1 Samueli 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 3:1-21

Yehova Ayitana Samueli

1Samueli ankatumikira Yehova moyangʼaniridwa ndi Eli. Masiku amenewo mawu a Yehova sankamveka pafupipafupi. Kuona zinthu mʼmasomphenya sikunkachitikanso kawirikawiri.

2Tsiku lina Eli, amene maso anali ofowoka ndi kuti sankatha kuona bwino, anagona pa malo ake. 3Nthawiyi nʼkuti nyale ya Mulungu isanazimitsidwe. Samueli anali gone mu Nyumba ya Yehova, kumene kunali Bokosi la Chipangano cha Mulungu. 4Yehova anayitana Samueli.

Iye anayankha kuti, “Wawa.” 5Ndipo iyeyo anathamangira kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera ndamva kuyitana.”

Koma Eli anati, “Ine sindinakuyitane, bwerera kagone.” Ndipo iye anapita kukagona.

6Yehova anayitananso, “Samueli!” Ndipo Samueli anadzuka ndi kupita kwa Eli nati, “Ndabwera popeza ndamva mukundiyitana.”

Eli nati, “Mwana wanga, ine sindinakuyitane, bwerera kagone.”

7Nthawiyi nʼkuti Samueli asanadziwe Yehova ndipo Mawu a Yehova nʼkuti asanawululidwe kwa iye.

8Yehova anayitananso Samueli kachitatu ndipo Samueli anadzuka ndikupita kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera popeza mwandiyitana ndithu.”

Apo Eli anazindikira kuti Yehova ndiye ankayitana mnyamatayo. 9Tsono Eli anamuwuza Samueli kuti, “Pita ukagone ndipo akakuyitananso ukanene kuti, ‘Yankhulani Yehova, pakuti mtumiki wanu ndikumvetsera.’ ” Choncho Samueli anapita ndi kukagona pamalo pake.

10Yehova anabwera ndi kuyima pomwepo, ndi kuyitana monga nthawi zina zija, “Samueli! Samueli!”

Ndipo Samueli anayankha, “Yankhulani, pakuti mtumiki wanu akumvetsera.”

11Ndipo Yehova anati kwa Samueli, “Taona, patsala pangʼono kuti ndichite chinthu china mu Israeli chimene chidzadabwitsa aliyense amene adzamve. 12Tsiku limenelo ndidzachitadi zonse zimene ndinayankhula zokhudza banja la Eli kuyambira poyamba mpaka pomaliza. 13Pakuti ndinamudziwitsa kuti Ine ndikhoza kulanga banja lake kwamuyaya chifukwa cha zoyipa zimene ana ake ankadziyipitsa nazo. Iye ankadziwa zimenezi koma osawaletsa. 14Nʼchifukwa chake ndinalumbira kuti, ‘Zoyipa zimene banja la Eli linandichita sizidzafafanizidwa mpaka muyaya ngakhale adzapereke nsembe kapena zopereka zina.’ ”

15Samueli anagona mpaka mmawa. Atadzuka anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova. Iye anachita mantha kumuwuza Eli za masomphenya ake. 16Koma Eli anamuyitana nati, “Samueli mwana wanga.”

Samueli anayankha kuti, “Wawa.”

17Tsono Eli anafunsa kuti, “Yehova wakuwuza chiyani? Usandibisire. Mulungu akulange ndithu ngati undibisira chilichonse cha zimene wakuwuza.” 18Choncho Samueli anamuwuza zonse, sanamubisire kalikonse. Ndipo Eli anati, “Iye ndi Yehova, mulekeni achite chimene chamukomera.”

19Yehova anali ndi Samueli pamene amakula, ndipo zonse zimene ankayankhula zinkachitikadi. 20Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dera la Dani mpaka ku Beeriseba anazindikira kuti Yehova analozadi chala pa Samueli kuti akhale mneneri wake. 21Yehova anapitiriza kuoneka ku Silo, ndipo kumeneko anadziwulula yekha kwa Samueli mwa mawu ake.

New Russian Translation

1 Царств 3:1-21

Господь призывает Самуила

1Мальчик Самуил служил перед Господом под руководством Илия. В те дни слово Господа было редким; не часты были и видения.

2Как-то ночью Илий, чьи глаза ослабели настолько, что он едва мог видеть, лежал на своем обычном месте. 3Светильник Бога еще не догорел, и Самуил лежал в храме Господа, где находился ковчег Бога. 4Господь позвал Самуила, и Самуил ответил:

– Вот я.

5Он подбежал к Илию, сказав:

– Вот я. Ты звал меня?

Но Илий сказал:

– Я не звал тебя, возвращайся и ложись.

Он пошел и лег.

6Господь позвал его вновь:

– Самуил!

Самуил поднялся, пришел к Илию и сказал:

– Вот я. Ты звал меня?

– Мой сын, – сказал Илий, – я не звал тебя, возвращайся и ложись спать.

7Самуил не знал еще Господа: слово Господа еще не открывалось ему. 8Господь позвал Самуила в третий раз, и Самуил поднялся, пришел к Илию и сказал:

– Вот я. Ты звал меня?

Тогда Илий понял, что мальчика зовет Господь. 9Илий сказал Самуилу:

– Иди и ложись, и если Он позовет тебя, скажи: «Говори, Господи, Твой слуга слушает Тебя».

Самуил пошел и лег на свое место. 10Господь пришел и встал там, призывая, как в первый и во второй раз:

– Самуил! Самуил!

Тогда Самуил сказал:

– Говори, Твой слуга слушает Тебя.

11И Господь сказал Самуилу:

– Я собираюсь совершить в Израиле такое, от чего у каждого, кто услышит об этом, зазвенит в ушах. 12Тогда Я исполню над Илием все, что говорил о его семье, – от начала до конца. 13Ведь Я говорил ему, что накажу его семью навеки из-за греха, о котором он знал; его сыновья сделались презренными3:13 Или: «хулили Бога»., а он не обуздывал их. 14Поэтому Я клянусь дому Илия: вина дома Илия никогда не будет заглажена жертвой или приношением.

15Самуил лежал до утра, а затем открыл двери дома Господа. Он боялся передать Илию видение, 16но Илий позвал его и сказал:

– Самуил, мой сын.

Самуил ответил:

– Вот я.

17– Что Он сказал тебе? – спросил Илий. – Не скрывай от меня. Бог сурово накажет тебя3:17 Букв.: «то и то сделает тебе Бог и еще добавит»., если ты скроешь от меня что-либо из того, что Он сказал тебе.

18Самуил рассказал ему все, ничего не скрывая. Тогда Илий сказал:

– Он – Господь; пусть поступает, как Ему угодно.

19Господь был с Самуилом, когда тот вырос, и не оставил несбывшимся ни одного из его слов. 20Весь Израиль от Дана до Вирсавии признал, что Самуил – истинный пророк Господа. 21Господь продолжал являться в Шило, и там Он открылся Самуилу через Свое слово.