1 Samueli 28 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 28:1-25

Sauli ndi Mfiti ya ku Endori

1Mʼmasiku amenewo Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo kuti akamenyane ndi Aisraeli. Akisi anawuza Davide kuti, “Udziwe kuti iwe pamodzi ndi anthu ako mudzapita nane ku nkhondo.”

2Davide anayankha kuti, “Tsono inu mudzaona zimene mtumiki wanune ndingachite.”

Akisi anayankha kuti, “Chabwino ine ndidzakuyika iwe kukhala mlonda wanga moyo wako wonse.”

3Nthawi imeneyi nʼkuti Samueli atamwalira, ndipo Aisraeli onse anamulira namuyika mʼmanda ku mzinda wake wa Rama. Sauli anali atachotsa mʼdzikomo anthu owombeza mawula ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa.

4Tsono Afilisti anasonkhana nabwera kudzamanga misasa yawo ku Sunemu. Nayenso Sauli anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kumanga misasa yawo ku Gilibowa. 5Sauli ataona gulu lankhondo la Afilisti anaopa ndipo ananjenjemera kwambiri. 6Choncho Sauli anafunsa nzeru kwa Yehova koma Yehova sanamuyankhe ngakhale kudzera mʼmaloto, kapena mwa Urimu ngakhalenso kudzera mwa aneneri. 7Kenaka Sauli anawuza nduna zake kuti, “Mundipezere mkazi amene amawombeza mawula kuti ndipite ndikafunse kwa iye.”

Nduna zakezo zinamuyankha kuti, “Alipo mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ku Endori.”

8Kotero Sauli anadzizimbayitsa navala zovala zachilendo. Tsono iye pamodzi ndi anthu awiri anapita nakafika kwa mkazi uja usiku, ndipo anamupempha kuti, “Chonde ndifunsireni nzeru kwa mizimu ya anthu akufa. Koma makamaka munditulutsire mzimu wa amene ndimutchule.”

9Koma mkaziyo anayankha kuti, “Ndithu inu mukudziwa chimene Sauli anachita. Paja iye anachotsa mʼdziko muno anthu onse owombeza ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Chifukwa chiyani mukutchera moyo wanga msampha kuti ndiphedwe?”

10Koma Sauli analonjeza mkaziyo molumbira nati, “Pali Yehova wamoyo, iweyo sudzalangidwa chifukwa cha zimenezi.”

11Kenaka mkaziyo anafunsa, “Ndikuyitanireni yani?”

Iye anati, “Undiyitanire Samueli.”

12Pamene mkaziyo anaona Samueli anakuwa kwambiri, nawuza Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani inu mwandipusitsa? Inu ndinu Sauli!”

13Mfumuyo inamuwuza kuti, “Usaope. Kodi ukuona chiyani?”

Mkaziyo anayankha kuti, “Ndikuona mzimu ukutuluka pansi.”

14Sauli anafunsa, “Kodi mzimuwo ukuoneka motani?”

Mkaziyo anayankha kuti, “Amene akutuluka ndi munthu wokalamba ndipo wavala mkanjo.”

Apo Sauli anadziwa kuti anali Samueli ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.

15Samueli anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandivutitsa pondiyitana kuti ndibwere kuno?”

Sauli anayankha kuti, “Ine ndavutika kwambiri mʼmaloto. Afilisti akumenyana nane, ndipo Mulungu wandifulatira. Iye sakundiyankhulanso, ngakhale kudzera mwa aneneri kapena maloto. Choncho ndakuyitanani kuti mundiwuze zoti ndichite.”

16Samueli anati, “Nʼchifukwa chiyani ukundifunsa ine, pakuti tsopano Yehova wakufulatira ndipo wasanduka mdani wako? 17Yehova wakuchita zimene ananeneratu kudzera mwa ine. Yehova wachotsa ufumu mʼmanja mwako ndipo waupereka kwa mnansi wako, kwa Davide. 18Yehova wachita zimenezi lero chifukwa sunamvere mawu ake ndipo sunawawonongeretu Aamaleki. 19Yehova adzapereka ndithu iweyo pamodzi ndi Aisraeli kwa Afilisti. Ndipo mmawa iweyo ndi ana ako mudzakhala ndi ine kuno. Ndithu Yehova adzapereka gulu lankhondo la Aisraeli kwa Afilisti.”

20Nthawi yomweyo Sauli anagwa pansi atadzazidwa ndi mantha chifukwa cha mawu a Samueli. Analibenso mphamvu, pakuti sanadye tsiku lonse.

21Mkazi uja tsono anasendera kufupi ndi Sauli, ndipo ataona kuti Sauli akuchita mantha, anamuwuza kuti, “Taonani, mdzakazi wanune ndakumverani. Ndayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndamvera zimene munandiwuza. 22Tsono inunso mumvere mawu a mdzakazi wanune. Mundilole kuti ndikupatseni ka buledi pangʼono kuti mukhale ndi mphamvu zoyendera pa ulendo wanu.”

23Iye anakana ndipo anati, “Ayi, ine sindidya.”

Koma nduna zake pamodzi ndi mkaziyo anamuwumiriza, ndipo anawamvera. Choncho anadzuka pansi nakhala pa bedi.

24Mkaziyo anali ndi mwana wangʼombe wonenepa ndipo anamupha mwachangu. Anatenga ufa nawukanyanga ndipo anaphika buledi wopanda yisiti. 25Tsono anapereka bulediyo kwa Sauli ndi nduna zake ndipo anadya. Pambuyo pake ananyamuka kupita kwawo usiku womwewo.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

撒母耳记上 28:1-25

扫罗求问巫婆

1非利士人召集大军与以色列人交战。亚吉大卫说:“你应该明白,你和部下要随我一起出战。” 2大卫答道:“仆人愿意效劳。”亚吉说:“很好!你就终生做我的护卫吧。” 3那时撒母耳已经死了,以色列举国都为他哀悼,把他葬在他的家乡拉玛。当时,扫罗把所有占卜和行巫术的都逐出了以色列4非利士人集合起来,在书念扎营,扫罗率领以色列军队在基利波扎营。 5扫罗看见非利士军队声势浩大,感到胆战心惊, 6就求问耶和华,但耶和华没有借着梦、乌陵或先知回答他。 7于是,扫罗命令臣仆找一个巫婆来,好求问她。臣仆在隐·多珥找到一个巫婆。

8扫罗乔装打扮,由两个人陪同乘夜赶到那妇人家里,说:“请你用法术把我要求问的亡灵招上来吧。” 9妇人对他说:“你知道扫罗铲除了国内占卜的和行巫术的,你为何来陷害我,置我于死地?” 10扫罗凭耶和华向妇人起誓,说:“我凭永活的耶和华起誓,你必不会因为此事而受到惩罚。” 11妇人问道:“你想让我招谁上来呢?”扫罗答道:“招撒母耳上来。” 12妇人看见了撒母耳,就惊叫起来,对扫罗说:“你是扫罗,你为什么骗我呢?” 13扫罗对她说:“不用害怕,你看见什么了?”妇人说:“我看见一个灵从地里上来。” 14扫罗说:“他是什么模样?”妇人说:“是个身披长袍的老人。”扫罗知道是撒母耳,便俯伏在地,向他下拜。 15撒母耳扫罗说:“你为什么打扰我,招我上来呢?”扫罗答道:“我深陷困境,非利士人与我们交战,上帝也撇弃了我,不再借着先知或梦来回答我。因此,我只好招你上来,好告诉我该怎么办。” 16撒母耳说:“既然耶和华已经离弃了你,与你为敌,你为什么还来问我? 17耶和华应验了祂借着我所说的预言,祂已把你的国权夺去,交给了你的同胞大卫18耶和华今天这样对待你,是因为你没有听从祂的吩咐,没有把祂憎恶的亚玛力人灭绝。 19耶和华必把你和以色列人交在非利士人手里,明天你和你的儿子们必跟我在一起了。耶和华必把以色列的军队交在非利士人手里。”

20扫罗听了撒母耳的话,顿时吓得浑身僵直,倒在地上,一天一夜没有进食,毫无力气。 21妇人到扫罗跟前,看见他惊恐万分,就对他说:“婢女冒着生命危险服从你的命令,照你的吩咐做了。 22现在,请你听婢女的话,让我给你一些食物吃,你好有体力赶路。” 23扫罗不肯,说:“我不吃。”他的随从和妇人再三劝告,他才同意了,从地上起来坐到床上。 24妇人连忙宰了家中一只小肥牛,又和面烤了无酵饼, 25摆在扫罗和他的随从面前,他们吃完后,当天晚上就离开了。