1 Yohane 2 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yohane 2:1-29

1Inu Ana anga okondedwa, ndikukulemberani zimenezi kuti musachimwe. Koma wina akachimwa, tili nayo Nkhoswe yotinenera kwa Atate, Yesu Khristu, Wolungamayo. 2Iyeyo ndiye nsembe yopepesera machimo athu, ndipo osati athu okha, komanso machimo onse a dziko lapansi.

Chikondi ndi Chidani

3Ife timatsimikiza kuti tikumudziwa ngati tikusunga malamulo ake. 4Munthu akamanena kuti, “Ine ndimadziwa Mulungu,” koma samvera malamulo a Mulunguyo, ndi wabodza ameneyo ndipo mwa iye mulibe choonadi. 5Koma munthu aliyense akamvera mawu ake, ndiye kuti chikondi cha Mulungu chafikadi penipeni mwa iyeyo. Pamenepo timatsimikizadi kuti tili mwa Iye. 6Aliyense amene amati amakhala mwa Mulungu, ayenera kukhala moyo umene Yesu ankakhala.

7Okondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lakale lomwe lija, limene munali nalo kuyambira pachiyambi. Lamulo la kalelo ndi mawu amene munawamva kale. 8Komabe ndi lamulo latsopano limene ndikukulemberani. Choonadi chake chikuoneka mwa Yesu ndiponso mwa inu, chifukwa mdima ukutha ndipo kuwunika kwenikweni kwayamba kale kuwala.

9Aliyense amene amati ali mʼkuwunika, koma nʼkumadana ndi mʼbale wake ali mu mdima. 10Aliyense amene amakonda mʼbale wake amakhalanso mʼkuwunika, ndipo mwa iye mulibe chokhumudwitsa. 11Koma aliyense wodana ndi mʼbale wake ali mu mdima ndipo akuyenda mu mdima. Iyeyo sakudziwa kumene akupita, chifukwa mdima wamudetsa mʼmaso mwake.

12Inu ana okondedwa, ndikukulemberani

popeza kuti machimo anu akhululukidwa chifukwa cha dzina la Yesu.

13Inu abambo, ndikukulemberani

popeza kuti munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi.

Inu anyamata, ndikukulemberani

popeza kuti munagonjetsa woyipayo.

14Ana okondedwa, ndikukulemberani

chifukwa mumawadziwa Atate.

Abambo, ndikukulemberani

chifukwa munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi.

Inu anyamata, ndikukulemberani

chifukwa ndinu amphamvu.

Mawu a Mulungu amakhala mwa inu

ndipo mumamugonjetsa woyipayo.

Musakonde Dziko Lapansi

15Musamakonde dziko lapansi kapena chilichonse cha dziko lapansi. Ngati munthu wina aliyense akonda dziko lapansi, mwa iyeyo mulibe chikondi chokonda Atate. 16Pakuti zonse za mʼdziko lapansi, zilakolako za thupi, zinthu zimene maso amakhumbira ndiponso kuyandikira zinthu za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku dziko lapansi. 17Dziko lapansi likupita pamodzi ndi zilakolako zake, koma amene amachita chifuniro cha Mulungu amakhalapo mpaka muyaya.

Anthu Okana Khristu

18Ana anga, ino ndi nthawi yotsiriza, ndipo monga munamva kale kuti anthu okana Khristu akubwera, ngakhale tsopano okana Khristu ambiri afika kale. Zimenezi zikutisonyeza kuti ino ndi nthawi yotsiriza. 19Anthu amenewa anachoka pakati pathu, komatu sanali a mʼgulu lathu. Pakuti akanakhala a mʼgulu lathu, akanakhalabe nafe, koma kuchoka kwawo kunatisonyeza kuti sanali a mʼgulu lathu.

20Koma inu muli ndi kudzoza kochokera kwa Woyerayo, ndipo nonsenu mukudziwa choonadi. 21Sindikukulemberani chifukwa choti simudziwa choonadi ayi, koma chifukwa choti mumadziwa choonadicho, ndipo mukudziwanso kuti bodza silichokera pa choonadi. 22Wabodzayo ndani? Ndi munthu aliyense amene amanena kuti Yesu si Mpulumutsi. Munthu woteroyo ndi wokana Khristu, ndiponso amakana Atate, ndi Mwana. 23Aliyense wokana Mwana alibenso Atate. Wovomereza Mwana alinso ndi Atate.

24Onetsetsani kuti zimene munazimva kuyambira pachiyambi zikhalebe mwa inu. Ngati zikhala mwa inu, inunso mudzakhala mwa Mwana ndiponso mwa Atate. 25Ndipo chimene anatilonjeza nʼchimenechi: moyo wosatha.

26Ine ndikukulemberani zimenezi kuti ndikuwuzeni za amene akufuna kukusocheretsani. 27Koma za inu, kudzoza kumene munalandira kwa Khristu kuli mwa inu, ndipo sipafunika wina aliyense kuti akuphunzitseni. Koma kudzozako kumakuphunzitsani zinthu zonse, ndipo popeza kudzoza kwakeko nʼkoona osati konama, monga munaphunzira, khalani mwa Iyeyo.

Ana a Mulungu

28Tsopano ana okondedwa, khalani mwa Yesu, kuti pamene adzaonekera, ife tidzakhale otsimikizika mu mtima ndi wopanda manyazi pamaso pake akamadzabwera.

29Popeza mukudziwa kuti Khristu ndi wolungama, choncho mukudziwanso kuti aliyense amene amachita chilungamo ndi mwana wa Mulungu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约翰一书 2:1-29

1我的孩子们,我写这些话给你们是为了叫你们不要犯罪。如果有人犯了罪,在父那里我们有一位护慰者,就是那位义者——耶稣基督。 2祂为我们的罪作了赎罪祭,不只是为我们的罪,也是为全人类的罪。

3我们若遵行上帝的命令,就知道自己认识祂。 4若有人说“我认识祂”,却不遵行祂的命令,这人是说谎的,他心中没有真理。 5遵行主话语的人是真正全心爱上帝的人,我们借此知道自己是在主里面。 6所以,自称住在主里面的,就该在生活中效法基督。

新命令

7亲爱的弟兄姊妹,我写给你们的并不是一条新命令,而是你们起初接受的旧命令,这旧命令就是你们已经听过的真道。 8然而,我写给你们的也是新命令,在基督和你们身上都显明是真实的,因为黑暗渐渐过去,真光已经照耀出来。

9若有人说自己在光明中,却恨他的弟兄姊妹,他就仍然活在黑暗里。 10爱弟兄姊妹的人活在光明中,没有什么可以绊倒他2:10 没有什么可以绊倒他”或译“他也不会绊倒别人”。11恨弟兄姊妹的人活在黑暗中,走在黑暗中,不知何去何从,因为黑暗弄瞎了他的眼睛。

12孩子们,我写信给你们,因为靠着祂的名,你们的罪已经得到赦免。 13父老们,我写信给你们,因为你们认识了从太初就存在的那位。年轻人,我写信给你们,因为你们已经战胜了那恶者。

14孩子们,我曾写信给你们,因为你们认识了父。父老们,我曾写信给你们,因为你们认识了从太初就存在的那位。年轻人,我曾写信给你们,因为你们刚强,上帝的道常存在你们心里,并且你们战胜了那恶者。

15不要爱世界和世上的事,因为人若爱世界,就不会再有爱父的心了。 16凡属世界的,如肉体的私欲、眼目的私欲和今生的骄傲都不是从父那里来的,而是从世界来的。 17这世界和其中一切的私欲都要过去,但遵守上帝旨意的人永远长存。

防备敌基督者

18孩子们,现在是末世了。你们从前听说敌基督者要来,其实现在许多敌基督者已经出现了,由此可知,现在是末世了。 19这些人是从我们中间出去的,但他们不属于我们。他们如果属于我们,就会留在我们当中了。他们的离去表明他们都不属于我们。

20你们从那位圣者领受了圣灵2:20 圣灵”希腊文指“膏抹”。,所以你们明白真理。 21我写信给你们不是因为你们不明白真理,而是因为你们明白真理,并且知道真理里面绝对没有谎言。 22谁是说谎的呢?不就是那否认耶稣是基督的吗?那不承认父和子的就是敌基督者。 23凡否认子的,也否认了父;凡承认子的,也承认了父。

24你们务要把起初所听见的教导谨记在心,这样,你们必住在子和父里面。 25主应许给我们的是永生。 26以上的话是针对那些引诱你们离开正道的人写的。

顺从圣灵

27你们既然从主领受了圣灵,圣灵又住在你们心中,就不需要其他人来教导你们,因为圣灵必会在一切事上指引你们。圣灵的教导是真实的,没有虚假,你们要按圣灵的教导住在主里面。 28孩子们,你们要住在主里面。这样,当主显现的时候,就是祂再来的时候,我们便能坦然无惧,不会在祂面前羞愧。 29既然你们知道主是公义的,也该知道所有按公义行事的人都是上帝的儿女。