1 Timoteyo 1 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 1:1-20

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa lamulo la Mulungu, Mpulumutsi wathu ndiponso Khristu Yesu chiyembekezo chathu.

2Kwa Timoteyo mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro.

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Ambuye athu zikhale ndi iwe.

Kutsutsa Aphunzitsi Onyenga

3Monga ndinakupempha pamene ndinkapita ku Makedoniya, khala ku Efeso komweko kuti uletse anthu ena kuphunzitsa ziphunzitso zonyenga, 4kapena kumangoyika mitima pa nthano zopeka ndi kufufuza za mayina a makolo awo. Zinthu zotere zimapititsa mʼtsogolo mikangano mʼmalo mwa ntchito ya Mulungu yomwe ndi ya chikhulupiriro. 5Cholinga cha lamuloli ndi chikondi, chomwe chimachokera mu mtima woyera, chikumbumtima chabwino ndi chikhulupiriro choona. 6Anthu ena anapatuka pa zimenezi ndipo anatsata nkhani zopanda tanthauzo. 7Iwo amafuna kukhala aphunzitsi amalamulo, koma sadziwa zimene akunena, kapena zimene akufuna kutsimikiza.

8Tikudziwa kuti Malamulo ndi abwino ngati munthu awagwiritsa ntchito bwino. 9Tikudziwanso kuti Malamulo sakhazikitsidwa chifukwa cha anthu olungama, koma ophwanya lamulo ndi owukira, osaopa Mulungu ndi ochimwa, wopanda chiyero ndi osapembedza; amene amapha abambo awo ndi amayi awo, kapena anthu ena. 10Malamulo amayikidwa chifukwa cha anthu achigololo ndi ochita zadama ndi amuna anzawo, anthu ogulitsa akapolo, abodza ndi olumbira zabodza, ndi ochita chilichonse chotsutsana ndi chiphunzitso choona. 11Chiphunzitso chimene chimagwirizana ndi Uthenga Wabwino wonena za ulemerero wa Mulungu wodala, umene Iye mwini anandisungitsa.

Chisomo cha Ambuye kwa Paulo

12Ndikuthokoza Khristu Yesu Ambuye athu, amene anandipatsa mphamvu pa ntchitoyi. Iye ananditenga kukhala wokhulupirira, nandipatsa ntchito mu utumiki wake. 13Ngakhale kuti kale ndinali wachipongwe, wozunza ndi wankhanza, anandichitira chifundo chifukwa ndinkachita mwaumbuli ndi mopanda chikhulupiriro. 14Chisomo cha Ambuye athu chinatsanulidwa pa ine mochuluka, pamodzi ndi chikhulupiriro ndi chikondi zimene zili mwa Khristu Yesu.

15Mawu odalirika ndi woyenera kuwavomereza kwathunthu ndi awa: Yesu Khristu anabwera pa dziko lapansi kudzapulumutsa ochimwa, ndipo mwa iwowo ine ndiye wochimwitsitsa. 16Ndipo pa chifukwa chimenechi, Mulungu anandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwitsitsa, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse kuti ndikhale chitsanzo cha omwe angathe kumukhulupirira ndi kulandira moyo wosatha. 17Tsopano kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Ameni.

Ntchito ya Timoteyo

18Mwana wanga Timoteyo, ndikukupatsa langizo ili molingana ndi maulosi amene aneneri ananena za iwe. Pamene ukumbukira mawu amenewa udzatha kumenya bwino nkhondo 19utagwiritsitsa chikhulupiriro ndi chikumbumtima chabwino. Ena anazikana zimenezi motero chikhulupiriro chawo chinawonongeka. 20Ena mwa amenewa ndi Humenayo ndi Alekisandro, amene ndinawapereka kwa Satana kuti aphunzire kusachita chipongwe Mulungu.

Thai New Contemporary Bible

1ทิโมธี 1:1-20

1จดหมายฉบับนี้จากข้าพเจ้าเปาโลผู้เป็นอัครทูตของพระเยซูคริสต์ตามพระบัญชาของพระเจ้าพระผู้ช่วยให้รอดของเรา และของพระเยซูคริสต์ผู้ทรงเป็นความหวังของเรา

2ถึงทิโมธีลูกแท้ของข้าพเจ้าในความเชื่อ

ขอพระคุณ พระเมตตา และสันติสุขจากพระเจ้าพระบิดาและพระเยซูคริสต์องค์พระผู้เป็นเจ้าของเรามีแก่ท่าน

คำเตือนเกี่ยวกับผู้สอนผิด

3ตามที่ข้าพเจ้าได้กำชับท่านเมื่อข้าพเจ้าไปยังแคว้นมาซิโดเนียว่าให้ท่านอยู่ที่เอเฟซัส เพื่อท่านจะได้กำชับบางคนไม่ให้สอนหลักข้อเชื่อผิดๆ อีกต่อไป 4ทั้งไม่ให้หมกมุ่นกับนิยายปรัมปราและลำดับวงศ์ตระกูลอันไม่รู้จบ ซึ่งเป็นการคาดเดาแบบส่งเดชมากกว่าจะส่งเสริมพระราชกิจของพระเจ้าซึ่งเป็นไปโดยความเชื่อ 5เป้าหมายของการกำชับนี้คือความรักอันมาจากใจบริสุทธิ์ จากจิตสำนึกที่ดีและจากความเชื่ออย่างจริงใจ 6บางคนหลงเตลิดไปจากสิ่งเหล่านี้ หันไปพูดจาไร้สาระ 7พวกเขาอยากจะเป็นครูสอนบทบัญญัติทั้งๆ ที่ไม่รู้ว่าตนเองพูดอะไรหรือยืนยันอย่างหนักแน่นถึงเรื่องอะไร

8เรารู้อยู่ว่าบทบัญญัตินั้นดีหากใช้ในทางที่ถูก 9ซึ่งหมายความว่าบทบัญญัติไม่ได้มีขึ้นเพื่อผู้ชอบธรรม แต่มีขึ้นเพื่อคนชอบแหกกฎกับคนกบฏ คนอธรรมกับคนบาป คนไม่บริสุทธิ์กับคนไม่มีศาสนา คนฆ่าพ่อกับคนฆ่าแม่ ฆาตกร 10คนสำส่อนและคนรักร่วมเพศ เพื่อคนค้าทาสกับคนโกหก และคนให้การเท็จ และเพื่อสิ่งอื่นๆ อีกสารพัดที่ขัดกับคำสอนอันมีหลัก 11ซึ่งสอดคล้องกับข่าวประเสริฐอันรุ่งโรจน์ของพระเจ้าผู้ทรงเป็นที่สรรเสริญ คือข่าวประเสริฐที่ทรงมอบหมายให้ข้าพเจ้าประกาศนี้

พระคุณของพระเจ้าต่อเปาโล

12ข้าพเจ้าขอบพระคุณพระเยซูคริสต์องค์พระผู้เป็นเจ้าของเราผู้ทรงประทานกำลังแก่ข้าพเจ้า เพราะพระองค์ทรงเห็นว่าข้าพเจ้าสัตย์ซื่อจึงทรงแต่งตั้งข้าพเจ้าให้รับใช้พระองค์ 13ถึงแม้ว่าครั้งหนึ่งข้าพเจ้าเคยหมิ่นประมาทพระองค์ ข่มเหงผู้เชื่อและก่อความรุนแรง แต่พระองค์ทรงกรุณาข้าพเจ้าเพราะข้าพเจ้าได้ทำไปด้วยความไม่รู้และไม่เชื่อ 14พระคุณขององค์พระผู้เป็นเจ้าของเราได้หลั่งลงมาแก่ข้าพเจ้าอย่างเหลือล้น พร้อมด้วยความเชื่อและความรักซึ่งอยู่ในพระเยซูคริสต์

15ข้อความนี้เป็นความจริงซึ่งสมควรแก่การยอมรับโดยไม่มีข้อกังขา คือพระเยซูคริสต์เสด็จเข้ามาในโลกเพื่อช่วยคนบาปให้รอด และในบรรดาคนบาปข้าพเจ้าเป็นตัวร้ายที่สุด 16แต่เนื่องด้วยเหตุนี้เองจึงทรงกรุณาข้าพเจ้าผู้เป็นตัวร้ายที่สุดในบรรดาคนบาป เพื่อพระเยซูคริสต์จะได้ทรงสำแดงความอดกลั้นพระทัยอันไม่จำกัดให้เป็นตัวอย่างแก่คนทั้งปวงที่จะเชื่อในพระองค์และรับชีวิตนิรันดร์ 17บัดนี้ขอพระเกียรติและพระสิริมีแด่จอมราชันองค์นิรันดร์ผู้ทรงอมตะและเราไม่อาจมองเห็นได้ ผู้ทรงเป็นพระเจ้าแต่ผู้เดียวนั้นตลอดกาลสืบๆ ไปเป็นนิตย์ อาเมน

18ทิโมธีลูกชายของข้าพเจ้า ที่ข้าพเจ้ากำชับท่านเช่นนี้ก็สอดคล้องกับคำเผยพระวจนะที่เคยมีมาเกี่ยวกับท่าน เพื่อเมื่อท่านปฏิบัติตามท่านจะได้ต่อสู้อย่างเข้มแข็ง 19จงยึดมั่นในความเชื่อและจิตสำนึกอันดี บางคนละทิ้งข้อนี้ทำให้ความเชื่อของตนอับปาง 20ในหมู่คนเหล่านี้ได้แก่ฮีเมเนอัสกับอเล็กซานเดอร์ ซึ่งข้าพเจ้ามอบไว้แก่ซาตานเพื่อเขาจะได้เรียนรู้ที่จะไม่หมิ่นประมาทพระเจ้า