1 Samueli 31 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 31:1-13

Imfa ya Sauli ndi Ana Ake

1Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa. 2Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa. 3Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza kwambiri.

4Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere kudzandizunza ine.”

Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo. 5Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa naye limodzi. 6Motero Sauli ndi ana ake atatu, wonyamula zida zake pamodzi ndi anthu ake onse anafera limodzi pa tsikulo.

7Pamene Aisraeli amene anali tsidya lina la chigwa ndi amene anali tsidya la chigwa cha Yorodani anaona kuti gulu la ankhondo la Aisraeli lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.

8Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa. 9Iwo anadula mutu wake ndi kumuvula zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo. 10Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba yopembedzera Asitoreti, ndipo thupi lake analikhomera pa khoma la mzinda wa Beti-Sani.

11Pamene anthu a ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli, 12anthu awo onse olimba mtima anayenda usiku wonse kupita ku Beti-Sani. Anakachotsa mtembo wa Sauli ndi mitembo ya ana ake pa khoma la mzinda wa Beti-Sani, ndipo anabwera nayo ku Yabesi kumene anayitentha ndi moto. 13Pambuyo pake anatenga mafupa awo ndi kuwakwirira pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

撒母耳记上 31:1-13

扫罗之死

1非利士人与以色列人交战,以色列人败逃,许多人在基利波山被杀。 2非利士人穷追扫罗及其众子,杀了扫罗的儿子约拿单亚比拿达麦基舒亚3扫罗周围战事激烈,他被弓箭手发现、射成重伤, 4就对为他拿兵器的人说:“拔出你的刀来刺死我吧,免得那些未受割礼的人来刺杀和凌辱我。”但拿兵器的人非常害怕,不敢动手,扫罗就自己伏刀自尽了。 5侍从看见扫罗已死,也伏刀自尽了。 6这样,扫罗和他三个儿子,以及为他拿兵器的人和他的军队都死了。 7平原一带和约旦河对面的以色列人见以色列军败逃、扫罗及其众子已死,都弃城而逃。于是,非利士人占据了那些城邑。

8次日,非利士人来剥阵亡者的衣物,发现扫罗和他的三个儿子横尸基利波山, 9就割下了扫罗的头颅,剥下他的盔甲,并派人走遍非利士全境,在他们偶像的庙里及民众中通告消息。 10非利士人把扫罗的盔甲放在亚斯她录神庙里,把他的尸体钉在伯·珊城墙上。 11基列·雅比人听说非利士人对扫罗的所作所为, 12他们所有的勇士就连夜赶到伯·珊,从墙上取下扫罗和他儿子们的尸体,带到雅比火化, 13把骨灰葬在雅比的垂丝柳树下,又为他们禁食了七天。