1 Timoteyo 4 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 4:1-16

Malangizo kwa Timoteyo

1Mzimu akunena momveka bwino kuti mʼmasiku otsiriza anthu ena adzataya chikhulupiriro chawo ndi kutsatira mizimu yonyenga ndi zinthu zophunzitsidwa ndi ziwanda. 2Ziphunzitso zimenezi zimachokera ku chinyengo cha anthu onama, amene chikumbumtima chawo chinamatidwa ndi chitsulo cha moto. 3Iwo amaletsa anthu ukwati ndi kuwalamula kuti asamadye zakudya zina, zimene Mulungu analenga kuti amene anakhulupirira ndi kudziwa choonadi, azidye moyamika. 4Pakuti chilichonse chimene Mulungu analenga ndi chabwino, ndipo chilichonse chisasalidwe, akamachilandira moyamika, 5pakuti chimayeretsedwa ndi mawu a Mulungu ndi pemphero.

6Ngati abale uwalangiza zimenezi, udzakhala mtumiki wabwino wa Khristu Yesu, woleredwa mʼchoonadi cha chikhulupiriro ndi mʼchiphunzitso chabwino chimene wakhala ukutsata. 7Koma upewe nkhani zachabe ndi nthano za amayi okalamba; mʼmalo mwake udziphunzitse kukhala moyo wolemekeza Mulungu. 8Pakuti kulimbitsa thupi kumapindulitsapo pangʼono, koma moyo woopa Mulungu umapindulitsa pa zonse. Umatilonjeza moyo pa moyo uno ndiponso pa moyo umene ukubwerawo.

9Amenewa ndi mawu odalirika ndi oyenera kuwalandira kwathunthu. 10Nʼchifukwa chake timagwira ntchito molimbika ndi kuyesetsa, chifukwa tayika chiyembekezo chathu mwa Mulungu wamoyo, amene ndi Mpulumutsi wa anthu onse, koma makamaka wa amene amakhulupirira.

11Lamulira ndi kuphunzitsa zinthu zimenezi. 12Usalole kuti wina akupeputse chifukwa ndiwe wachinyamata, koma khala chitsanzo kwa okhulupirira pa mayankhulidwe, pa makhalidwe, pa chikondi, pa chikhulupiriro ndi pa kuyera mtima. 13Mpaka nditabwera, udzipereke powerenga mawu a Mulungu kwa anthu, kulalikira ndi kuphunzitsa. 14Usanyozere mphatso yako yomwe inapatsidwa kwa iwe kudzera mʼmawu auneneri pamene gulu la akulu ampingo linakusanjika manja.

15Uzichita zimenezi mosamalitsa ndi modzipereka kwathunthu, kuti aliyense aone kuti ukupita mʼtsogolo. 16Samala kwambiri moyo wako ndi ziphunzitso zako. Uzichitabe zimenezi chifukwa ukatero, udzadzipulumutsa ndiponso udzapulumutsa okumvetsera.

New International Version – UK

1 Timothy 4:1-16

1The Spirit clearly says that in later times some will abandon the faith and follow deceiving spirits and things taught by demons. 2Such teachings come through hypocritical liars, whose consciences have been seared as with a hot iron. 3They forbid people to marry and order them to abstain from certain foods, which God created to be received with thanksgiving by those who believe and who know the truth. 4For everything God created is good, and nothing is to be rejected if it is received with thanksgiving, 5because it is consecrated by the word of God and prayer.

6If you point these things out to the brothers and sisters,4:6 The Greek word for brothers and sisters (adelphoi) refers here to believers, both men and women, as part of God’s family. you will be a good minister of Christ Jesus, nourished on the truths of the faith and of the good teaching that you have followed. 7Have nothing to do with godless myths and old wives’ tales; rather, train yourself to be godly. 8For physical training is of some value, but godliness has value for all things, holding promise for both the present life and the life to come. 9This is a trustworthy saying that deserves full acceptance. 10That is why we labour and strive, because we have put our hope in the living God, who is the Saviour of all people, and especially of those who believe.

11Command and teach these things. 12Don’t let anyone look down on you because you are young, but set an example for the believers in speech, in conduct, in love, in faith and in purity. 13Until I come, devote yourself to the public reading of Scripture, to preaching and to teaching. 14Do not neglect your gift, which was given you through prophecy when the body of elders laid their hands on you.

15Be diligent in these matters; give yourself wholly to them, so that everyone may see your progress. 16Watch your life and doctrine closely. Persevere in them, because if you do, you will save both yourself and your hearers.