1 Samueli 24 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 24:1-22

Davide Amusiya Sauli Wosamupha

1Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.” 2Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.

3Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo. 4Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’ ” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.

5Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli. 6Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.” 7Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.

8Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi. 9Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’ 10Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’ 11Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe. 12Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani. 13Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.

14“Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi? 15Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”

16Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza. 17Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa. 18Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe. 19Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi. 20Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako. 21Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”

22Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.

New Russian Translation

1 Царств 24:1-23

Давид щадит жизнь Саула

1Давид поднялся оттуда и остался жить в неприступных местах Эн-Геди.

2Когда Саул вернулся из погони за филистимлянами, ему сказали:

– Давид в пустыне Эн-Геди.

3Саул взял три тысячи лучших воинов со всего Израиля и отправился искать Давида и его людей к Скалам Диких Коз. 4Он пришел к овечьим загонам у дороги. Там была пещера, и Саул зашел в нее облегчиться. А Давид и его люди сидели в глубине пещеры. 5Люди Давида сказали ему:

– Вот он, тот день, о котором Господь говорил тебе: «Я отдам врага в твои руки, чтобы ты поступил с ним так, как тебе угодно».

Давид тихонько подкрался и отрезал край у верхней одежды Саула. 6После этого Давида стала мучить совесть за то, что он отрезал край верхней одежды Саула.

7Он сказал своим людям:

– Не приведи Господь мне сделать такое моему господину, помазаннику Господню, или поднять на него руку, ведь он – помазанник Господень.

8Этими словами упрекнул Давид своих людей и не позволил им напасть на Саула. А Саул вышел из пещеры и отправился своей дорогой. 9Потом и Давид вышел из пещеры и закричал вслед Саулу:

– Господин мой, царь!

Когда Саул оглянулся, Давид поклонился ему лицом до земли. 10Он сказал Саулу:

– Зачем ты слушаешь, когда люди говорят: «Давид замышляет причинить тебе зло?» 11Сегодня ты своими глазами видел, как Господь отдал тебя в мои руки в пещере. Меня уговаривали убить тебя, но я пощадил тебя, сказав: «Я не подниму руки на моего господина, потому что он – помазанник Господа». 12Вот, отец мой, посмотри на кусок твоей верхней одежды у меня в руке! Я отрезал край твоей одежды, но не убил тебя. Пойми же и признай, что я не виновен ни в злодеянии, ни в мятеже. Я не согрешил против тебя, но ты охотишься за мной, чтобы лишить меня жизни. 13Пусть Господь рассудит нас! И пусть Господь отомстит тебе за меня: моя рука тебя не коснется. 14Как говорится в старой пословице: «От злодеев исходят злые дела», – поэтому моя рука тебя не коснется.

15Против кого вышел царь Израиля? Кого ты преследуешь? Мертвого пса! Блоху! 16Пусть Господь будет нашим судьей и рассудит нас. Пусть Он рассмотрит мое дело и защитит его. Пусть Он оправдает меня, избавив от твоей руки.

17Когда Давид сказал это, Саул спросил:

– Это твой голос, Давид, сын мой? – и громко заплакал.

18– Ты праведнее меня, – сказал он. – Ты поступил со мной хорошо, а я обходился с тобой плохо. 19Ты только что рассказал мне, как по-доброму ты обошелся со мной: Господь отдал меня в твои руки, но ты не убил меня. 20Кто, найдя своего врага, позволит ему уйти невредимым? Пусть Господь воздаст тебе добром за то, что ты сегодня сделал для меня. 21Я знаю, что ты непременно будешь царем, и что царство Израиля установится в твоих руках. 22Поклянись же мне Господом, что ты не искоренишь моих потомков после меня и не уничтожишь моего имени из семьи моего отца.

23Давид поклялся Саулу. После этого Саул вернулся домой, а Давид и его люди поднялись в укрепление.