1 Petro 2 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 2:1-25

1Choncho, lekani zoyipa zonse, chinyengo chilichonse, chiphamaso, nsanje ndi kusinjirira kulikonse. 2Monga makanda obadwa kumene amalirira mkaka, inunso muzilakalaka mkaka weniweni wauzimu, kuti mukule ndi kukufikitsani ku chipulumutso chanu, 3pakuti tsopano mwalawadi kuti Ambuye ndi wabwino.

Mwala wa Moyo ndi Anthu Osankhidwa

4Pamene mukubwera kwa Iye, amene ndi Mwala wa moyo, umene anthu anawukana, koma Mulungu anawusankha kuti ndi wa mtengowapatali, 5inunso, mukhale ngati miyala ya moyo yoti Mulungu amangire nyumba yake yauzimu kuti mukhale ansembe opatulika, opereka nsembe zauzimu zovomerezeka ndi Mulungu mwa Yesu Khristu. 6Pakuti mʼMalemba mwalembedwa kuti,

“Taonani, ndikuyika mwala wa maziko mu Ziyoni,

wosankhika ndi wamtengowapatali.

Amene akhulupirira Iye

sadzachititsidwa manyazi.”

7Tsono kwa inu okhulupirira, mwalawo ndi wamtengowapatali. Koma kwa amene sakhulupirira,

“Mwala umene amisiri anawukana

wasanduka mwala wa maziko,

8ndi

“Mwala wopunthwitsa anthu

ndiponso thanthwe limene limagwetsa anthu.”

Iwo amapunthwa chifukwa samvera uthenga, pakuti ichi ndiye chinali chifuniro cha Mulungu pa iwo.

9Koma inu ndinu anthu osankhidwa ndi Mulungu, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu ake enieni a Mulungu, munasankhidwa kuti mulalikire za ntchito zamphamvu za Iye amene anakuyitanani kuti mutuluke mu mdima ndi kulowa mʼkuwunika kwake kodabwitsa. 10Kale simunali anthu ake, koma tsopano ndinu anthu a Mulungu. Kale simunalandire chifundo, koma tsopano mwalandira chifundo.

11Okondedwa, ndikukupemphani, ngati alendo pansi pano, pewani zilakolako za uchimo, zimene zimachita nkhondo ndi moyo wanu. 12Khalani moyo wabwino pakati pa anthu osapembedza kuti ngakhale atakusinjirirani kuti mumachita zoyipa, iwowo akaona ntchito zanu zabwino, adzalemekeza Mulungu pa tsiku lomwe Iye adzatiyendere.

Kugonjera Olamulira

13Gonjerani maulamuliro onse chifukwa cha Ambuye. Kaya ndi mfumu, imvereni chifukwa ili ndi ulamuliro waukulu, 14kaya ndi mabwanamkubwa, pakuti watumidwa ndi mfumu kuti alange onse amene amachita zoyipa ndi kuyamikira onse amene amachita zabwino. 15Pakuti Mulungu akufuna kuti pochita ntchito zabwino muthetse kuyankhula mosazindikira ndi mopusa. 16Mukhale monga mfulu, koma musagwiritse ntchito ufulu wanuwo ngati chophimbira zoyipa; mukhale monga atumiki a Mulungu. 17Chitirani ulemu aliyense, kondani abale okhulupirira, wopani Mulungu, ndipo chitirani mfumu ulemu.

Akapolo

18Inu akapolo, gonjerani ambuye anu ndi kuwachitira ulemu, osati kwa iwo okha amene ndi abwino ndi omvetsa zinthu, komanso kwa amene ndi ankhanza. 19Pakuti ndi chinthu chokoma ngati munthu apirira mu zowawa zimene sizinamuyenera chifukwa chodziwa kuti Mulungu alipo. 20Kodi pali choti akuyamikireni ngati mupirira pomenyedwa chifukwa choti mwalakwa? Koma ngati mumva zowawa chifukwa chochita zabwino ndi kupirira, mwachita choyamikika pamaso pa Mulungu. 21Munayitanidwa kudzachita zimenezi, chifukwa Khristu anamva zowawa chifukwa cha inu, anakusiyirani chitsanzo, kuti inu mutsatire mʼmapazi ake.

22“Iye sanachite tchimo

kapena kunena bodza.”

23Pamene anthu ankamuchita chipongwe, Iye sanabwezere chipongwe, pamene Iye ankamva zowawa, sanaopseze. Mʼmalo mwake, anadzipereka kwa Mulungu amene amaweruza molungama. 24Iye mwini anasenza machimo athu mʼthupi lake pa mtanda, kuti ife tife kutchimo ndi kukhala ndi moyo potsata chilungamo, ndipo ndi mabala ake munachiritsidwa. 25Pakuti munali monga nkhosa zosochera, koma tsopano mwabwerera kwa mʼbusa ndi woyangʼanira miyoyo yanu.

Słowo Życia

1 Piotra 2:1-25

1Dlatego porzućcie wszelką złość, fałsz, obłudę, zazdrość i obmawianie innych. 2Jako nowo narodzone niemowlęta pragnijcie czystego, duchowego mleka, które pomoże wam dojrzewać w wierze i osiągnąć zbawienie. 3Sami bowiem przekonaliście się, że Pan jest dobry.

Żywe kamienie i lud wybrany

4Przyjdźcie do Chrystusa, który jest żywym kamieniem, odrzuconym wprawdzie przez ludzi, ale wybranym przez Boga i bardzo cennym. 5Wy również jesteście żywymi kamieniami, z których powstaje duchowy dom. Jesteście świętymi kapłanami, którzy—dzięki Jezusowi Chrystusowi—składają duchowe ofiary, podobające się Bogu. 6Pismo mówi bowiem:

„Kładę na górze Syjon kamień węgielny

—wybrany i bardzo cenny.

Ten, kto mu uwierzy,

nie zawiedzie się”.

7Dla was, którzy Mu wierzycie, jest on bardzo cenny. Dla niewierzących jest On natomiast:

„Kamieniem odrzuconym przez budujących,

który stał się kamieniem węgielnym,

8ale

także kamieniem, o który się potkną,

i skałą, z powodu której upadną”.

Niewierzący nie są posłuszni słowu Bożemu, więc potykają się i upadają—takie jest ich przeznaczenie. 9Wy natomiast zostaliście wybrani przez Boga. Jesteście więc kapłanami Króla, świętym narodem i Bożą własnością. Dlatego macie opowiadać innym o tym, jak wspaniały jest Bóg, który wyprowadził was z ciemności i pokazał wam swoje cudowne światło.

10Dawniej nie należeliście do Boga, ale teraz staliście się Jego ludem. Wcześniej nie mieliście też pojęcia o Jego miłości, a teraz doświadczacie jej.

11Kochani, wzywam was, abyście nie poddawali się pragnieniom waszego ciała, które szkodzą duszy. Pamiętajcie, że nie należycie do tego świata i jesteście tu tylko cudzoziemcami. 12Będąc wśród pogan, zachowujcie się nienagannie. Gdy bowiem nadejdzie dzień powrotu Pana, nie będą już niesłusznie was oskarżać, ale przypomną sobie wasze dobre czyny i będą wielbić Boga.

Posłuszeństwo wobec władzy

13Ze względu na Pana, bądźcie poddani wszelkiej ludzkiej władzy: zarówno głowie państwa, 14jak i urzędnikom państwowym. Ich zadaniem jest bowiem karanie przestępców, a nagradzanie dobrych obywateli.

15Jeśli będziecie czynić dobro—a tego oczekuje od was Bóg—to ci, którzy są nierozumni i nie znają prawdy, nie będą mieli podstaw do oskarżania was. 16Postępujcie jak ludzie naprawdę wolni, dla których wolność nie jest jedynie przykrywką do czynienia zła. Zachowujcie się jednak jak niewolnicy Boga. 17Szanujcie wszystkich ludzi, kochajcie wierzących, miejcie respekt dla Boga, ale okazujcie także szacunek głowie państwa.

18Niewolnicy, szanujcie i słuchajcie swoich panów—nie tylko dobrych i wyrozumiałych, ale także złych. 19Bóg obdarza bowiem swoją łaską tych, którzy niewinnie cierpią za to, że są Mu posłuszni. 20Co to za zaszczyt, jeśli cierpicie z powodu swojego grzechu? Jeśli jednak cierpicie z powodu waszego dobrego postępowania, to Bóg obdarzy was swoją łaską. 21On powołał was bowiem właśnie do takiego życia, dlatego Chrystus—cierpiąc za was—zostawił wam wzór do naśladowania.

22On nie popełnił żadnego grzechu i nigdy nie skłamał.

23Gdy Go znieważano, nie odpowiadał zniewagą, a gdy zadawano Mu cierpienia, nie odgrażał się. Powierzył się bowiem Bogu, który jest sprawiedliwym sędzią. 24On sam wziął na siebie ciężar naszych grzechów i zaniósł je na krzyż. Uczynił to, aby uwolnić nas od win i dać nam moc do nowego, prawego życia. To dzięki Jego ranom zostaliście uleczeni! 25Byliście bowiem jak zabłąkane owce, ale teraz wróciliście do Pasterza i Opiekuna waszych dusz.