1 Timoteyo 1 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 1:1-20

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa lamulo la Mulungu, Mpulumutsi wathu ndiponso Khristu Yesu chiyembekezo chathu.

2Kwa Timoteyo mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro.

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Ambuye athu zikhale ndi iwe.

Kutsutsa Aphunzitsi Onyenga

3Monga ndinakupempha pamene ndinkapita ku Makedoniya, khala ku Efeso komweko kuti uletse anthu ena kuphunzitsa ziphunzitso zonyenga, 4kapena kumangoyika mitima pa nthano zopeka ndi kufufuza za mayina a makolo awo. Zinthu zotere zimapititsa mʼtsogolo mikangano mʼmalo mwa ntchito ya Mulungu yomwe ndi ya chikhulupiriro. 5Cholinga cha lamuloli ndi chikondi, chomwe chimachokera mu mtima woyera, chikumbumtima chabwino ndi chikhulupiriro choona. 6Anthu ena anapatuka pa zimenezi ndipo anatsata nkhani zopanda tanthauzo. 7Iwo amafuna kukhala aphunzitsi amalamulo, koma sadziwa zimene akunena, kapena zimene akufuna kutsimikiza.

8Tikudziwa kuti Malamulo ndi abwino ngati munthu awagwiritsa ntchito bwino. 9Tikudziwanso kuti Malamulo sakhazikitsidwa chifukwa cha anthu olungama, koma ophwanya lamulo ndi owukira, osaopa Mulungu ndi ochimwa, wopanda chiyero ndi osapembedza; amene amapha abambo awo ndi amayi awo, kapena anthu ena. 10Malamulo amayikidwa chifukwa cha anthu achigololo ndi ochita zadama ndi amuna anzawo, anthu ogulitsa akapolo, abodza ndi olumbira zabodza, ndi ochita chilichonse chotsutsana ndi chiphunzitso choona. 11Chiphunzitso chimene chimagwirizana ndi Uthenga Wabwino wonena za ulemerero wa Mulungu wodala, umene Iye mwini anandisungitsa.

Chisomo cha Ambuye kwa Paulo

12Ndikuthokoza Khristu Yesu Ambuye athu, amene anandipatsa mphamvu pa ntchitoyi. Iye ananditenga kukhala wokhulupirira, nandipatsa ntchito mu utumiki wake. 13Ngakhale kuti kale ndinali wachipongwe, wozunza ndi wankhanza, anandichitira chifundo chifukwa ndinkachita mwaumbuli ndi mopanda chikhulupiriro. 14Chisomo cha Ambuye athu chinatsanulidwa pa ine mochuluka, pamodzi ndi chikhulupiriro ndi chikondi zimene zili mwa Khristu Yesu.

15Mawu odalirika ndi woyenera kuwavomereza kwathunthu ndi awa: Yesu Khristu anabwera pa dziko lapansi kudzapulumutsa ochimwa, ndipo mwa iwowo ine ndiye wochimwitsitsa. 16Ndipo pa chifukwa chimenechi, Mulungu anandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwitsitsa, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse kuti ndikhale chitsanzo cha omwe angathe kumukhulupirira ndi kulandira moyo wosatha. 17Tsopano kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Ameni.

Ntchito ya Timoteyo

18Mwana wanga Timoteyo, ndikukupatsa langizo ili molingana ndi maulosi amene aneneri ananena za iwe. Pamene ukumbukira mawu amenewa udzatha kumenya bwino nkhondo 19utagwiritsitsa chikhulupiriro ndi chikumbumtima chabwino. Ena anazikana zimenezi motero chikhulupiriro chawo chinawonongeka. 20Ena mwa amenewa ndi Humenayo ndi Alekisandro, amene ndinawapereka kwa Satana kuti aphunzire kusachita chipongwe Mulungu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

提摩太前書 1:1-20

1保羅奉我們救主上帝和賜我們盼望的基督耶穌的命令,作基督耶穌的使徒, 2寫信給因信主而作我真兒子的提摩太

願父上帝和我們的主基督耶穌的恩典、憐憫和平安臨到你!

謹防異端邪說

3我去馬其頓的時候,曾經勸你繼續留在以弗所,好命令那幾個人不要傳講異端邪說, 4也不要沉迷於虛構的神話和冗長的家譜,因為這些事只會引起無用的猜測和辯論,無法幫助人憑信心認識上帝的救贖計劃。 5制止這些人的目的是為了愛,這愛來自於清潔的心、無虧的良心和真實無偽的信心。 6可惜有些人卻偏離這些,轉向空洞的談論。 7他們想做律法教師,卻不明白自己所談論所主張的。

8我們知道,只要用得合宜,律法本是好的。 9因為律法並不是為義人設的,而是為了對付那些目無法紀、大逆不道、不敬畏上帝、犯罪作惡、不聖潔、貪戀世俗、謀殺父母、行兇害命、 10淫亂、同性戀、拐賣人口、說謊、起假誓的人,以及其他違反正道的人。 11這正道來自當受稱頌的上帝託付我傳揚的榮耀福音。

感謝上帝的憐憫

12我感謝賜我力量的主基督耶穌,因為祂視我忠心可靠,派我事奉祂。 13儘管我從前是個褻瀆上帝、迫害和侮辱信徒的人,但我仍然蒙了憐憫,因為那時我無知,還沒有信耶穌。 14主賜給我豐富的恩典,使我在基督耶穌裡有信心和愛心。

15有句話千真萬確、完全可信,就是「基督耶穌降世,為要拯救罪人。」在罪人中我是個罪魁, 16但我依然蒙了憐憫,因為耶穌基督要在我這個罪魁身上彰顯祂無限的忍耐,使我做那些要信靠祂並得到永生之人的榜樣。

17願尊貴、榮耀歸給那位不朽的、肉眼不能見的萬世君王——獨一無二的上帝,直到永遠。阿們!

18我兒提摩太啊,我依照從前有關你的預言,把這命令託付給你,好使你藉此打美好的仗。 19你要持守信心和無虧的良心。有些人喪掉良心,結果他們的信仰就像船觸了礁, 20其中有許米乃亞歷山大。我已經把他們交給撒旦,使他們受些教訓,不敢再說褻瀆的話。