1 Samueli 19 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 19:1-24

Sauli Ayesanso Kupha Davide

1Sauli anawuza mwana wake Yonatani ndi nduna zake zonse kuti aphe Davide. Koma Yonatani amamukonda kwambiri Davide. 2Choncho anawuza Davide kuti, “Abambo anga Sauli akufuna kukupha. Tsono uchenjere. Mmawa upite ukabisale ndipo ukakhale komweko. 3Ine ndidzapita ndi kukayima pafupi ndi abambo anga ku munda kumene iwe ukabisale. Ndipo ndidzayankhula ndi abambo anga za iwe ndipo chilichonse chimene ndikamve ndidzakuwuza.”

4Tsono Yonatani anakanena zabwino za Davide kwa abambo ake Sauli ndipo anati, “Mfumu musachimwire mtumiki wanu Davide, sanakuchimwireni, koma amakuchitirani zabwino kwambiri. 5Iye anayika moyo wake pa chiswe pamene anapha Mfilisiti uja. Choncho Yehova anachita zazikulu popambanitsa Aisraeli pa nkhondo. Inu munaona zonsezo ndipo munakondwera. Nanga nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwira munthu wosalakwa pofuna kupha Davide?”

6Sauli anamvera mawu a Yonatani ndipo analumbira kuti, “Pali Yehova, Davide sadzaphedwa.”

7Pambuyo pake Yonatani anayitana Davide namuwuza zonsezi. Choncho Yonatani anabwera naye Davide kwa Sauli ndipo ankamutumikira Sauliyo monga kale.

8Panabukanso nkhondo ina ndipo Davide anapita ndi kukamenyana ndi Afilisti. Iye anawakantha mwamphamvu kotero kuti Afilisti anathawa.

9Tsiku lina mzimu woyipa uja unafikanso pa Sauli. Nthawi imeneyi nʼkuti Sauli uja ali mʼnyumba mwake, mkondo uli mʼdzanja lake ndi Davide akuyimba zeze, 10Sauli anafuna kumubaya Davide ndi kumukhomera kukhoma, koma Davide anapewa mkondowo kotero Sauli anakabaya pa khoma. Usiku womwewo Davide anathawa.

11Usiku womwewo Sauli anatumiza anthu ku nyumba ya Davide kuti akamubisalire ndi kumupha mmamawa. Koma Mikala mkazi wake anamuchenjeza nati, “Ngati usiku uno supulumutsa moyo wako, mawa udzaphedwa.” 12Choncho Mikala anamutulutsira Davide pa zenera, ndipo anathawa ndi kupulumuka. 13Kenaka Mikala anatenga fano naligoneka pa bedi nayika pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwa fanolo ndipo analifunditsa nsalu.

14Pamene amithenga a Sauli aja anafika kuti akamugwire Davide, Mikala anati, “Davide akudwala.”

15Koma Sauli anatumanso anthuwo kuti akamuone Davide, nati, “Mubwere naye kuno ali pa bedi pomwepo kuti ndidzamuphe.” 16Koma pamene anthuwo analowa, anangoona fano pa bedipo ndi pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwake.

17Tsono Sauli anafunsa Mikala kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandinamiza chotere polola kuti mdani wanga athawe?”

Mikala anayankha kuti, “Davide anandiwuza kuti, ‘Ukapanda kutero ndikupha.’ ”

18Choncho Davide anathawa napulumuka. Pambuyo pake anapita kwa Samueli ku Rama nakamuwuza zonse zimene Sauli anamuchita. Kenaka iye ndi Samueli anapita kukakhala ku Nayoti. 19Sauli anamva kuti, “Davide ali ku Nayoti ku Rama.” 20Choncho iye anatumiza anthu kuti akamugwire Davide. Koma anaona gulu la aneneri likulosera ndi Samueli akuwatsogolera. Pomwepo Mzimu wa Mulungu unawafikira ndipo nawonso anayamba kulosera. 21Sauli atamva zimenezi anatumizanso anthu ena, koma nawonso anayamba kulosa. Anatumanso anthu ena kachitatu, koma nawonso anayamba kulosa. 22Pomaliza Sauli mwini wake ananyamuka kupita ku Rama ndipo anafika ku chitsime chachikulu cha ku Seku. Ndipo anafunsa, “Samueli ndi Davide ali kuti?”

Munthu wina anamuyankha kuti, “Ali ku Nayoti ku Rama.”

23Choncho Sauli anapita ku Nayoti ku Rama. Koma Mzimu wa Mulungu unafikanso pa iye ndipo ankalosa akuyenda mpaka anafika ku Nayoti. 24Nayenso anavula zovala zake nayamba kulosa pamaso pa Samueli. Kenaka anagona wamaliseche tsiku lonse ndi usiku wonse. Nʼchifukwa chake anthu amati, “Kodi Sauli alinso mmodzi wa aneneri?”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

撒母耳记上 19:1-24

扫罗试图杀大卫

1扫罗吩咐他儿子约拿单和众臣仆去杀掉大卫。但约拿单非常喜爱大卫2便告诉他,说:“我父亲要杀你,明天早上你要小心,找个僻静的地方躲起来。 3我会出去和父亲站在你藏身的田间,跟他提你的事,然后把消息告诉你。” 4约拿单就在父亲面前替大卫说好话,他说:“王不要伤害大卫,他从来没有对不起王,他所做的使王大受益处。 5他冒着生命危险去杀非利士人,耶和华使以色列人大获全胜,当时你看见了,非常欢喜,现在为什么要犯罪,枉杀无辜的大卫呢?” 6扫罗听了约拿单的话,就凭永活的耶和华起誓说:“我不杀大卫。” 7约拿单叫来大卫,把经过告诉他,带他去见扫罗大卫又像以前一样伺候扫罗

8后来,战事再度爆发,大卫领兵与非利士人交战,大败敌人,杀得他们四散溃逃。 9一天,扫罗手里拿着矛正坐在家中,从耶和华那里来的邪灵降临在扫罗身上。大卫正在弹琴, 10扫罗想用矛把大卫刺透,钉在墙上,大卫躲开了,矛插在了墙上。大卫当晚逃走了。

11扫罗派人监视大卫的家,要在早上杀死他。大卫的妻子米甲警告他说:“如果你今晚不逃命,明早必死无疑。” 12于是,她从窗口把大卫缒下去,让他逃走了。 13然后她把家中的神像放在床上,头枕在山羊毛的枕头上,盖上被子。 14扫罗派人来捉拿大卫的时候,米甲说他病了。 15扫罗又派人去见大卫,并吩咐说:“把他连床一起抬来,我好杀他。” 16众人进去发现躺在床上的是一个神像,头枕在山羊毛的枕头上。 17扫罗米甲:“你为什么欺骗我,让我的敌人逃走?”米甲答道:“他说如果我不让他逃走,就杀了我。”

18大卫逃到住在拉玛撒母耳那里,把扫罗的所作所为告诉他。后来,他和撒母耳拿约住了下来。 19扫罗听说大卫拉玛拿约20就派人去捉拿他。扫罗的人看到一群先知在说预言,撒母耳在当中带领他们。上帝的灵也临到扫罗的人,他们也说起预言来。 21扫罗听说后又派人去,派去的人也说起预言来。扫罗第三次派人去,派去的人同样说起预言来。 22最后扫罗亲自前往拉玛,走到西沽的大井,问撒母耳大卫在哪里,有人说在拉玛拿约23扫罗便去拉玛拿约。上帝的灵临到扫罗,他就一边走一边说起预言来,一直到拉玛拿约24他脱下自己的衣服,在撒母耳面前说起预言来。他赤身躺了一天一夜。因此有句俗语说:“扫罗也在先知当中吗?”