1 Timoteyo 2 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 2:1-15

Malangizo Achipembedzo

1Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika. 2Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima. 3Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu, 4amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi. 5Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu. 6Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera. 7Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.

8Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.

9Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali. 10Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.

11Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu. 12Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete. 13Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava. 14Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa. 15Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.

Słowo Życia

1 Tymoteusza 2:1-15

Wskazówki dotyczące spotkań

1Gorąco zachęcam was do modlitwy za wszystkich ludzi. Proście i błagajcie Boga, aby im pomagał i dziękujcie Mu za nich. 2Módlcie się również za rządzących i wszystkich sprawujących władzę, abyśmy mogli żyć w pokoju, zachowując godność i oddając chwałę Panu. 3Takie postępowanie jest dobre i podoba się Bogu, naszemu Zbawicielowi, 4który pragnie zbawić i doprowadzić do prawdy wszystkich ludzi. 5Istnieje bowiem tylko jeden Bóg i jeden pośrednik między Nim a ludźmi: Człowiek—Chrystus Jezus. 6To On złożył siebie jako okup za wszystkich ludzi. We właściwym czasie prawda ta została oznajmiona światu. 7Mnie zaś Bóg wybrał na apostoła i nakazał mi głosić tę nowinę poganom, nauczając ich wiary i prawdy. Jest to prawdziwe Boże powołanie. Mówiąc o tym, nie kłamię.

8Proszę więc, aby na spotkaniach mężczyźni modlili się wznosząc ku Bogu czyste ręce i mając serca wolne od gniewu oraz złości na innych ludzi. 9Kobiety zaś, przychodząc na spotkania, niech się odpowiednio ubierają—skromnie i niewyzywająco. Niech nie zwracają na siebie uwagi fryzurą, biżuterią czy modnymi ubraniami. 10Prawdziwą ozdobą kobiet, które kochają Boga, powinno być bowiem dobre postępowanie.

11Na spotkaniach niech słuchają i uczą się w pokoju i uległości. 12Nie zgadzam się, aby nauczały i rządziły swoimi mężami, ale niech zachowują pokój. 13To Adam został bowiem stworzony jako pierwszy, nie Ewa. 14I nie on został oszukany przez szatana, lecz Ewa—to ona bowiem zgrzeszyła jako pierwsza. 15Kobiety dostąpią jednak zbawienia poprzez macierzyństwo, jeśli będą wierzyć Chrystusowi, okazywać innym miłość oraz prowadzić czyste i skromne życie.