo da smo prešli iz smrti u vječni život. Onaj tko ih ne voli, još je uvijek mrtav. 15Tko god mrzi svojeg brata, u srcu je ubojica, a znate da nijedan ubojica u sebi nema trajnoga, vječnog života. 16Pravu smo ljubav spoznali jer je Krist za nas dao svoj život. Tako smo i mi dužni dati život za svoju braću. 17Ali ima li tko zemaljskih dobara te dobro živi, a vidi svojeg brata u potrebi i ostane pred njim tvrda srca—kako da ljubav Božja ostane u njemu?

18Nemojmo, djeco draga, voljeti samo riječju i jezikom, već djelom i iskreno. 19Po tome ćemo znati da smo od istine i umirit ćemo pred Gospodinom svoje srce 20ako nas ono u bilo čemu osuđuje. Jer Bog je veći od našeg srca i znade sve.

21Dragi moji, ako nas savjest ne osuđuje, možemo hrabro i s pouzdanjem doći k Bogu 22i dobit ćemo od njega sve što zatražimo jer vršimo njegove zapovijedi i činimo što mu je drago. 23A njegova je zapovijed: da vjerujemo u ime njegova Sina Isusa Krista i da volimo jedni druge kao što nam je on zapovjedio. 24Tko je poslušan Božjim zapovijedima, živi u Bogu i Bog u njemu. A da on živi u nama, znamo po Duhu kojega nam je poslao.