1 Petro 3 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 3:1-22

Akazi ndi Amuna

1Momwemonso, akazi inu gonjerani amuna anu kuti ngati ena a iwo sakhulupirira Mawu a Mulungu, akopeke ndi makhalidwe a akazi awo ndipo sipadzafunikanso mawu 2pamene aona moyo wanu wachiyero ndi moyo woopa Mulungu. 3Kudzikongoletsa kwanu kusakhale kwa maonekedwe akunja, monga kuluka tsitsi ndi kuvala zokometsera zagolide ndi zovala zamberewere. 4Mʼmalo mwake kudzikongoletsa kwanu kukhale kwa munthu wa mʼkatimo, kukongola kosatha kwa mtima ofatsa ndi mzimu wachete, zimene ndi za mtengowapatali pamaso pa Mulungu. 5Pakuti umo ndi mmene akazi oyera mtima akale amene anali ndi chiyembekezo pa Mulungu anadzikongoletsera. Iwo ankagonjera amuna awo, 6monga Sara, amene anamvera Abrahamu namutcha iye mbuye wake. Akazi inu ndinu ana ake ngati muchita zoyenera, ndipo musaope choopsa chilichonse.

7Momwemonso amuna inu, khalani mwanzeru ndi akazi anu, ndipo muwachitire ulemu monga anzanu ofowoka ndiponso olandira nanu pamodzi mphatso ya moyo wosatha, kuti pasakhale kanthu kotsekereza mapemphero anu.

Kumva Zowawa Chifukwa cha Chilungamo

8Potsiriza, nonse khalani a mtima umodzi, omverana chisoni. Kondanani monga abale, muchitirane chifundo ndi kudzichepetsa. 9Wina akakuchitirani choyipa musabwezere pochitanso choyipa, kapena kubwezera chipongwe akakuchitirani chipongwe, koma muwadalitse. Munayitanidwa kuti mulandire mdalitso. 10Pakuti,

“Iye amene angakonde moyo

ndi kuona masiku abwino,

aletse lilime lake kuyankhula zoyipa,

ndiponso milomo yake kunena mabodza.

11Apewe zoyipa, ndipo azichita zabwino.

Afunefune mtendere ndi kuyesetsa kuwupeza.

12Pakuti Ambuye amayangʼanira bwino anthu olungama

ndipo amatchera khutu ku mapemphero awo.

Koma Ambuye sawayangʼana bwino amene amachita zoyipa.”

13Ndani angakuchitireni zoyipa ngati muchita changu kuchita zabwino? 14Koma ngakhale mumve zowawa chifukwa cha chilungamo, ndinu odala. “Musaope anthu, musachite mantha.” 15Koma lemekezani Khristu mʼmitima mwanu ngati Ambuye wanu. Khalani okonzeka nthawi zonse kuyankha aliyense amene akufunsani za chiyembekezo chimene muli nacho. 16Koma chitani zimenezi mofatsa ndi mwaulemu, mukhale ndi chikumbumtima chosakutsutsani, kuti anthu ena akanena zoyipa za makhalidwe anu abwino mwa Khristu, achite okha manyazi ndi chipongwe chawocho. 17Nʼkwabwino ngati ndi chifuniro cha Mulungu kumva zowawa chifukwa chochita zabwino kusiyana ndi kumva zowawa chifukwa chochita zoyipa. 18Pakuti Khristu anafa chifukwa cha machimo kamodzi kokha kufera onse, wolungama kufera osalungama, kuti akufikitseni kwa Mulungu. Anaphedwa ku thupi koma anapatsidwa moyo mu mzimu. 19Ndipo ali ngati mzimu chomwecho anapita ndi kukalalikira mizimu imene inali mʼndende, 20ya anthu amene sanamvere Mulungu atadikira moleza mtima pa nthawi imene Nowa ankapanga chombo. Mʼchombo chija anthu owerengeka okha, asanu ndi atatu, ndiwo anapulumutsidwa ku madzi. 21Madziwo akufanizira ubatizo umene lero ukukupulumutsaninso, osati chifukwa chochotsa litsiro la mʼthupi koma chifukwa cha chikumbumtima choona pamaso pa Mulungu. Umakupulumutsani chifukwa cha kuuka kwa Yesu Khristu, 22amene anapita kumwamba ndipo ali kudzanja lamanja la Mulungu komwe angelo ndi maulamuliro ndi amphamvu amamvera Iye.

Słowo Życia

1 Piotra 3:1-22

Żony i mężowie

1-2Również wy, żony, bądźcie uległe wobec swoich mężów. Nawet jeśli niektórzy z nich nie są posłuszni słowu Bożemu, dzięki waszej postawie mogą zostać zdobyci dla Boga. Wasze zachowanie—nienaganne i podobające się Bogu—może bowiem przemówić do nich lepiej niż słowa.

3Nie zwracajcie na siebie uwagi fryzurą, biżuterią czy modnymi ubraniami, 4ale pięknem wewnętrznym: łagodnością i pokojem ducha. To piękno nie przemija i ma wielką wartość w oczach Boga. 5Cechy te były ozdobą świętych kobiet, które ufały Bogu i były uległe wobec swoich mężów. 6Jedną z nich była Sara, która okazywała posłuszeństwo Abrahamowi, uznając go za głowę rodziny. Dobrze postępując i niczego się nie obawiając, będziecie do niej podobne.

7Wy zaś, mężowie, okazujcie żonom szacunek i bądźcie wyrozumiali wobec słabej płci, a Bóg będzie wysłuchiwał waszych modlitw. Pamiętajcie, że wasze żony razem z wami otrzymają dar życia wiecznego.

Cierpienie z powodu dobra

8Wszyscy bądźcie jednomyślni, pełni współczucia, przyjacielskiej miłości i pokory. 9Nie odpłacajcie złem za zło i nie obrażajcie tych, którzy was obrażają. Przeciwnie—tym, którzy was krzywdzą, życzcie szczęścia. Was samych Bóg również obdarzył bowiem szczęściem. 10Pismo mówi:

„Ten, kto chce być szczęśliwy i cieszyć się życiem,

niech przestanie grzeszyć mową oraz kłamać.

11Niech odwróci się od zła i czyni dobro.

Niech szuka tego, co prowadzi do pokoju,

i niech do niego dąży.

12Pan troszczy się bowiem o prawych

i wysłuchuje ich modlitw.

Odwraca się natomiast od tych, którzy czynią zło”.

13Czy ktoś będzie chciał was skrzywdzić, jeśli z całych sił będziecie czynić dobro? 14A jeśli nawet tak by się stało, to i tak będziecie szczęśliwi. Nie dajcie się więc nikomu zastraszyć ani zaniepokoić, 15ale z całego serca oddawajcie chwałę Chrystusowi, naszemu Panu. Gdy inni będą was pytać o źródło waszej nadziei, bądźcie gotowi, aby dać im odpowiedź. 16Czyńcie to jednak łagodnie, z szacunkiem i bez złych intencji. W ten sposób zawstydzicie bowiem tych, którzy oczerniają was z powodu waszej wierności Chrystusowi. 17Lepiej jest bowiem cierpieć, jeśli taka jest wola Boga, z powodu dobrego postępowania niż z powodu popełnionego zła.

Wartość cierpienia

18Chrystus również doznał cierpień—raz na zawsze płacąc za ludzkie grzechy. Był niewinny, ale cierpiał za winnych, aby pojednać was z Bogiem. Poniósł fizyczną śmierć, ale został ożywiony przez Ducha.

19W mocy tego Ducha głosił dobrą nowinę duchom ludzi, zamkniętym w więzieniu. 20Dawno temu, gdy Noe budował okręt, ludzie ci nie okazali posłuszeństwa Bogu, choć On cierpliwie na to czekał. W okręcie tym uratowało się więc przed potopem tylko osiem osób. 21Teraz takim ratunkiem jest chrzest. On zbawia was nie dlatego, że w wodzie oczyszczacie wasze ciało z brudu, ale dlatego, że prosicie Boga o czyste sumienie. Wszystko to jest możliwe dzięki Jezusowi Chrystusowi, który zmartwychwstał 22i wstąpił do nieba, a teraz przebywa po prawej stronie Boga i stoi ponad wszystkimi aniołami, władcami tego świata, a także duchowymi mocami.