1 Samueli 19 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 19:1-24

Sauli Ayesanso Kupha Davide

1Sauli anawuza mwana wake Yonatani ndi nduna zake zonse kuti aphe Davide. Koma Yonatani amamukonda kwambiri Davide. 2Choncho anawuza Davide kuti, “Abambo anga Sauli akufuna kukupha. Tsono uchenjere. Mmawa upite ukabisale ndipo ukakhale komweko. 3Ine ndidzapita ndi kukayima pafupi ndi abambo anga ku munda kumene iwe ukabisale. Ndipo ndidzayankhula ndi abambo anga za iwe ndipo chilichonse chimene ndikamve ndidzakuwuza.”

4Tsono Yonatani anakanena zabwino za Davide kwa abambo ake Sauli ndipo anati, “Mfumu musachimwire mtumiki wanu Davide, sanakuchimwireni, koma amakuchitirani zabwino kwambiri. 5Iye anayika moyo wake pa chiswe pamene anapha Mfilisiti uja. Choncho Yehova anachita zazikulu popambanitsa Aisraeli pa nkhondo. Inu munaona zonsezo ndipo munakondwera. Nanga nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwira munthu wosalakwa pofuna kupha Davide?”

6Sauli anamvera mawu a Yonatani ndipo analumbira kuti, “Pali Yehova, Davide sadzaphedwa.”

7Pambuyo pake Yonatani anayitana Davide namuwuza zonsezi. Choncho Yonatani anabwera naye Davide kwa Sauli ndipo ankamutumikira Sauliyo monga kale.

8Panabukanso nkhondo ina ndipo Davide anapita ndi kukamenyana ndi Afilisti. Iye anawakantha mwamphamvu kotero kuti Afilisti anathawa.

9Tsiku lina mzimu woyipa uja unafikanso pa Sauli. Nthawi imeneyi nʼkuti Sauli uja ali mʼnyumba mwake, mkondo uli mʼdzanja lake ndi Davide akuyimba zeze, 10Sauli anafuna kumubaya Davide ndi kumukhomera kukhoma, koma Davide anapewa mkondowo kotero Sauli anakabaya pa khoma. Usiku womwewo Davide anathawa.

11Usiku womwewo Sauli anatumiza anthu ku nyumba ya Davide kuti akamubisalire ndi kumupha mmamawa. Koma Mikala mkazi wake anamuchenjeza nati, “Ngati usiku uno supulumutsa moyo wako, mawa udzaphedwa.” 12Choncho Mikala anamutulutsira Davide pa zenera, ndipo anathawa ndi kupulumuka. 13Kenaka Mikala anatenga fano naligoneka pa bedi nayika pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwa fanolo ndipo analifunditsa nsalu.

14Pamene amithenga a Sauli aja anafika kuti akamugwire Davide, Mikala anati, “Davide akudwala.”

15Koma Sauli anatumanso anthuwo kuti akamuone Davide, nati, “Mubwere naye kuno ali pa bedi pomwepo kuti ndidzamuphe.” 16Koma pamene anthuwo analowa, anangoona fano pa bedipo ndi pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwake.

17Tsono Sauli anafunsa Mikala kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandinamiza chotere polola kuti mdani wanga athawe?”

Mikala anayankha kuti, “Davide anandiwuza kuti, ‘Ukapanda kutero ndikupha.’ ”

18Choncho Davide anathawa napulumuka. Pambuyo pake anapita kwa Samueli ku Rama nakamuwuza zonse zimene Sauli anamuchita. Kenaka iye ndi Samueli anapita kukakhala ku Nayoti. 19Sauli anamva kuti, “Davide ali ku Nayoti ku Rama.” 20Choncho iye anatumiza anthu kuti akamugwire Davide. Koma anaona gulu la aneneri likulosera ndi Samueli akuwatsogolera. Pomwepo Mzimu wa Mulungu unawafikira ndipo nawonso anayamba kulosera. 21Sauli atamva zimenezi anatumizanso anthu ena, koma nawonso anayamba kulosa. Anatumanso anthu ena kachitatu, koma nawonso anayamba kulosa. 22Pomaliza Sauli mwini wake ananyamuka kupita ku Rama ndipo anafika ku chitsime chachikulu cha ku Seku. Ndipo anafunsa, “Samueli ndi Davide ali kuti?”

Munthu wina anamuyankha kuti, “Ali ku Nayoti ku Rama.”

23Choncho Sauli anapita ku Nayoti ku Rama. Koma Mzimu wa Mulungu unafikanso pa iye ndipo ankalosa akuyenda mpaka anafika ku Nayoti. 24Nayenso anavula zovala zake nayamba kulosa pamaso pa Samueli. Kenaka anagona wamaliseche tsiku lonse ndi usiku wonse. Nʼchifukwa chake anthu amati, “Kodi Sauli alinso mmodzi wa aneneri?”

Священное Писание

1 Царств 19:1-24

Ионафан предупреждает Давуда

1Шаул повелел своему сыну Ионафану и всем слугам убить Давуда. Но Ионафан был очень привязан к Давуду 2и предупредил его:

– Мой отец Шаул ищет возможности убить тебя. Завтра утром берегись, спрячься в укрытии и оставайся там. 3Я выйду в поле и встану рядом с отцом там, где будешь ты. Я буду говорить с ним о тебе и перескажу тебе всё, что узнаю.

4Ионафан говорил своему отцу Шаулу о Давуде только хорошее:

– Пусть царь не грешит против своего раба Давуда, потому что Давуд не согрешил против тебя и потому что своими делами он сослужил тебе большую службу. 5Он рисковал жизнью, когда вышел против филистимлянина Голиафа. Вечный одержал для всего Исраила великую победу, и ты радовался, видя это. Зачем тебе грешить против невиновного человека, убив Давуда без всякой причины?

6Шаул послушался Ионафана и дал клятву:

– Верно, как и то, что жив Вечный, – Давуд не будет предан смерти.

7Ионафан позвал Давуда и передал ему весь разговор. Он привёл его к Шаулу, и Давуд остался у Шаула, как и прежде.

Побег Давуда

8Опять началась война, и Давуд вышел сражаться с филистимлянами. Он нанёс им такое поражение, что они бежали от него.

9Злой дух от Вечного напал на Шаула, когда тот сидел у себя дома с копьём в руках, а Давуд в это время играл на арфе. 10Шаул попытался пригвоздить Давуда к стене своим копьём, но Давуд увернулся от него, и копьё вонзилось в стену. В ту ночь Давуд убежал и спасся. 11А Шаул послал людей в дом Давуда, чтобы выследить и убить его утром. Но Михаль, жена Давуда, предупредила его:

– Если сегодня вечером ты не спасёшься бегством, завтра тебя убьют.

12Михаль помогла Давуду спуститься через окно, и он убежал и спасся. 13Тогда Михаль взяла истукан, положила его на кровать, накрыла ему голову покрывалом из козьей шерсти и закутала его одеждой.

14Когда Шаул прислал людей, чтобы схватить Давуда, Михаль сказала:

– Он болен.

15Тогда Шаул послал людей посмотреть на Давуда и сказал им:

– Принесите его ко мне прямо на постели, чтобы я убил его.

16Но когда те пришли, они обнаружили в постели истукан, а на голове у него – покрывало из козьей шерсти.

17Шаул сказал Михаль:

– Зачем ты обманула меня и отпустила моего врага, чтобы он спасся?

Михаль ответила ему:

– Он сказал мне: «Отпусти меня, или я убью тебя».

Шаул у пророков в Раме

18Когда Давуд убежал и спасся, он пришёл к Шемуилу в Раму и рассказал ему всё, что сделал Шаул. После этого они с Шемуилом ушли в Найот и оставались там. 19Шаула известили: «Давуд в Найоте, в Раме», 20и он послал людей, чтобы схватить его. Но когда они увидели группу пророков, которые пророчествовали19:20 Слово, стоящее здесь в тексте оригинала, можно понять как прорицание, но, скорее всего, в этом месте говорится о прославлении Всевышнего в состоянии особого эмоционального возбуждения., и Шемуила, который возглавлял их, Дух Всевышнего сошёл на людей Шаула, и они также стали пророчествовать. 21Шаулу сказали об этом, и он послал ещё людей, но и они также стали пророчествовать. Шаул послал людей в третий раз, но и те стали пророчествовать. 22Наконец, он сам отправился в Раму и пришёл к огромному колодцу в Секу. Он спросил:

– Где Шемуил и Давуд?

– Они в Найоте, в Раме, – ответил ему кто-то.

23Шаул пошёл в Найот в Раме. Но Дух Всевышнего сошёл и на него, и он шёл, пророчествуя, пока не пришёл в Найот. 24Он снял одежду и также стал пророчествовать перед Шемуилом. Он лежал обнажённым весь день и всю ночь. Вот почему люди говорят: «Разве и Шаул среди пророков?»