1 Samueli 28 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 28:1-25

Sauli ndi Mfiti ya ku Endori

1Mʼmasiku amenewo Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo kuti akamenyane ndi Aisraeli. Akisi anawuza Davide kuti, “Udziwe kuti iwe pamodzi ndi anthu ako mudzapita nane ku nkhondo.”

2Davide anayankha kuti, “Tsono inu mudzaona zimene mtumiki wanune ndingachite.”

Akisi anayankha kuti, “Chabwino ine ndidzakuyika iwe kukhala mlonda wanga moyo wako wonse.”

3Nthawi imeneyi nʼkuti Samueli atamwalira, ndipo Aisraeli onse anamulira namuyika mʼmanda ku mzinda wake wa Rama. Sauli anali atachotsa mʼdzikomo anthu owombeza mawula ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa.

4Tsono Afilisti anasonkhana nabwera kudzamanga misasa yawo ku Sunemu. Nayenso Sauli anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kumanga misasa yawo ku Gilibowa. 5Sauli ataona gulu lankhondo la Afilisti anaopa ndipo ananjenjemera kwambiri. 6Choncho Sauli anafunsa nzeru kwa Yehova koma Yehova sanamuyankhe ngakhale kudzera mʼmaloto, kapena mwa Urimu ngakhalenso kudzera mwa aneneri. 7Kenaka Sauli anawuza nduna zake kuti, “Mundipezere mkazi amene amawombeza mawula kuti ndipite ndikafunse kwa iye.”

Nduna zakezo zinamuyankha kuti, “Alipo mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ku Endori.”

8Kotero Sauli anadzizimbayitsa navala zovala zachilendo. Tsono iye pamodzi ndi anthu awiri anapita nakafika kwa mkazi uja usiku, ndipo anamupempha kuti, “Chonde ndifunsireni nzeru kwa mizimu ya anthu akufa. Koma makamaka munditulutsire mzimu wa amene ndimutchule.”

9Koma mkaziyo anayankha kuti, “Ndithu inu mukudziwa chimene Sauli anachita. Paja iye anachotsa mʼdziko muno anthu onse owombeza ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Chifukwa chiyani mukutchera moyo wanga msampha kuti ndiphedwe?”

10Koma Sauli analonjeza mkaziyo molumbira nati, “Pali Yehova wamoyo, iweyo sudzalangidwa chifukwa cha zimenezi.”

11Kenaka mkaziyo anafunsa, “Ndikuyitanireni yani?”

Iye anati, “Undiyitanire Samueli.”

12Pamene mkaziyo anaona Samueli anakuwa kwambiri, nawuza Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani inu mwandipusitsa? Inu ndinu Sauli!”

13Mfumuyo inamuwuza kuti, “Usaope. Kodi ukuona chiyani?”

Mkaziyo anayankha kuti, “Ndikuona mzimu ukutuluka pansi.”

14Sauli anafunsa, “Kodi mzimuwo ukuoneka motani?”

Mkaziyo anayankha kuti, “Amene akutuluka ndi munthu wokalamba ndipo wavala mkanjo.”

Apo Sauli anadziwa kuti anali Samueli ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.

15Samueli anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandivutitsa pondiyitana kuti ndibwere kuno?”

Sauli anayankha kuti, “Ine ndavutika kwambiri mʼmaloto. Afilisti akumenyana nane, ndipo Mulungu wandifulatira. Iye sakundiyankhulanso, ngakhale kudzera mwa aneneri kapena maloto. Choncho ndakuyitanani kuti mundiwuze zoti ndichite.”

16Samueli anati, “Nʼchifukwa chiyani ukundifunsa ine, pakuti tsopano Yehova wakufulatira ndipo wasanduka mdani wako? 17Yehova wakuchita zimene ananeneratu kudzera mwa ine. Yehova wachotsa ufumu mʼmanja mwako ndipo waupereka kwa mnansi wako, kwa Davide. 18Yehova wachita zimenezi lero chifukwa sunamvere mawu ake ndipo sunawawonongeretu Aamaleki. 19Yehova adzapereka ndithu iweyo pamodzi ndi Aisraeli kwa Afilisti. Ndipo mmawa iweyo ndi ana ako mudzakhala ndi ine kuno. Ndithu Yehova adzapereka gulu lankhondo la Aisraeli kwa Afilisti.”

20Nthawi yomweyo Sauli anagwa pansi atadzazidwa ndi mantha chifukwa cha mawu a Samueli. Analibenso mphamvu, pakuti sanadye tsiku lonse.

21Mkazi uja tsono anasendera kufupi ndi Sauli, ndipo ataona kuti Sauli akuchita mantha, anamuwuza kuti, “Taonani, mdzakazi wanune ndakumverani. Ndayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndamvera zimene munandiwuza. 22Tsono inunso mumvere mawu a mdzakazi wanune. Mundilole kuti ndikupatseni ka buledi pangʼono kuti mukhale ndi mphamvu zoyendera pa ulendo wanu.”

23Iye anakana ndipo anati, “Ayi, ine sindidya.”

Koma nduna zake pamodzi ndi mkaziyo anamuwumiriza, ndipo anawamvera. Choncho anadzuka pansi nakhala pa bedi.

24Mkaziyo anali ndi mwana wangʼombe wonenepa ndipo anamupha mwachangu. Anatenga ufa nawukanyanga ndipo anaphika buledi wopanda yisiti. 25Tsono anapereka bulediyo kwa Sauli ndi nduna zake ndipo anadya. Pambuyo pake ananyamuka kupita kwawo usiku womwewo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

1 Царств 28:1-25

1В те дни филистимляне собрали свои войска, чтобы воевать с Исроилом. Ахиш сказал Довуду:

– Ты со своими людьми должен выступить со мной в войске.

2Довуд сказал Ахишу:

– Хорошо. Ты узнаешь, что может сделать твой раб.

Ахиш ответил:

– Прекрасно! Я на всю жизнь сделаю тебя своим телохранителем.

Шаул у ендорской колдуньи

3Самуил умер, и все исроильтяне оплакали и похоронили его в Раме, в его родном городе. Шаул изгнал из страны колдунов и вызывателей умерших.

4Филистимляне собрались, пришли и разбили лагерь в городе Шунеме, а Шаул собрал всех исроильтян и разбил лагерь на горной вершине в Гильбоа. 5Увидев филистимское войско, Шаул испугался, его сердце охватил страх. 6Он спрашивал Вечного, но Вечный не отвечал ему ни в снах, ни через священный жребий28:6 Букв.: «урим («свет»)». См. сноску на 2:28., ни через пророков.

7Тогда Шаул сказал своим слугам:

– Найдите мне женщину-колдунью. Я пойду к ней и спрошу её.

– В Ен-Доре есть одна колдунья, – сказали ему слуги.

8Шаул, изменив свою внешность и надев другие одежды, отправился в путь вместе с двумя спутниками и ночью пришёл к той женщине.

– Спроси для меня духа, – сказал он, – и вызови мне того, кого я тебе назову.

9Но женщина сказала ему:

– Ты, конечно, знаешь о том, что сделал Шаул. Он выгнал из страны колдунов и вызывателей умерших28:9 Или: «Он по всей стране предал смерти колдунов и вызывателей умерших».. Зачем же ты расставляешь ловушку мне на погибель?

10Шаул поклялся ей Вечным:

– Верно, как и то, что жив Вечный, – ты не будешь за это наказана.

11Тогда женщина спросила:

– Кого же тебе вызвать?

– Вызови мне Самуила, – сказал он.

12Когда женщина увидела Самуила, она громко вскрикнула и сказала Шаулу:

– Почему ты меня обманул? Ты – Шаул!

13Царь сказал ей:

– Не бойся. Что ты видишь?

Женщина сказала:

– Я вижу духа, который поднимается из земли.

14Как он выглядит? – спросил он.

– Поднимается старик, одетый в верхнюю одежду, – сказала она.

Тогда Шаул понял, что это Самуил, и почтительно поклонился ему лицом до земли.

15Самуил сказал Шаулу:

– Зачем ты тревожишь меня? Зачем вызываешь?

– Я в большой беде, – сказал Шаул. – Филистимляне воюют со мной, а Всевышний от меня отвернулся. Он больше не отвечает мне ни через пророков, ни в сновидениях. Поэтому-то я и позвал тебя, чтобы ты сказал мне, что делать.

16– Зачем же ты спрашиваешь меня, если Вечный отвернулся от тебя и стал твоим врагом? – ответил Самуил. – 17Вечный совершил то, о чем Он предсказал через меня. Вечный вырвал царство из твоих рук и отдал его одному из тех, кто рядом с тобой, – Довуду. 18Так как ты не послушался Вечного и не обрушил на амаликитян Его пылающего гнева, Вечный сегодня и сделал с тобой это. 19Вечный отдаст Исроил вместе с тобой филистимлянам, и завтра ты и твои сыновья будете со мной. А ещё Вечный отдаст филистимлянам исроильское войско.

20Шаул, в ужасе от слов Самуила, тотчас же рухнул всем телом на землю. Силы оставили его, потому что он ничего не ел весь день и всю ночь. 21Подойдя к Шаулу и увидев, как он потрясён, женщина сказала:

– Твоя рабыня послушалась тебя. Рискнув жизнью, я сделала то, что ты мне сказал. 22Пожалуйста, послушайся и ты своей рабыни и позволь мне предложить тебе кусок хлеба, чтобы ты поел и у тебя появились силы, прежде чем ты тронешься в путь.

23Он сказал:

– Я не буду есть.

Но его люди присоединились к уговорам женщины, и он послушался их. Он поднялся с земли и сел на постель. 24У женщины был упитанный телёнок, которого она немедленно заколола. Она взяла муки, замесила её и испекла лепёшки без закваски. 25Затем она поставила их перед Шаулом и его людьми, и они поели. Той же ночью они встали и ушли.