1 Samueli 29 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 29:1-11

Afilisti Akana Davide

1Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli. 2Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi. 3Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?”

Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”

4Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa? 5Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti,

“ ‘Sauli wapha anthu 1,000

koma Davide wapha miyandamiyanda?’ ”

6Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna. 7Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”

8Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”

9Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’ 10Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”

11Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.

New Russian Translation

1 Царств 29:1-11

Филистимляне отказываются от помощи Давида

1Филистимляне собрали все свои войска в Афеке, а израильтяне разбили лагерь у источника в Изрееле. 2Когда филистимские правители шли со своими сотнями и тысячами воинов, Давид и его люди шли сзади с Ахишем. 3Начальники филистимлян спросили:

– Что делают здесь эти евреи?

Ахиш ответил:

– Ведь это Давид, который был слугой Саула, царя Израиля! Он у меня уже больше года, и с того дня, когда он покинул Саула, я не нашел в нем ничего плохого.

4Но филистимские начальники разгневались на него и сказали:

– Отошли этого человека назад, пусть возвращается на место, которое ты ему определил. Он не должен идти с нами на войну, иначе он обратится против нас во время сражения. Чем еще он мог бы примириться со своим господином, как не головами наших людей? 5Разве это не тот Давид, о котором они, танцуя, пели:

«Саул сразил тысячи,

а Давид – десятки тысяч?»

6Ахиш призвал Давида и сказал ему:

– Верно, как и то, что жив Господь: ты честен, и мне было бы приятно позволить тебе служить со мной в войске. С того дня, когда ты пришел ко мне, и до сегодняшнего дня я не нашел в тебе ничего плохого, но вожди тебя не одобряют. 7Поворачивай и иди с миром; не делай ничего, что могло бы рассердить филистимских правителей.

8– Но что же я сделал? – спросил Давид. – Что плохого ты нашел в твоем слуге с того дня, когда я пришел к тебе, и до сегодняшнего дня? Почему я не могу идти и сражаться с врагами моего господина царя?

9Ахиш ответил:

– Я знаю, ты был в моих глазах хорош, как Божий ангел, но филистимские вожди сказали: «Он не должен идти с нами на войну». 10Итак, поднимись рано вместе со слугами твоего господина, которые пришли с тобой. Встаньте на рассвете и уходите.

11Давид и его люди встали рано утром, чтобы вернуться в филистимскую землю, а филистимляне поднялись к Изреелю.