1 Timoteyo 2 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 2:1-15

Malangizo Achipembedzo

1Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika. 2Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima. 3Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu, 4amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi. 5Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu. 6Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera. 7Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.

8Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.

9Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali. 10Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.

11Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu. 12Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete. 13Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava. 14Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa. 15Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.

Knijga O Kristu

1 Timoteju 2:1-15

Upute za bogoštovlje

1Prije svega, molite se za sve ljude; prizivajte Božju milost za njih i zahvaljujte Bogu. 2Molite se i za kraljeve i za sve koji su na vlasti, da možemo živjeti u miru i spokojno, u svoj pobožnosti i svetosti. 3To je dobro i ugodno našemu Bogu Spasitelju 4jer on želi da se svi ljudi spase i da spoznaju ovu istinu: 5jedan je Bog i jedan je posrednik između Boga i ljudi, Čovjek Isus Krist, 6koji je svoj život položio kao otkupninu za sve čovječanstvo. To je poruka koju je Bog dao svijetu u pravo vrijeme. 7A ja sam—istinu govorim, ne lažem—postavljen propovjednikom i apostolom, da poučavam pogane u vjeri i istini.

8Želim da se muškarci, gdje god se okupljate, mole podižući čiste ruke prema Bogu, bez srdžbe i raspravljanja. 9A žene neka se oblače pristojno. Neka se rese skromnošću i razborom, a ne upadljivim frizurama, zlatom, biserjem ili skupocjenom odjećom. 10Žena koja se smatra vjernicom trebala bi se resiti dobrim djelima.

11Neka žene slušaju pouku i uče tiho i pokorno. 12Ne dopuštam da žena poučava niti da gospodari nad mužem. Neka šuti i sluša. 13Jer Bog je najprije stvorio Adama, pa tek onda Evu. 14I Sotona nije prevario Adama, nego Evu; ona je prva zgriješila. 15Ali Bog će ženama sačuvati život za vrijeme porođaja2:15 Ili: žena će se spasiti rađanjem djece budu li ustrajale u vjeri, ljubavi, svetosti i razboritosti.