1 Samueli 5 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 5:1-12

Bokosi la Chipangano Pakati pa Afilisti

1Afilisti atalanda Bokosi la Mulungu lija, analitenga kuchoka ku Ebenezeri kupita ku Asidodi. 2Kenaka anatenga Bokosi la Chipanganolo nabwera nalo ku nyumba ya Dagoni ndi kuliyika pambali pa Dagoni. 3Anthu a ku Asidodi atadzuka mmawa mwake, anangoona Dagoni atagwa pansi chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova! Iwo anatenga Dagoni ndi kumuyimika pamalo pake. 4Koma mmawa mwakenso atadzuka, anaona Dagoni atagwa chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova. Mutu wake ndi manja ake zinali zitaduka ndi kugwera pa khonde polowera, thunthu lake lokha ndilo linatsala. 5Nʼchifukwa chake mpaka lero ansembe a Dagoni kapena wina aliyense amene amalowa mʼkachisi wa Dagoni ku Asidodi saponda pa khonde.

6Yehova analanga koopsa anthu a ku Asidodi. Yehova anawawononga ndi kuwazunza ndi zithupsa Asidoniwa pamodzi ndi anthu a madera ozungulira. 7Anthu a ku Asidodi ataona zimene zimachitika anati, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lisakhale kuno chifukwa akutizunza ife pamodzi ndi mulungu wathu Dagoni.” 8Choncho anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anawafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu wa Israeli tichite nalo chiyani?”

Iwo anayankha kuti, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lipite ku Gati.” Kotero analichotsa Bokosi la Mulungu wa Israelilo.

9Koma atafika nalo ku Gati, Yehova analanga mzindawo, ndipo anthu anachita mantha aakulu. Iye anazunza anthu a mu mzindawo, ana ndi akulu omwe, ndi zithupsa. 10Choncho anatumiza Bokosi la Mulungu ku Ekroni.

Koma Bokosi la Mulungu lija litangofika ku Ekroni, anthu a ku Ekroni analira kuti, “Abwera nalo Bokosi la Mulungu wa Israeli kwa ife kuti atiphe pamodzi ndi anthu athu.” 11Kotero iwo anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anati, “Chotsani Bokosi la Mulungu wa Israeli, libwerere ku malo ake. Tikapanda kutero lidzatipha ife ndi anthu athu.” Pakuti mu mzinda monse munali mantha aakulu kwambiri ndipo Mulungu ankawalanga kwambiri anthu a kumeneko. 12Anthu amene sanafe anavutika ndi zithupsa, ndipo kulira kwa anthu a mu mzindamo kunamveka kumwamba.

New International Version – UK

1 Samuel 5:1-12

The ark in Ashdod and Ekron

1After the Philistines had captured the ark of God, they took it from Ebenezer to Ashdod. 2Then they carried the ark into Dagon’s temple and set it beside Dagon. 3When the people of Ashdod rose early the next day, there was Dagon, fallen on his face on the ground before the ark of the Lord! They took Dagon and put him back in his place. 4But the following morning when they rose, there was Dagon, fallen on his face on the ground before the ark of the Lord! His head and hands had been broken off and were lying on the threshold; only his body remained. 5That is why to this day neither the priests of Dagon nor any others who enter Dagon’s temple at Ashdod step on the threshold.

6The Lord’s hand was heavy on the people of Ashdod and its vicinity; he brought devastation on them and afflicted them with tumours.5:6 Hebrew; Septuagint and Vulgate tumours. And rats appeared in their land, and there was death and destruction throughout the city 7When the people of Ashdod saw what was happening, they said, ‘The ark of the god of Israel must not stay here with us, because his hand is heavy on us and on Dagon our god.’ 8So they called together all the rulers of the Philistines and asked them, ‘What shall we do with the ark of the god of Israel?’

They answered, ‘Let the ark of the god of Israel be moved to Gath.’ So they moved the ark of the God of Israel.

9But after they had moved it, the Lord’s hand was against that city, throwing it into a great panic. He afflicted the people of the city, both young and old, with an outbreak of tumours.5:9 Or with tumours in the groin (see Septuagint) 10So they sent the ark of God to Ekron.

As the ark of God was entering Ekron, the people of Ekron cried out, ‘They have brought the ark of the god of Israel round to us to kill us and our people.’ 11So they called together all the rulers of the Philistines and said, ‘Send the ark of the god of Israel away; let it go back to its own place, or it5:11 Or he will kill us and our people.’ For death had filled the city with panic; God’s hand was very heavy on it. 12Those who did not die were afflicted with tumours, and the outcry of the city went up to heaven.