1 Samueli 25 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 25:1-44

Davide, Nabala ndi Abigayeli

1Samueli anamwalira, ndipo Aisraeli onse anasonkhana kudzalira maliro ake ndipo anamuyika mʼmanda ku mudzi kwawo ku Rama.

Ndipo Davide anapita ku chipululu cha Parani. 2Kunali munthu wina wolemera kwambiri ku Maoni amene malo ake a ntchito anali ku Karimeli. Iyeyu anali ndi mbuzi 1,000 ndi nkhosa 3,000. 3Dzina lake linali Nabala ndipo anali wa fuko la Kalebe. Dzina la mkazi wake linali Abigayeli. Anali mkazi wanzeru ndi wokongola, koma mwamuna wake, wa banja la Kalebe, anali wowuma mtima ndi wamwano pa zochita zake.

4Davide anamva akanali ku chipululu kuti Nabala akumeta nkhosa. 5Choncho anatuma anyamata khumi nawawuza kuti, “Pitani kwa Nabala ku Karimeli ndipo mukamulonjere mʼdzina langa. 6Mukamuwuze kuti, ‘Mtendere ukhale ndi inu, banja lanu pamodzi ndi zonse zimene muli nazo.

7“ ‘Tsono ndamva kuti muli ndi anthu ometa nkhosa. Pamene abusa anu anali nafe kuno, sitinawachite china chilichonse choyipa, ndipo sanasowe kanthu pa nthawi yonse imene anali ku Karimeli. 8Muwafunse antchito anu ndipo akuwuzani. Kotero akomereni mtima anyamata anga, pakuti tabwera pa nthawi yachikondwerero. Chonde apatseniko antchito anuwo ndi mwana wanu Davide chilichonse chimene mungakhale nacho.’ ”

9Anyamata a Davide aja atafika, anamuwuza Nabala zonse zimene Davide anayankhula. Ndipo anadikira yankho.

10Nabala anayankha anyamata a Davide kuti, “Kodi Davide ndi ndani? Mwana wa Yese ndi ndani? Masiku ano pali antchito ambiri amene akuthawa kwa mabwana awo. 11Nditengerenji buledi, madzi ndi nyama zimene ndaphera anthu anga ometa nkhosa ndi kuzipereka kwa anthu amene sindikudziwa kumene achokera?”

12Choncho anyamata a Davide aja anatembenuka nabwerera. Atafika anafotokozera Davide mawu onse a Nabala. 13Davide anawuza anthu ake kuti, “Aliyense amangirire lupanga lake!” Choncho aliyense anamangirira lupanga lake. Davidenso anamangirira lupanga lake. Anthu pafupifupi 400 ndiwo anapita ndi Davide, pamene anthu 200 anatsala ndi katundu.

14Tsono mmodzi mwa antchito anawuza Abigayeli mkazi wa Nabala kuti, “Davide anatumiza amithenga kuchokera ku chipululu kudzalonjera mbuye wathu, koma iye anawalalatira. 15Komatu anthuwa anatichitira zabwino kwambiri. Sanatizunze, ndipo nthawi yonse imene tinali nawo ku busa sitinasowe kanthu. 16Ankatitchinjiriza ngati mpanda usiku ndi usana nthawi yonse tinkaweta nkhosa. 17Tsono onani chimene mungachite, chifukwa zimenezi zingadzetse tsoka pa mbuye wathu pamodzi ndi nyumba yake. Paja mbuye athu aja ndi munthu wa khalidwe loyipa moti palibe amene angathe kuyankhula naye.”

18Ndipo Abigayeli sanataye nthawi. Iye anatenga malofu a buledi 200, matumba a chikopa awiri a vinyo, nkhosa zisanu zowotcheratu, makilogalamu 17 a tirigu wokazinga, makeke a mphesa zowuma 100, ndiponso makeke a nkhuyu 200, ndipo anazisenzetsa abulu. 19Kenaka anawuza antchito ake kuti, “Tsogolani, ine ndikutsatirani.” Koma sanawuze mwamuna wake Nabala.

20Mayi uja atakwera pa bulu wake ndi kufika pa tsinde la phiri, anangoona Davide ndi ankhondo ake akubwera kunali iye. Choncho anakumana nawo. 21Nthawiyi nʼkuti Davide atanena kuti, “Kani ndinalondera pachabe katundu wa munthu uyu mʼchipululu muja! Ndipotu palibe kanthu nʼkamodzi komwe kake kamene kanasowa. Tsono wandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino. 22Mulungu andilange kwambiri ngati pofika mmawa nditakhale nditasiyako ngakhale munthu mmodzi mwa onse amene ali nawo.”

23Abigayeli ataona Davide, anatsika pa bulu wake mofulumira ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pa Davide. 24Ali chigonere choncho pa mapazi a Davide anati, “Mbuye wanga, kulakwa kukhale pa ine ndekha. Chonde lolani kuti mdzakazi wanune ndiyankhule nanu, ndipo mumve mawu a ine mdzakazi wanu. 25Mbuye wanga musasamale za mwamuna wanga Nabala, munthu wa khalidwe loyipa. Iyeyu ali monga dzina lake liliri. Monga dzina lake litanthauza kuti chitsiru, ndiye kuti zake zonse ndi zauchitsiru basi. Koma ine mdzakazi wanu, sindinawaone anthu amene mbuye wanga munawatuma. 26Tsono mbuye wanga muli apa, ndikulumbira pali Yehova wamoyo amene wakuletsani kuti musakhetse magazi a munthu ndi kulipsira nokha, kuti adani anu amene afuna kukuchitani zoyipa adzakhale ngati Nabala. 27Choncho, nazi mphatso zimene mdzakazi wanu ndabwera nazo kwa mbuye wanga kuti zipatsidwe kwa anyamata amene muli nawo. 28Chonde khululukani zolakwa za ine mdzakazi wanu. Ndithu Yehova adzakhazikitsa banja la mbuye wanga mu ufumu, popeza mukumenya nkhondo ya Yehova. Choncho choyipa sichidzapezeka mwa inu masiku onse a moyo wanu. 29Ngati munthu wina akuwukirani ndi kukulondani, Yehova Mulungu wanu adzateteza moyo wa mbuye wanga monga mmene munthu asungira chuma mʼphukusi, koma moyo wa adani anu adzawutaya kutali monga momwe munthu amaponyera mwala ndi legeni. 30Yehova adzakuchitirani mbuye wanga zabwino zonse zimene anakulonjezani. Adzakuyikani kukhala wolamulira Aisraeli. 31Zikadzatero, inu mbuye wanga simudzakhala ndi chikumbumtima choti munakhetsa magazi kapena kulipsira popanda chifukwa. Koma Yehova akadzakuchitirani zabwino zonsezi musadzandiyiwale ine mdzakazi wanu.”

32Tsono Davide anawuza Abigayeli kuti, “Alemekezeke Yehova Mulungu wa Israeli, amene wakutuma iwe lero kuti ukumane nane. 33Yehova akudalitseni chifukwa cha nzeru zanu pondiletsa lero kuti ndisakhetse magazi ndi kubwezera adani anga ndi manja anga. 34Kunena zoona, pali Yehova Wamoyo, Mulungu wa Israeli, amene wandiletsa kuti ndisakupwetekeni, mukanapanda kubwera msanga kudzakumana nane, palibe munthu aliyense wamwamuna wa Nabala akanasiyidwa wamoyo pakucha mmawa.”

35Ndipo Davide analandira kwa mayiyo zimene anamutengera ndipo anati, “Pitani kwanu mu mtendere. Ine ndamva mawu anu ndipo ndavomera zimene mwapempha.”

36Abigayeli atabwerera kwa Nabala anamupeza ali mʼnyumba akuchita mphwando ngati la mfumu. Iye anali atakondwa kwambiri popeza anali ataledzera kwambiri. Choncho mkazi wakeyo sanamuwuze kalikonse mpaka mmawa kutacha. 37Tsono mmawa, mowa utamuchoka Nabala, mkazi wake anamuwuza zonse. Pomwepo mtima wake unaleka kugunda ndipo unawuma gwaa ngati mwala. 38Patapita masiku khumi, Yehova anakantha Nabala ndipo anafa.

39Pamene Davide anamva kuti Nabala wamwalira, iye anati, “Alemekezeke Yehova, walipsira Nabala chipongwe chimene anandichita ndipo anandiletsa ine mtumiki wake kuti ndisachite choyipa. Yehova wabwezera pamutu pa Nabala choyipa chimene iye anachita.”

Kenaka Davide anatumiza mawu kwa Abigayeli, kumupempha kuti akhale mkazi wake. 40Anyamata a Davide atafika ku Karimeli anawuza Abigayeli kuti, “Davide watituma kwa iwe kuti tikutenge ukhale mkazi wake.”

41Abigayeli anagwada nagunditsa nkhope yake pansi ndipo anati, “Ine mdzakazi wa mbuye wanga ndakonzeka kutumikira ngakhale kusambitsa mapazi a anyamata ake.” 42Motero Abigayeli ananyamuka mofulumira nakwera bulu wake. Tsono iye pamodzi ndi anamwali ake asanu amene ankamutumikira, anatsagana ndi amithenga a Davide aja ndipo anakakhala mkazi wake wa Davide. 43Davide nʼkuti atakwatiranso Ahinoamu wa ku Yezireeli ndipo onse awiri anali akazi ake. 44Koma Sauli anali atakwatitsa Mikala, mkazi wa Davide kwa Paliti mwana wa Laisi wa ku Galimu.

New Russian Translation

1 Царств 25:1-44

Навал отказывает просьбе Давида

1Самуил умер, и все израильтяне собрались и оплакивали его. Они похоронили его рядом с его домом, в Раме. А Давид спустился в пустыню Паран.

2Один человек в городе Маоне, который владел имуществом в Кармиле, был очень богат. У него была тысяча коз и три тысячи овец, которых он стриг в Кармиле. 3Его звали Навал, а его жену – Авигайль. Она была умной и красивой женщиной, но ее муж, из рода Халева, был человек грубый и злонравный.

4Находясь в пустыне, Давид услышал, что у Навала стрижка овец. 5Он послал десять юношей и сказал им:

– Поднимитесь к Навалу в Кармил и приветствуйте его от моего имени. 6Скажите ему: «Мир тебе! Мир всему твоему дому! Мир всему, что у тебя есть! 7Я слышал, у тебя идет стрижка овец. Когда твои пастухи были с нами, мы не обижали их, и все время, что они были в Кармиле, ничего у них не пропадало. 8Спроси об этом своих слуг, и они скажут тебе. Поэтому пусть мои молодые люди найдут у тебя расположение, ведь мы пришли в праздничный день. Пожалуйста, дай твоим слугам и твоему сыну Давиду все, что сможешь для них найти».

9Когда посланцы Давида пришли, они передали Навалу от имени Давида все эти слова и стали ждать. 10Но Навал ответил слугам Давида:

– Кто такой этот Давид? Кто такой этот сын Иессея? Теперь много стало таких слуг, что бегут от своих господ. 11Неужели я возьму хлеб, воду и мясо, приготовленное для моих стригалей, и отдам людям, которые явились неизвестно откуда?

12Люди Давида повернулись и пошли назад. Возвратившись, они пересказали ему каждое слово. 13Давид приказал своим людям:

– Препояшьте свои мечи!

Они опоясались мечами, и сам Давид опоясался своим. Около четырехсот человек пошло вслед за Давидом, а двести человек осталось при обозе.

Авигайль предотвращает кровопролитие

14Один из слуг сказал жене Навала Авигайль:

– Давид послал вестников из пустыни, чтобы приветствовать нашего господина, но он их оскорбил. 15А эти люди были с нами очень добры. Они не обижали нас, и все то время, что мы были рядом с ними в полях, ничего у нас не пропадало. 16Ночью и днем они были нам стеной все время, пока мы пасли наших овец рядом с ними. 17Подумай же об этом и посмотри, что ты можешь сделать, потому что над нашим господином и над всем его домом нависла беда. Он такой злобный человек, что никто не может с ним говорить.

18Авигайль не стала терять времени. Она взяла двести лепешек, два бурдюка с вином, пять приготовленных овец, пять мер жареного зерна, сто связок изюма, двести связок сушеного инжира и нагрузила все это на ослов. 19Она сказала своим слугам:

– Ступайте вперед, а я пойду за вами.

Но своему мужу Навалу она не сказала ничего. 20Когда она спустилась на осле в горное ущелье, навстречу ей шел Давид со своими людьми, и она встретилась с ними. 21Давид только что сказал:

– Да, напрасно я охранял собственность этого человека в пустыне, чтобы ничего не пропало. Он отплатил мне злом за добро. 22Пусть Бог сурово накажет Давида25:22 Так в одном из древних переводов; в нормативном еврейском тексте: «врагов Давида»., если к утру я оставлю в живых хотя бы одного мужчину из всех, кто принадлежит Навалу!

23Увидев Давида, Авигайль быстро слезла с осла и поклонилась перед Давидом до земли. 24Она пала к его ногам и сказала:

– Мой господин, пусть вина будет на мне одной. Пожалуйста, позволь твоей служанке поговорить с тобой; выслушай то, что твоя служанка тебе скажет. 25Пусть мой господин не обращает внимания на этого негодного человека Навала. Он таков, каково его имя, – его зовут Глупец25:25 Навал – по-еврейски это имя означает «глупец»., и глупость его с ним. Что же до меня, твоей служанки, то я не видела людей, которых присылал мой господин.

26А теперь, так как Господь удержал моего господина от кровопролития и от того, чтобы мстить за себя своими руками, то верно, как и то, что Господь жив и жив ты сам, пусть твои враги и все, кто замышляет зло против моего господина, будут подобны Навалу. 27И пусть этот дар, который принесла моему господину твоя служанка, будет вручен людям, что следуют за тобой. 28Пожалуйста, прости вину твоей служанки, ведь Господь непременно создаст для моего господина прочный дом, потому что мой господин ведет войны Господа. Пусть не будет в тебе никакого зла всю твою жизнь. 29Даже если кто-нибудь станет преследовать тебя, чтобы отнять у тебя жизнь, то жизнь моего господина будет надежно завязана в узле жизни у Господа, твоего Бога. Но жизни твоих врагов Он метнет прочь, словно камень из пращи. 30Когда Господь совершит для моего господина все доброе, что Он говорил о тебе, и поставит тебя вождем над Израилем, 31у моего господина не будет повода горевать или терзаться муками совести о том, что пролил напрасно кровь и отомстил за себя. И когда Господь даст моему господину успех, вспомни твою служанку.

32Давид сказал Авигайль:

– Благословен Господь, Бог Израиля, Который послал тебя сегодня мне навстречу! 33Благословен твой разум, и благословенна ты за то, что удержала меня от кровопролития и от мести за себя. 34Иначе, верно, как и то, что жив Господь, Бог Израиля, Который удержал меня от того, чтобы причинить тебе вред, – если бы ты не поспешила мне навстречу, ни один из мужчин в доме Навала не остался бы в живых к рассвету.

35Затем Давид принял из ее рук то, что она ему принесла, и сказал:

– Ступай домой с миром. Я послушаюсь твоих слов и исполню твою просьбу.

Авигайль становится женой Давида

36Когда Авигайль пришла к Навалу, он был дома и сидел на пиру, подобном царскому. Он был весел и сильно пьян. Она ничего не говорила ему до рассвета. 37Утром, когда Навал протрезвел, жена рассказала ему обо всем. Его сердце замерло, и он будто окаменел. 38Спустя примерно десять дней Господь поразил Навала, и он умер. 39Когда Давид услышал, что Навал умер, он сказал:

– Благословен Господь, Который отомстил за оскорбление, полученное мной от Навала. Он удержал Своего слугу от злого дела и обратил злобу Навала на его же голову.

Затем Давид послал Авигайль известие, прося ее стать его женой. 40Его слуги пришли в Кармил и сказали Авигайль:

– Давид послал нас к тебе, чтобы взять тебя ему в жены.

41Она поклонилась лицом до земли и сказала:

– Вот твоя служанка, готовая служить тебе и мыть ноги слугам моего господина.

42Авигайль быстро села на осла и в сопровождении пяти своих служанок отправилась с посланниками Давида к нему и стала его женой. 43Еще Давид женился на Ахиноамь из Изрееля, и они обе были его женами. 44Но Саул отдал свою дочь Михаль, жену Давида, Фалтию, сыну Лаиша из Галлима.