1 Petro 2 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 2:1-25

1Choncho, lekani zoyipa zonse, chinyengo chilichonse, chiphamaso, nsanje ndi kusinjirira kulikonse. 2Monga makanda obadwa kumene amalirira mkaka, inunso muzilakalaka mkaka weniweni wauzimu, kuti mukule ndi kukufikitsani ku chipulumutso chanu, 3pakuti tsopano mwalawadi kuti Ambuye ndi wabwino.

Mwala wa Moyo ndi Anthu Osankhidwa

4Pamene mukubwera kwa Iye, amene ndi Mwala wa moyo, umene anthu anawukana, koma Mulungu anawusankha kuti ndi wa mtengowapatali, 5inunso, mukhale ngati miyala ya moyo yoti Mulungu amangire nyumba yake yauzimu kuti mukhale ansembe opatulika, opereka nsembe zauzimu zovomerezeka ndi Mulungu mwa Yesu Khristu. 6Pakuti mʼMalemba mwalembedwa kuti,

“Taonani, ndikuyika mwala wa maziko mu Ziyoni,

wosankhika ndi wamtengowapatali.

Amene akhulupirira Iye

sadzachititsidwa manyazi.”

7Tsono kwa inu okhulupirira, mwalawo ndi wamtengowapatali. Koma kwa amene sakhulupirira,

“Mwala umene amisiri anawukana

wasanduka mwala wa maziko,

8ndi

“Mwala wopunthwitsa anthu

ndiponso thanthwe limene limagwetsa anthu.”

Iwo amapunthwa chifukwa samvera uthenga, pakuti ichi ndiye chinali chifuniro cha Mulungu pa iwo.

9Koma inu ndinu anthu osankhidwa ndi Mulungu, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu ake enieni a Mulungu, munasankhidwa kuti mulalikire za ntchito zamphamvu za Iye amene anakuyitanani kuti mutuluke mu mdima ndi kulowa mʼkuwunika kwake kodabwitsa. 10Kale simunali anthu ake, koma tsopano ndinu anthu a Mulungu. Kale simunalandire chifundo, koma tsopano mwalandira chifundo.

11Okondedwa, ndikukupemphani, ngati alendo pansi pano, pewani zilakolako za uchimo, zimene zimachita nkhondo ndi moyo wanu. 12Khalani moyo wabwino pakati pa anthu osapembedza kuti ngakhale atakusinjirirani kuti mumachita zoyipa, iwowo akaona ntchito zanu zabwino, adzalemekeza Mulungu pa tsiku lomwe Iye adzatiyendere.

Kugonjera Olamulira

13Gonjerani maulamuliro onse chifukwa cha Ambuye. Kaya ndi mfumu, imvereni chifukwa ili ndi ulamuliro waukulu, 14kaya ndi mabwanamkubwa, pakuti watumidwa ndi mfumu kuti alange onse amene amachita zoyipa ndi kuyamikira onse amene amachita zabwino. 15Pakuti Mulungu akufuna kuti pochita ntchito zabwino muthetse kuyankhula mosazindikira ndi mopusa. 16Mukhale monga mfulu, koma musagwiritse ntchito ufulu wanuwo ngati chophimbira zoyipa; mukhale monga atumiki a Mulungu. 17Chitirani ulemu aliyense, kondani abale okhulupirira, wopani Mulungu, ndipo chitirani mfumu ulemu.

Akapolo

18Inu akapolo, gonjerani ambuye anu ndi kuwachitira ulemu, osati kwa iwo okha amene ndi abwino ndi omvetsa zinthu, komanso kwa amene ndi ankhanza. 19Pakuti ndi chinthu chokoma ngati munthu apirira mu zowawa zimene sizinamuyenera chifukwa chodziwa kuti Mulungu alipo. 20Kodi pali choti akuyamikireni ngati mupirira pomenyedwa chifukwa choti mwalakwa? Koma ngati mumva zowawa chifukwa chochita zabwino ndi kupirira, mwachita choyamikika pamaso pa Mulungu. 21Munayitanidwa kudzachita zimenezi, chifukwa Khristu anamva zowawa chifukwa cha inu, anakusiyirani chitsanzo, kuti inu mutsatire mʼmapazi ake.

22“Iye sanachite tchimo

kapena kunena bodza.”

23Pamene anthu ankamuchita chipongwe, Iye sanabwezere chipongwe, pamene Iye ankamva zowawa, sanaopseze. Mʼmalo mwake, anadzipereka kwa Mulungu amene amaweruza molungama. 24Iye mwini anasenza machimo athu mʼthupi lake pa mtanda, kuti ife tife kutchimo ndi kukhala ndi moyo potsata chilungamo, ndipo ndi mabala ake munachiritsidwa. 25Pakuti munali monga nkhosa zosochera, koma tsopano mwabwerera kwa mʼbusa ndi woyangʼanira miyoyo yanu.

Slovo na cestu

1. Petrův 2:1-25

1A tak se zbavujte všech špatných vlastností, návyků a pocitů. Mezi ně patří nečestnost, závist, pomluvy a přetvářka. 2Jste jako nemluvňátka nově narozená pro Boží rodinu. Jako se nemluvně dožaduje mléka, tak i vy byste se měli živit Božím slovem – číst je a přemýšlet o něm, abyste rostli ve víře a k spáse. 3Vždyť jste už na sobě poznali Boží dobrotivost.

Živý kámen a vyvolení lidé

4Přicházejte ke Kristu, kameni živému, který byl lidmi zavržen, ale před Bohem je vyvolený a vzácný. 5I vy buďte živými kameny, z nichž se staví duchovní dům. Nadto vám Kristus vydobyl právo, abyste mohli jako kněží bezprostředně přistupovat k Bohu. Přinášejte mu tedy duchovní oběti vašeho čistého života, které rád přijme pro zásluhy Ježíše Krista. 6Písmo o tom hovoří takto:

„Posílám Krista jako pečlivě vybraný,

vzácný základní kámen mé církve a nikdy nezklamu ty,

kdo v něho věří.“

7Ano, vám, kteří věříte, je velmi drahý, ale nevěřícím jsou určena tato slova Písma:

„Stavitelé zavrhli kámen,

který se stal základním kamenem.

Pro ně je kamenem,

o nějž klopýtnou,

a skálou,

která způsobí jejich pád.“

8Svým vzdorem vůči Božímu slovu na sebe přivolávají to, co Bůh předem řekl, svůj úplný pád. 9Ale vy jste vyvoleni samým Bohem jako kněží Krále, jste svatí a čistí, jste jeho vlastní lid. To vše pro to, abyste svědčili druhým o tom, který vás povolal ze tmy do svého úžasného světla. 10Dříve jste nebyli ničím, nyní jste Božím lidem. Dříve jste nevěděli o Boží dobrotě, a nyní proměnila vaše životy.

Chování Božího lidu v utrpení

11Prosím vás, moji milí, žijte na tomto světě jako hosté. Váš skutečný domov je nyní v nebi, proto se zřekněte zlých přání, která ohrožují váš život s Kristem. 12Mezi nevěřícími se chovejte vždy správně. I když o vás mluví jako o nejhorších lidech, nakonec, uvidí-li vaše dobré jednání, mohou být při druhém příchodu Ježíše Krista mezi zachráněnými.

13-14Jako věřící respektujte představitele své země. Mají povinnost stíhat všechny, kdo činí zlo, a odměňovat ty, kteří jednají dobře. 15Bůh si přeje, abyste svým příkladným životem umlčeli kritiku těch, kteří odsuzují Boží zvěst, třebaže nevědí, co jim přináší, a aniž zakusili její moc. 16Jste svobodní lidé, neznamená to však, že máte svobodu k činění zla. Pro vás je vždy směrodatná Boží vůle. 17S každým jednejte s úctou, mějte rádi své spoluvěřící, žijte v uctivé poslušnosti před Bohem a vládu mějte ve vážnosti.

18Respektujte své nadřízené, nejen když jsou k vám mírní a laskaví, ale i když jsou přísní a tvrdí. 19Je to přednost, když někdo pro věrnost Bohu snáší utrpení neprávem. 20Vždyť co je na tom záslužného, snášíte-li trest, který je vám spravedlivě vyměřen? Ale když jednáte správně, a přece za to trpíte, Bůh to ocení. 21Taková utrpení jsou jen částí toho, co zakusil pro nás Kristus, který se v tom stal naším příkladem. Proto ho následujte! 22On nikdy nezhřešil, nikdy nevyslovil lež; 23snášel urážky, ale sám neurážel; když trpěl, nehrozil, ale ponechával vše Bohu, který soudí spravedlivě. 24On sám nesl naše hříchy na sobě, když zemřel na kříži, aby nám dal sílu skoncovat s hříchem a žít novým životem. Jeho utrpením jsme byli uzdraveni. 25Byli jste jako ovce, které zabloudily, ale nyní jste navráceni ke svému pastýři a strážci.