1 Samueli 17 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 17:1-58

Davide ndi Goliati

1Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo ku Soko mʼdziko la Yuda. Iwo anamanga misasa yawo ku Efesi-Damimu, pakati pa Soko ndi Azeka. 2Sauli ndi Aisraeli anasonkhana namanga misasa mʼchigwa cha Ela ndipo anandandalitsa ankhondo kuti amenyane ndi Afilisti. 3Afilisti anali phiri lina ndipo Aisraeli analinso phiri lina, ndipo pakati pawo panali chigwa.

4Tsono munthu wina wamphamvu, dzina lake Goliati wochokera ku Gati anatuluka ku misasa ya Afilisti. Msinkhu wake unali pafupipafupi mamita atatu. 5Iye ankavala chipewa chamkuwa ndi malaya achitsulo olemera makilogalamu 57. 6Ankavalanso zokuta miyendo yake zamkuwa, ndipo ankanyamula nthungo ya mkuwa pa phewa pake. 7Thunthu la mkondo wake linali ngati mkombero wowombera nsalu, ndipo mutu wa mkondowo unkalemera makilogalamu asanu ndi awiri. Patsogolo pake pamakhala munthu wonyamula zida zake za nkhondo.

8Goliatiyo anayimirira ndi kufuwula kwa ankhondo a Israeli, nati, “Nʼchifukwa chiyani mwakonzekera nkhondo chotere? Kodi sindine Mfilisiti ndipo inu sindinu akapolo a Sauli? Sankhani munthu kuti abwere kwa ine. 9Ngati angathe kumenyana nane ndi kundipha, ife tidzakhala akapolo anu, koma ngati ine ndimugonjetsa ndi kumupha, inu mudzakhala akapolo athu ndi kumatitumikira.” 10Ndipo Mfilisitiyo anati, “Bwerani lero timenyane basi! Patseni munthu kuti ndimenyane naye.” 11Atamva mawu a Mfilisitiyo, Sauli ndi Aisraeli onse anataya mtima nachita mantha kwambiri.

12Davide anali mwana wa munthu wa fuko la Efurati dzina lake Yese amene amachokera ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Yese anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri. Pa nthawi ya Sauli nʼkuti ali wokalamba. 13Ana atatu oyamba kubadwa a Yese nʼkuti atapita nawo ku nkhondo pamodzi ndi Sauli. Woyamba dzina lake anali Eliabu, wachiwiri anali Abinadabu, ndipo wachitatu anali Sama. 14Davide ndiye anali mzime. Ana aakulu atatuwo ndiwo anapita ku nkhondo ndi Sauli. 15Koma Davide ankapita ku misasa ya Sauli ndi kubwerako kuti azikaweta nkhosa za abambo ake ku Betelehemu.

16Kwa masiku makumi anayi, Mfilisiti uja ankabwera mmawa ndi madzulo kumadzionetsera.

17Tsiku lina Yese anawuza mwana wake Davide kuti, “Atengere abale ako makilogalamu khumi a tirigu wokazinga ndi malofu a buledi khumi ndipo upite nazo mofulumira ku misasa yawo. 18Utengerenso wolamulira wa gulu lawo tchizi khumi uyu. Ukaone mmene abale ako akukhalira ndipo ubwere ndi kanthu kosonyeza kuti ali bwino. 19Sauli, abale akowo ndi asilikali onse a Israeli ali ku chigwa cha Ela, akumenyana ndi Afilisti.”

20Mʼmamawa mwake Davide anasiya nkhosa mʼmanja mwa munthu wina ndipo anatenga zakudyazo nanyamuka monga momwe Yese abambo ake anamulamulira. Anakafika ku misasa pamene asilikali ankapita kukandanda pa mzere ku nkhondo, nʼkufuwula mfuwu wankhondo. 21Aisraeli ndi Afilisti anandanda pa mzere wankhondo moyangʼanana. 22Tsono Davide anasiyira zakudya zija munthu wosunga katundu nathamangira kumene kunali ankhondo kuja ndi kukalonjera abale ake. 23Pamene iye ankayankhula nawo anangoona Goliati wa ku Gati uja akuchoka pa mzere wa Afilisti akufuwula mawu onyoza monga mwa masiku onse, ndipo Davide ankawamva. 24Aisraeli ataona munthuyo, anamuthawa ndi mantha aakulu.

25Ndipo Aisraeli ankanena kuti, “Kodi mwamuona munthu akubwerayo? Iye amangobwera kudzanyoza Israeli. Tsono mfumu inati kuti idzapereka chuma chambiri kwa munthu amene adzamuphe. Idzaperekanso mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndiponso banja la abambo ake silidzaperekanso msonkho mu Israeli.”

26Davide anafunsa anthu amene anayima pafupi naye kuti, “Kodi adzamuchita chiyani munthu amene adzapha Mfilisiti uyu ndi kuchotsa chitonzo pakati pa Israeli? Mfilisiti wosachita mdulidweyu ndi ndani kuti azinyoza gulu lankhondo la Mulungu wamoyo?”

27Anthu anamuwuzanso zonse zimene mfumu inanena kuti idzachitira munthu amene adzapha Mfilisitiyo.

28Eliabu, mkulu wake wa Davide, atamumva akuyankhula ndi anthuwo, anamukwiyira ndipo anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabwera kuno? Ndipo wasiyira yani nkhosa zochepazo mʼchipululu? Ndikudziwa kuti ndiwe wodzikuza ndiponso woyipa mtima. Unabwera kuno kuti udzaonere nkhondo.”

29Davide anati, “Kodi ndachita chiyani ine? Kodi ndisamayankhule?” 30Ndipo anamuchokera napita kwa munthu wina ndipo anamufunsa nkhani yomweyo, ndipo anthu anamuyankha iye monga poyamba paja. 31Mawu amene Davide anayankhula atamveka, anthu anakafotokozera Sauli ndipo Sauli anamuyitanitsa.

32Davide anati kwa Sauli, “Munthu aliyense asataye mtima chifukwa cha Mfilisitiyu. Ine kapolo wanu ndipita kukamenyana naye.”

33Sauli anayankha Davide kuti, “Iwe sungathe kupita kukamenyana ndi Mfilisitiyu. Iwe ukanali mnyamata, koma iyeyu ndi amene wakhala akumenya nkhondo kuyambira unyamata wake.”

34Koma Davide anati kwa Sauli, “Kapolo wanune ndinkaweta nkhosa za abambo anga. Ndipo mkango kapena chimbalangondo chikamabwera ndi kugwira mwana wankhosa pakati pa nkhosazo, 35ine ndinkatsatira ndi kupha chirombocho. Choncho ndinkapulumutsa mwana wankhosa uja mʼkamwa mwake. Ndipo chinkati chikandiwukira, ine ndinkagwira tchowa lake, nʼkuchikantha mpaka kuchipha. 36Ine kapolo wanu ndinapha mkango ngakhalenso chimbalangondo. Tsono Mfilisiti wosachita mdulidweyu adzaphedwa monga zinazo chifukwa wanyoza ankhondo a Mulungu wamoyo. 37Yehova amene anandilanditsa mʼkamwa mwa mkango ndi chimbalangondo adzandilanditsa mʼmanja mwa Mfilisiti uyu.”

Sauli anati kwa Davide, “Pita, ndipo Yehova akhale nawe.”

38Ndipo Sauli anamveka Davide mwinjiro wake. Anamuveka zovala zankhondo ndi chipewa cha mkuwa. 39Davide anamangirira lupanga pa mwinjirowo. Atayesa kuyenda nazo, analephera chifukwa anali asanazizolowere.

Iye anati kwa Sauli, “Sindingathe kuyenda nazo chifukwa sindinazizolowere.” Ndipo anazivula. 40Pambuyo pake anatenga ndodo yake mʼmanja. Kenaka anasankha miyala yosalala bwino mu mtsinje ndi kuyiika mʼthumba lake la ku ubusa. Legeni ili mʼmanja mwake, Davide ananyamuka kukakumana ndi Mfilisiti uja.

41Tsono Mfilisiti uja anayambapo kupita kumene kunali Davide, mnyamata wonyamula zida zake za nkhondo ali patsogolo pake. 42Mfilisitiyo atangomuona Davide, anamunyoza popeza kuti Davide anali mnyamata chabe wofiirira ndi wa maonekedwe abwino. 43Iye anati kwa Davide, “Kodi ndine galu, kuti ubwere kwa ine ndi ndodo?” Ndipo Mfilisitiyo anamutemberera Davide potchula mayina a milungu yake. 44Iye anatinso, “Bwera kuno ndipo ndidzapereka mnofu wako kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa zirombo zakuthengo!”

45Koma Davide anati kwa Mfilisitiyo, “Iwe wabwera kwa ine ndi lupanga, mkondo ndi nthungo, koma ine ndikubwera kwa iwe mʼdzina la Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa ankhondo Aisraeli amene iwe ukuwanyoza. 46Anatinso lero lino Yehova adzakupereka mʼmanja mwanga. Ndidzakukantha ndi kudula mutu wako. Ndidzapereka mitembo ya asilikali a Afilisti kwa mbalame za mlengalenga, ndi kwa zirombo zakuthengo ndipo dziko lonse lapansi lidzadziwa kuti mu Israeli muli Mulungu. 47Onse amene asonkhana pano adzadziwa kuti Mulungu sapulumutsa anthu ndi lupanga kapena mkondo, pakuti nkhondo ndi ya Yehova. Iye adzakuperekani mʼmanja mwathu.”

48Mfilisitiyo akusendera pafupi kuti akumane naye, Davideyo anathamangira mofulumira ku mzere wa nkhondo kukakumana naye. 49Davideyo anapisa dzanja lake mʼthumba lake natengamo mwala ndipo anawuponya, nalasa pa mphumi pa Mfilisitiyo. Mwalawo unalowa pa chipumi chake, ndipo anagwa chafufumimba.

50Kotero Davide anamupambana Mfilisitiyo pomugenda ndi mwala wa legeni ndi kumupha. Mʼmanja mwa Davide munalibe lupanga.

51Davide anathamanga nakayimirira pamwamba pa Mfilisiti uja. Anasolola lupanga lake lomwe moyikamo mwake, namupha pomudula mutu wake.

Afilisti ataona kuti ngwazi yawo yafa, anathawa. 52Ndipo Aisraeli ndi anthu a ku Yuda ananyamuka, ndipo akufuwula anathamangitsa Afilisti aja mpaka ku Gati ndi ku zipata za Ekroni. Anthu akufa awo amagwa njira yonse ya ku Saaraimu mpaka ku Gati ndi ku Ekroni. 53Aisraeli anabwerako kothamangitsa Afilisti kuja ndipo anadzatenga zonse zimene zinali mʼmisasa ya Afilistiwo. 54Pambuyo pake Davide anatenga mutu wa Mfilisitiyo napita nawo ku Yerusalemu, koma anayika zida za Mfilisitiyo mu tenti yake.

55Sauli ataona Davide akupita kukakumana ndi Mfilisitiyo anafunsa Abineri, mkulu wa ankhondo kuti, “Abineri, kodi mnyamatayu ndi mwana wa yani?”

Abineri anayankha kuti, “Ndithu mfumu muli apa ine sindikumudziwa.”

56Mfumu inati, “Pita kafufuze kuti mnyamata ameneyu ndi mwana wa yani.”

57Davide atangobwerako kokapha Mfilisiti kuja, Abineri anamutenga nabwera naye kwa Sauli, mutu wa Mfilisiti uja uli mʼmanja mwake.

58Sauli anamufunsa, “Mnyamata iwe, kodi paja ndiwe mwana wayani?”

Davide anati, “Ndine mwana wa mtumiki wanu Yese wa ku Betelehemu.”

New Russian Translation

1 Царств 17:1-58

Вызов Голиафа

1Филистимляне собрали войска для войны и пришли в поселение Сохо, что в Иудее. Они разбили лагерь в Эфес-Даммиме, между Сохо и Азекой. 2Саул и израильтяне собрались, расположились лагерем в долине Эла и выстроились против филистимлян. 3Филистимляне стояли на одном холме, а израильтяне на другом; между ними была долина.

4Из филистимского лагеря вышел борец по имени Голиаф, родом из Гата. Ростом он был шесть локтей и пядь17:4 Около трех метров.. 5На голове у него был бронзовый шлем, а сам он был одет в бронзовую кольчугу весом в пять тысяч шекелей17:5 Около 57 кг.. 6На ногах у него были бронзовые наколенники, а за спиной висел бронзовый дротик. 7Древко его копья было большое, как ткацкий навой, а железный наконечник весил шестьсот шекелей17:7 Около 7 кг.. Перед ним шел его щитоносец.

8Голиаф остановился и закричал выстроившимся израильтянам:

– Зачем вы вышли и построились на битву? Разве я не филистимлянин, а вы – не рабы Саула? Выберите человека, пусть он спустится ко мне. 9Если он сможет сразиться со мной и убить меня, мы станем вашими рабами, но если я одержу победу и убью его, вы станете нашими рабами и будете нам служить.

10Филистимлянин сказал:

– Сегодня я бросаю израильтянам вызов! Выберите человека, чтобы нам сразиться друг с другом.

11Услышав слова филистимлянина, Саул и все израильтяне пришли в смятение и сильно испугались.

Давид приходит в военный лагерь

12Давид был сыном ефрафянина по имени Иессей из Вифлеема, что в Иудее. У Иессея было восемь сыновей, и во времена Саула он достиг преклонных лет и был старший между мужчинами. 13Три старших сына Иессея пошли за Саулом на войну: первенца звали Элиав, второго сына – Авинадав, а третьего – Шамма. 14Давид был самым младшим. Три старших сына пошли за Саулом, 15а Давид ходил к Саулу и возвращался в Вифлеем, чтобы пасти овец своего отца. 16Сорок дней филистимлянин выходил каждое утро и каждый вечер и бросал свой вызов.

17Иессей сказал своему сыну Давиду:

– Возьми ефу17:17 Вероятно, около 22 кг. поджаренного зерна и десять лепешек для братьев и поспеши к ним в лагерь. 18Возьми еще десять голов сыра для тысяченачальника. Проведай братьев и принеси от них какую-нибудь весточку. 19Они вместе с Саулом и всеми его людьми в долине Эла воюют с филистимлянами.

20Рано утром Давид оставил стадо другому пастуху, взял ношу и отправился в путь, как велел Иессей. Он добрался до лагеря, когда войско с боевым кличем выходило на свои места. 21Израиль и филистимляне построились в ряды друг напротив друга. 22Давид оставил свою ношу обозному сторожу и побежал в ряды, поприветствовать братьев.

23Когда он говорил с ними, Голиаф, филистимский воин из Гата, выступил из рядов и прокричал свой обычный вызов на бой, и Давид услышал его. 24Увидев этого человека, израильтяне убегали от него в великом страхе. 25Они говорили:

– Видите, как выходит этот человек? Он выходит, чтобы бросить Израилю вызов. Царь одарит большим богатством того, кто убьет его. Еще он даст ему в жены свою дочь и освободит от налогов семью его отца в Израиле.

26Давид спросил у людей, которые стояли рядом с ним:

– Что будет тому, кто убьет этого филистимлянина и снимет позор с Израиля? Кто он такой, этот необрезанный филистимлянин, чтобы бросать вызов войскам живого Бога?

27Они повторили ему то, что говорили раньше, и сказали:

– Вот что будет тому, кто убьет его.

28Когда Элиав, старший брат Давида, услышал, как тот говорит с людьми, он разгневался на него и спросил:

– Зачем ты пришел сюда? И на кого ты оставил тех немногих овец в пустыне? Я знаю, как ты тщеславен и как порочно твое сердце; ты пришел только для того, чтобы посмотреть на битву.

29– Что же я сделал? – сказал Давид. – Мне что, даже поговорить нельзя?

30Он отвернулся от него к кому-то другому и заговорил о том же самом, и народ отвечал ему, как и прежде. 31Когда слова Давида передали Саулу, он послал за ним. 32Давид сказал Саулу:

– Не падайте духом из-за этого филистимлянина; твой слуга пойдет и сразится с ним.

33Саул ответил:

– Ты не можешь выйти против этого филистимлянина и сразиться с ним; ты всего лишь мальчик, а он – воин с юных лет.

34Но Давид сказал Саулу:

– Твой слуга пас отцовских овец, и когда, бывало, лев или медведь приходил и уносил из отары овцу, 35я гнался за ним, разил его и спасал овцу из его пасти. Когда же он бросался на меня, я хватал его за шерсть, разил и убивал. 36Твой слуга убивал и льва, и медведя. Этот необрезанный филистимлянин уподобится им, потому что он бросил вызов войскам живого Бога. 37Господь, Который избавлял меня от лап льва и медведя, избавит меня от руки и этого филистимлянина.

Саул сказал Давиду:

– Иди, и да будет с тобой Господь!

38Саул одел Давида в свои собственные доспехи. Он надел на него кольчугу и возложил ему на голову бронзовый шлем. 39Давид опоясался мечом поверх доспехов и попробовал ходить в них, так как не привык к этому.

– Я не могу ходить в них, – сказал он Саулу, – потому что я к ним не привык.

И он снял их. 40Взяв в руку посох, он выбрал себе в ручье пять гладких камней, положил их в свою пастушью сумку и с пращей в руке приблизился к филистимлянину.

Давид убивает Голиафа

41Тем временем и филистимлянин со своим щитоносцем приближался к Давиду. 42Когда филистимлянин увидел Давида, румяного и красивого, он с презрением посмотрел на него, потому что тот был всего лишь юноша. 43Он сказал Давиду:

– Разве я – собака, что ты идешь на меня с палками?

И филистимлянин проклял Давида своими богами.

44– Иди сюда, – сказал он, – и я отдам твою плоть небесным птицам и земным зверям!

45Давид сказал филистимлянину:

– Ты идешь против меня с мечом, копьем и дротиком, а я иду против тебя во имя Господа Сил, Бога армий Израиля, которым ты бросил вызов. 46Сегодня Господь отдаст тебя мне, и я сражу тебя и отсеку тебе голову. Сегодня я отдам трупы филистимского войска небесным птицам и земным зверям, и весь мир узнает, что есть Бог в Израиле! 47Все, кто собрался здесь, узнают, что Господь спасает не мечом и не копьем, ведь эта битва – битва Господа, и Он отдаст всех вас в наши руки.

48Когда филистимлянин начал приближаться, чтобы напасть на него, Давид быстро побежал к строю воинов ему навстречу. 49Опустив руку в сумку и вынув камень, он метнул его из пращи и поразил филистимлянина в лоб. Камень вонзился ему в лоб, и он упал лицом на землю. 50Так Давид одержал победу над филистимлянином с помощью пращи и камня. Без меча в руке он сразил филистимлянина и убил его.

51Давид подбежал и встал над ним. Он взял меч филистимлянина и вынул его из ножен. Убив его, он отсек ему голову мечом.

Когда филистимляне увидели, что их герой мертв, они развернулись и побежали. 52Воины Израиля и Иудеи рванулись вперед и преследовали филистимлян до входа в Гат17:52 Так в некоторых древних переводах; в нормативном еврейском тексте: «Гай». и до ворот Экрона. Тела убитых филистимлян были разбросаны вдоль шаараимской дороги, которая вела в Гат и Экрон. 53Вернувшись из погони за филистимлянами, израильтяне разграбили их лагерь. 54Давид взял голову филистимлянина и принес ее в Иерусалим, а оружие филистимлянина он положил у себя в шатре.

Представление Давида Саулу

55Когда Саул смотрел на Давида, идущего навстречу филистимлянину, он спросил Авнера, начальника войска:

– Авнер, чей сын этот юноша?

Авнер ответил:

– Верно, как и то, что ты жив, царь, – я не знаю.

56Царь сказал:

– Узнай, чей сын этот юноша.

57Как только Давид вернулся, убив филистимлянина, Авнер позвал его и привел к Саулу, а Давид все еще держал в руках голову филистимлянина.

58– Чей ты сын, юноша? – спросил его Саул.

Давид ответил:

– Я сын твоего слуги Иессея из Вифлеема.